< Salmos 25 >
1 A ti, oh SEÑOR, mi alma enaltece.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 Oh Dios mío, he puesto mi fe en ti, no me avergüences; no permitas que mis enemigos se glorien sobre mí.
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 No se avergüence ningún siervo tuyo que en ti confía; serán avergonzados aquellos que se rebelan sin causa.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Muéstrame tus caminos, oh Señor; enséñame tus senderos.
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Sé mi guía y maestro de la manera verdadera; porque tú eres el Dios de mi salvación; Estoy esperando tu palabra todo el día.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Oh Señor, ten en cuenta tu compasión y tus misericordias; que son perpetuas.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 No tengas en cuenta mis pecados cuando era joven, o mi maldad: deja que tu recuerdo de mí esté lleno de misericordia, oh Señor, por tu gran amor y bondad.
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Bueno y justo es el Señor: entonces él enseñará a los pecadores el camino.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Y guía para los pobres en espíritu: enseñará a los mansos el camino.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Todos los caminos del Señor son misericordia y verdad para aquellos que mantienen su pacto y su testimonio.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Por tu nombre, oh Señor, permíteme tener perdón por mi pecado, que es muy grande.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Si un hombre tiene temor del Señor, el Señor le enseñará el camino que debe seguir,
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 gozará de bienestar, y su simiente tendrá la tierra por su herencia.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 La comunión íntima de Jehová es con los que le temen, con aquellos en cuyo corazón está el temor de él; y a ellos hará conocer su pacto.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Mis ojos se vuelven al Señor todo el tiempo; porque él sacará mis pies de la red.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Mírame Señor ten misericordia de mí; porque estoy solo y preocupado.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Los problemas de mi corazón aumentan: Oh sácame de mis dolores.
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Mira mi penas y mi dolor; y perdona todos mis pecados.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Mira cómo aumentan los que están en mi contra, con su odio violento me aborrecen.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Guarda mi alma, y arráncame fuera de peligro; no me avergüences, porque he puesto mi fe en ti.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Que mis caminos limpios y rectos me protejan, porque mi esperanza está en ti.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Dale a Israel salvación, oh Dios, de todas sus angustias.
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!