< Salmos 78 >

1 Escucha, oh mi pueblo, a mi ley; deja que tus oídos se inclinen a las palabras de mi boca.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 Abriendo mi boca voy a dar una historia, incluso los dichos oscuros de los viejos tiempos;
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 Que han venido a nuestro oído y a nuestro conocimiento, tal como nos fueron dados por nuestros padres.
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 No los mantendremos en secreto de nuestros hijos; aclararemos a la generación venidera las alabanzas del Señor y su fortaleza, y las grandes obras de asombro que ha hecho.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 Puso un testigo en Jacob, e hizo una ley en Israel; que él dio a nuestros padres para que pudieran darles conocimiento de ellos a sus hijos;
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 Para que la generación venidera pueda tener conocimiento de ellos, incluso de los hijos del futuro, que les den a conocer a sus hijos;
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 Para que pongan su esperanza en Dios, y no dejen que las obras de Dios se salgan de sus mentes, sino que guarden sus leyes;
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 y no sean como sus padres, una generación dura e incontrolada; una generación cuyo corazón era duro, cuyo espíritu no era fiel a Dios.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 Los hijos de Efraín, armados con arcos, volvieron las espaldas en el día de la pelea.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 No fueron gobernados por la palabra de Dios, y no quisieron ir en el camino de su ley;
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 Dejaron sus obras fuera de su memoria, y las maravillas que les había hecho ver.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 Hizo grandes obras delante de sus padres, en la tierra de Egipto, en los campos de Zoán.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 El mar fue cortado en dos para que pudieran pasar; las aguas se juntaron de lado a lado.
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 Durante el día los guiaba en la nube, y durante toda la noche con una luz de fuego.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 Las rocas del desierto fueron quebradas por su poder, y él les dio a beber como de las aguas profundas.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 Hizo salir arroyos de la peña; y las aguas descender como ríos.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 Y siguieron pecando contra él aún más, apartándose del Altísimo en el desierto;
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 Probando a Dios en sus corazones, pidiendo carne por su deseo.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 Dijeron palabras crueles contra Dios, diciendo: ¿Puede Dios preparar una mesa en el desierto?
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Mira, la roca fue cortada por su poder, por lo que el agua salió corriendo, y arroyos desbordantes; ¿él puede darnos pan? ¿es capaz de obtener carne para su gente?
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Así que estas cosas vinieron a oídos del Señor, y él se enojó; y se encendió un fuego contra Jacob, y vino la ira contra Israel;
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 Porque no tenían fe en Dios, ni esperanza en su salvación.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 Y dio órdenes a las nubes en lo alto, y las puertas del cielo estaban abiertas;
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 Y envió como lluvia de maná, y les dio el grano del cielo.
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 El hombre tomó parte en el alimento de los ángeles; les envió carne en toda su medida.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Envió un viento del este del cielo, impulsando el viento del sur con su poder.
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 Envió carne sobre ellos como el polvo, y aves emplumadas como la arena del mar,
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 Y él dejó que baje a su lugar de descanso, alrededor de sus tiendas.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 Así que tenían comida y estaban llenos; porque él les dio su deseo;
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 Pero no se apartaron de sus deseos; y mientras la comida todavía estaba en sus bocas,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 Vino sobre ellos la ira de Dios, y mató a los más robustos, y acabó con los jóvenes de Israel.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 Por todo esto siguieron pecando aún más, y no tuvieron fe en sus grandes maravillas.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 Así que sus días fueron desperdiciados como un aliento, y sus años en problemas.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 Cuando les mandó la muerte, lo buscaron; entonces se volvían a él buscándolo con cuidado;
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 Entonces se acordaban que Dios era su Roca, y el Dios Altísimo su salvador.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 Pero sus labios y lengua le eran falsos;
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 Y sus corazones no estaban bien con él, y no guardaron su pacto con él.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 Pero él, lleno de piedad, tiene perdón por el pecado, y no pone fin al hombre: frecuentemente retracta su ira, y no se enoja violentamente.
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 Así que tuvo en cuenta que ellos eran solo carne; un aliento que se va rápidamente, y no volverá.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 ¡Con qué frecuencia iban contra él en el desierto. y le daban motivo de aflicción en el desierto!
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Otra vez pusieron a Dios a prueba, y le dieron dolor al Santo de Israel.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 No tuvieron en cuenta el trabajo de su mano, ni el día en que los quitó del poder de sus enemigos;
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 cómo hizo sus señales en Egipto, y sus maravillas en el campo de Zoán;
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 De modo que sus ríos se convirtieron en sangre, y no pudieron beber de sus arroyos.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 Envió diferentes tipos de moscas entre ellos, envenenando su carne; y ranas para su destrucción.
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 El dio el aumento de sus campos a los gusanos, los frutos de su industria a los saltamontes.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 Envió hielo para la destrucción de sus vides; sus árboles fueron dañados por el frío glacial.
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 Hielo fue llovido sobre su ganado; tormentas eléctricas enviaron destrucción entre las bandadas.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Envió sobre ellos el ardor de su ira, su amargo disgusto, y liberó ángeles malvados entre ellos.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 Dejó que su ira se saliera con la suya; él no retuvo su alma de la muerte, sino que dio su vida a la enfermedad.
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 Él dio a la destrucción a todos los primeros hijos de Egipto; los primeros frutos de su fuerza en las tiendas de Cam;
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 Pero él tomó a su pueblo como ovejas, y los guió en la tierra desolada como un rebaño.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 Los llevó a salvo para que no tuvieran miedo; pero sus enemigos estaban cubiertos por el mar.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 Y él fue su guía a su tierra santa, hasta el monte que su diestra había hecho suyo;
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 Expulsando naciones delante de ellos, marcando la línea de su herencia, y dando a las personas de Israel sus tiendas para un lugar de descanso.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 Pero ellos se amargaron contra el Dios Altísimo, lo probaron y no guardaron sus leyes;
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 Sus corazones se volvieron atrás y falsos como sus padres; fueron convertidos a un lado como un arco retorcido.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 Le enojaron con sus altares paganos; adorando ídolos, lo provocaron a celos.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 Cuando esto llegó a oídos de Dios, se enojó mucho y abandonó a Israel por completo;
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 Y se fué del lugar santo en Silo, la tienda que había puesto entre los hombres;
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 Y permitió que sus enemigos capturaran él símbolo de su poder y gloria.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 Él entregó a su pueblo a la espada, y se enojó con su pueblo.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Sus jóvenes fueron quemados en el fuego; y sus vírgenes no fueron alabadas en la canción de la novia.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 Sus sacerdotes fueron muertos a espada, y sus viudas no lloraron por ellos.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Entonces el Señor era como el que se despierta del sueño, y como un hombre fuerte que clama por el vino.
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 Sus enemigos fueron rechazados por sus golpes y avergonzados para siempre.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Y puso la tienda de José a un lado, y no tomó la tribu de Efraín;
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 Pero él tomó la tribu de Judá para sí, y el monte de Sión, en el cual tuvo placer.
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 E hizo su lugar santo como el alto cielo, como la tierra que él fija para siempre.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 Tomó a David para que fuera su siervo, y lo llevó del lugar de las ovejas;
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 De cuidar las ovejas que daban leche, lo llevó a dar de comer a Jacob su pueblo, y a Israel su heredad.
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 Y David cuido del pueblo de Dios. Los cuido y dirigió con mano hábil y corazón sincero.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

< Salmos 78 >