< Proverbios 9 >
1 La sabiduría hizo su casa, levantando sus siete pilares.
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 Ella ha puesto sus bestias gordas a la muerte; su vino está mixto, su mesa está lista.
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 Ella ha enviado a sus sirvientas; su voz sale a los lugares más altos de la ciudad, diciendo:
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 Él que sea simple, que entre aquí; y al que no tiene sentido, ella dice:
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 Ven, toma de mi pan y de mi vino mezclado.
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 Renuncia a los simples y ten vida, y sige el camino del conocimiento.
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
7 El que enseña a un hombre de orgullo se avergüenza a sí mismo; el que corrige a un pecador recibe un mal nombre.
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
8 No reprendas a un hombre orgulloso, o él te odiará; corrige a un hombre sabio, y tu serás querido por él.
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
9 Da enseñanza a un hombre sabio, y él se hará más sabio; da entrenamiento a un hombre recto, y su aprendizaje se incrementará.
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
10 El temor del Señor es el comienzo de la sabiduría, y el conocimiento del Santo da una mente sabia.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
11 Porque en mí aumentarán tus días, y los años de tu vida serán largos.
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
12 Si eres sabio, eres sabio para ti mismo; si tu corazón está lleno de orgullo, solo tendrás el dolor de ello.
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
13 La mujer necia está llena de ruido; ella no tiene ningún sentido en absoluto.
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
14 Sentada a la puerta de su casa, en los altos del pueblo,
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
15 y clamando a los que pasan, yendo en su camino, dice:
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
16 Cualquiera que sea simple, que entre aquí; y al que es sin sentido, ella dice:
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
17 La bebida tomada sin derecho es dulce, y la comida en secreto es agradable.
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
18 Pero él no ve que los muertos están allí, que sus invitados están en los lugares profundos del inframundo. (Sheol )
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )