< Salmos 92 >

1 Es bueno alabar al Señor y hacer melodía a tu nombre, ¡oh Altísimo!
Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
2 Para declarar tu misericordia en la mañana, y tu fe inmutable todas las noches;
Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
3 En un instrumento de diez cuerdas, y música de arpa.
kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
4 Porque tú, oh Jehová, me has agradado por tus obras; Tendré alegría en la obra de tus manos.
Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
5 ¡Oh Señor, qué grandes son tus obras! y tus pensamientos son muy profundos.
Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
6 Un hombre sin sentido no tiene conocimiento de esto; y un hombre necio no puede asimilarlo.
Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
7 Cuando los pecadores se levantan como la hierba, y todos los que hacen mal florecen, es para que su fin sea la destrucción eterna.
kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
8 Pero tú, oh Señor, estás en lo alto para siempre.
Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
9 Para ver! tus enemigos, oh Señor, morirán; todos los hacedores del mal serán esparcidos;
Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 Pero mi fuerzas aumentan como las del búfalo; el mejor aceite fluye sobre mi cabeza.
Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 Mis ojos han visto problemas en mis enemigos; mis oídos tienen noticias del destino de los malhechores que se han enfrentado a mí.
Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
12 El hombre bueno será como un árbol alto en su fuerza; su crecimiento será como los árboles que se extienden en el Líbano.
Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 Los plantados en la casa del Señor subirán altos y fuertes en sus jardines.
odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 Darán fruto aun cuando sean viejos; serán fértiles y llenos de crecimiento;
Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 Para anunciar que el Señor es recto; él es mi Roca, no hay engaño en él.
kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

< Salmos 92 >