< Salmos 115 >

1 No a nosotros, oh Señor, no a nosotros, sino a tu nombre démosle gloria, por tu misericordia y tu fe inmutable.
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 ¿Por qué dirán las naciones: Dónde está ahora su Dios?
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 Mas nuestro Dios está en el cielo; hizo todo lo que le agradaba.
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 Sus imágenes son plata y oro, obra de manos de hombres.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 Tienen bocas, pero no voz; tienen ojos, pero no ven;
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 Tienen oídos, pero no oyen; tienen narices, pero no tienen olfato;
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 Tienen manos sin más no palpan. y pies sin poder de caminar; y ningún sonido sale de su garganta.
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 Los que los hacen son como ellos; y también lo es cada uno que pone su fe en ellos.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 Israel, ten fe en el Señor; él es tu ayuda y tu coraza.
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 Casa de Aarón, ten fe en el Señor; él es tu ayuda y tu escudo.
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Adoradores del Señor, ten fe en el Señor; él es tu ayuda y tu escudo.
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 El Señor nos ha tenido en cuenta y nos dará su bendición; él enviará bendiciones sobre la casa de Israel y sobre la casa de Aarón.
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 Él enviará bendiciones sobre los adoradores del Señor, sobre los pequeños y sobre los grandes.
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 Que el Señor les dé a ustedes y a sus hijos un mayor aumento.
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Que tengas la bendición del Señor, que hizo el cielo y la tierra.
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Los cielos son del Señor; pero la tierra la ha dado a los hijos de los hombres.
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Los muertos no alaban al Señor; o aquellos que descienden al inframundo.
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 Pero alabaremos al Señor ahora y para siempre. Alabado sea el Señor.
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.

< Salmos 115 >