< Salmos 145 >
1 Déjame glorificarte, oh Dios, mi Rey; y bendecir tu nombre por los siglos de los siglos.
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Todos los días te daré bendición, alabando tu nombre por los siglos de los siglos.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Grande es el Señor, y muy digno de alabanza; su poder excede nuestro entendimiento.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Una generación tras otra alabarán tus grandes actos y dejarán en claro el funcionamiento de tu fortaleza.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 Mis pensamientos serán del honor y la gloria de tu gobierno y de la maravilla de tus obras.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 Los hombres hablarán del poder y temor de tus actos; Daré noticias de tu gloria.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Sus dichos estarán llenos del recuerdo de toda tu misericordia, y ellos harán canciones de tu justicia.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 El Señor está lleno de gracia y compasión; lento para enojarse, pero grande en misericordia.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 El Señor es bueno con todos los hombres; y sus misericordias son sobre todas sus obras.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Todas las obras de tus manos te alaban, oh Señor; y tus santos te dan bendición.
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 Sus palabras serán de la gloria de tu reino y de sus palabras sobre tu fortaleza;
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 Para que los hijos de los hombres conozcan sus actos de poder y la gran gloria de su reino.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Tu reino es un reino eterno, y tu gobierno es por todas las generaciones.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 El Señor es el sostén de todos los que caen y el levanta a todos los oprimidos.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Los ojos de todos los hombres te esperan; y les das su comida a su tiempo.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Con la apertura de tu mano, todo ser vivo tiene su deseo en toda su plenitud.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 El Señor es recto en todos sus caminos, y amable en todas sus obras.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 El Señor está cerca de todos los que le dan honor a su nombre; de todos los que le dan honor con verdaderos corazones.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 A sus adoradores, les dará su deseo; su clamor llega a sus oídos, y él les da salvación.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 El Señor guardará a todos sus adoradores del peligro; pero él enviará destrucción a todos los pecadores.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 Mi boca alabará al Señor; que todos bendigan su santo nombre por los siglos de los siglos.
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.