< Salmos 114 >
1 Cuando Israel salió de Egipto, los hijos de Jacob de un pueblo cuyo idioma les era extraño;
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Judá se convirtió en su lugar santo, e Israel su reino.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 El mar lo vio y se fue en vuelo; Jordan fue rechazado.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 Las montañas saltaban como cabras, y las pequeñas colinas como corderos.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 ¿Qué te sucedió, oh mar, que fuiste a volar? O Jordan, que fuiste devuelto?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Ustedes montañas, ¿por qué saltaron como cabras, y sus pequeñas colinas como corderos?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Sé ha turbado, tierra, delante de Jehová, delante del Dios de Jacob;
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 Que hizo la roca en un manantial de agua, y la piedra dura en una fuente.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.