< Salmos 106 >
1 Dejen que el Señor sea alabado. Alaben al Señor, porque él es bueno; porque su misericordia es inmutable para siempre.
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 ¿Quién puede dar cuenta de los grandes actos del Señor, o dejar en claro toda su alabanza?
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 Felices son aquellos cuyas decisiones son rectas, y el que hace justicia todo el tiempo.
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Recuerda, oh Señor, cuando eres bueno con tu pueblo; Oh, deja que tu salvación venga a mí;
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 Para que pueda ver el bienestar de las personas de tu elección y participe en la alegría de tu nación y enorgullezca de tu herencia.
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 Somos pecadores como nuestros padres, hemos hecho mal, nuestros actos son malos.
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Nuestros padres no pensaron en tus maravillas en Egipto; ellos no guardaron en la memoria la gran cantidad de tus misericordias, sino que te dieron motivos para la ira en el mar, incluso en el Mar Rojo.
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 Pero él era su salvador a causa de su nombre, para que los hombres pudieran ver su gran poder.
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 Por su palabra, el mar Rojo se secó, y él los llevó por las aguas profundas como a través del desierto.
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 Y los tomó a salvo de las manos de sus enemigos, y los mantuvo lejos de los ataques de los que estaban contra ellos.
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 Y las aguas pasaron sobre sus enemigos; todos ellos llegaron a su fin.
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 Entonces tuvieron fe en su palabra; ellos le dieron canciones de alabanza.
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 Pero el recuerdo de sus obras fue breve; no esperando ser guiado por él,
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 Ellos dieron paso a sus malos deseos en la tierra baldía, y pusieron a Dios a prueba en el desierto.
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 Y él les dio su pedido, pero envió una enfermedad devastadora en sus almas.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 Estaban llenos de envidia contra Moisés en las tiendas, y contra Aarón, el santo del Señor.
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 La apertura de la tierra puso fin a Datán, cubriendo a Abiram y su banda.
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 Y se encendió un fuego entre sus tiendas; los pecadores fueron quemados por las llamas.
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Hicieron un becerro en Horeb, y adoraron a una imagen de oro.
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 Y su gloria fue transformada en imagen de buey, cuyo alimento es hierba.
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 No tenían memoria de Dios su salvador, que había hecho grandes cosas en Egipto;
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 Obras de maravilla en la tierra de Ham, y cosas de miedo en el Mar Rojo.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 Y él se proponía poner fin a ellos si Moisés, su siervo especial, no se hubiera levantado delante de él, entre él y su pueblo, haciendo retroceder su ira, para guardarlos de la destrucción.
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Estaban disgustados con la buena tierra; no tenían fe en su palabra;
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 Hablando contra él secretamente en sus tiendas, no escucharon la voz del Señor.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 Entonces les juró que los exterminaría en la tierra baldía.
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 para que sus hijos se mezclen entre las naciones, y sean enviados a otras tierras.
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Y se juntaron con Baal-peor, y tomaron parte en las ofrendas a los muertos.
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 Entonces lo enojaron por su comportamiento; y él envió enfermedad sobre ellos.
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Entonces se levantó Finees y oró por ellos; y la enfermedad no se expandió.
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 Y todas las generaciones que vinieron después de él guardaban para siempre el recuerdo de su justicia.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 E hicieron enojar a Dios otra vez en las aguas de Meriba, y Moisés se angustió por causa de ellos;
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 Porque ellos hicieron amargar su espíritu, y él dijo cosas impías.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 No pusieron fin a los pueblos, como el Señor había dicho;
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 Pero se unieron a las naciones, aprendiendo sus obras.
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 Y adoraron a las imágenes; que eran un peligro para ellos:
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 Incluso hicieron ofrendas de sus hijos y sus hijas a espíritus malignos,
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 Y dieron la sangre de sus hijos y de sus hijas que no habían hecho mal, ofreciéndolas a las imágenes de Canaán; y la tierra quedó contaminada con sangre.
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 Y se contaminaron con sus obras, yendo tras sus malos deseos.
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 Entonces la ira del Señor ardió contra su pueblo, y él se enojó contra su heredad.
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 Y él los entregó en manos de las naciones; y fueron gobernados por sus enemigos.
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 Por ellos fueron aplastados, y humillados bajo sus manos.
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Una y otra vez los hizo libres; pero sus corazones se volvieron contra su propósito, y fueron vencidos por sus pecados.
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Pero cuando su clamor llegó a sus oídos, tuvo piedad de su problema:
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 Y tuvo en cuenta su acuerdo con ellos, y en su gran misericordia les dio el perdón.
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 Él puso lástima en los corazones de aquellos que los hicieron prisioneros.
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Sé nuestro Salvador, Señor Dios nuestro, y nos volvamos a reunir de entre las naciones, para que glorifiquemos tu santo nombre y nos gloriamos en tu alabanza.
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Alabado sea el Señor Dios de Israel por los siglos de los siglos; y que toda la gente diga: que así sea. Alaba al Señor.
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.