< Proverbios 1 >

1 Palabras sabias de Salomón, hijo de David, rey de Israel.
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 Para tener conocimiento de la enseñanza sabia; para ser claro acerca de las palabras de la razón:
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 Para ser entrenado en los caminos de la sabiduría, en la rectitud y en juzgar el comportamiento verdadero y recto:
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 Para hacer sagaces a los ingenuos, y para darle al joven conocimiento, y un propósito serio:
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 El hombre sabio, al escuchar, obtendrá un mayor aprendizaje, y los actos del hombre de buen sentido serán guiados sabiamente:
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 Para obtener el sentido de dichos sabios, y de las palabras de los sabios y sus dichos secretos.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 El temor del Señor es el comienzo del conocimiento; pero los necios no tienen uso para la sabiduría y la enseñanza.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Hijo mío, presta oído al entrenamiento de tu padre, y no abandones la enseñanza de tu madre:
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 Porque serán corona de gracia para tu cabeza, y adornos de cadenas alrededor de tu cuello.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Hijo mío, si los pecadores te sacarán del camino correcto, no vayas con ellos.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 Si dicen: Ven con nosotros; hagamos designios contra el bien, esperando en secreto a los rectos, sin causa;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Los tragaremos vivos a los hombres rectos, como se traga la muerte a quienes caen en el sepulcro; (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 Los bienes de gran precio serán nuestros, nuestras casas estarán llenas de riqueza;
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Aproveche tu oportunidad con nosotros, y todos tendremos una bolsa de dinero:
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Hijo mío, no vayas con ellos; mantén tus pies alejados de sus caminos:
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Porque sus pies corren tras el mal, y se apresuran a quitarle la vida a un hombre.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 En verdad, para nada sirve la red extendida ante los ojos del pájaro:
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 Y están secretamente esperando su sangre y preparándose destrucción para sí mismos.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Tal es el destino de todos los que van en busca de ganancias; le quita la vida a sus dueños.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 La sabiduría está clamando en la calle; su voz es fuerte en los lugares abiertos;
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 Sus palabras están sonando en los lugares de reunión, y en las puertas de la ciudad:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 ¿Hasta cuándo, ustedes simples, las cosas necias serán queridas para ustedes? y es un placer para los que odian la autoridad? ¿Cuánto tiempo los tontos seguirán odiando el conocimiento?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Vuélvanse a mis correcciones: mira, enviaré el flujo de mi espíritu sobre ustedes, y les haré saber mis palabras.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Porque tus oídos estaban cerrados a mi voz; nadie prestó atención a mi mano estirada;
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 Ustedes rechazaron mis consejos, y no tendrían nada que ver con mis correcciones:
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 En el día de tu angustia me reiré; Y me burlaré de tu miedo;
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 Cuando te sobreviene tu temor, como tormenta, y tu angustia como viento impetuoso; cuando el dolor y la tristeza vienen sobre ti.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Entonces no daré respuesta a sus clamores; buscándome temprano, no me verán:
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Porque aborrecieron el conocimiento, y no entregaron sus corazones al temor de Jehová:
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 No deseaban mi enseñanza, y mis palabras de protesta no fueron nada para ellos.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Así que el fruto de su camino será su alimento, y con los designios de sus corazones se llenarán.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Porque el retorno de lo simple de la enseñanza será la causa de su muerte, y la paz de los necios será su destrucción.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Pero el que me escuchará tomará su descanso a salvo, viviendo en paz sin temor al mal.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Proverbios 1 >