< Proverbios 8 >

1 ¿No está la sabiduría clamando, y la voz de la inteligencia sonando?
Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 En la parte superior de las autopistas, en la intersección de las carreteras, ella toma su lugar;
Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
3 Cuando los caminos entran a la ciudad, se hace oír su grito, en las puertas su voz es fuerte:
Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 A ustedes les llamo, oh hombres; mi voz llegue a los hijos de los hombres.
Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
5 Conviértanse en expertos en la razón, ¡oh, simples! ustedes tontos, tomen el entrenamiento de corazón.
Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Escuchen, porque mis palabras son verdaderas, y mis labios están abiertos para dar a conocer lo recto.
Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 Porque la buena fe sale de mi boca, y los labios falsos me repugnan.
Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 Todas las palabras de mi boca son justicia; no hay nada falso o retorcido en ellas.
Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 Todas ellas son verdad a cuya mente está despierta, y directas para aquellos que obtienen conocimiento.
Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Toma mi enseñanza, y no plata; obtén conocimiento en lugar del mejor oro.
Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 Porque la sabiduría es mejor que las joyas, y todas las cosas que se desean no son nada en comparación con ella.
Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 Yo, la sabiduría, he convertido la conducta sabia en mi pariente cercano; Me ven como el amigo especial de los propósitos sabios.
Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 El temor del Señor se ve al odiar el mal: el orgullo, una alta opinión de uno mismo, el mal camino y la falsa lengua, me son desagradables.
Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 El diseño inteligente y el buen sentido son míos; la razón y la fuerza son mías.
Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 A través de mí los reyes tienen su poder, y los gobernantes dan las decisiones correctas.
Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 A través de mí, los jefes tienen autoridad, y los nobles juzgan en justicia.
Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 Los que me han dado su amor son amados por mí, y aquellos que me buscan con cuidado me hallarán.
Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 La riqueza y el honor están en mis manos, incluso la riqueza sin igual y la justicia.
Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 Mejor es mi fruto que el oro, que el mejor oro; y mi aumento es más deseado que la plata.
Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 En el camino de la justicia voy, en el camino de los juicios justos,
Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 pues daré a los que me aman riquezas por su herencia, haciendo llenas sus tiendas.
Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
22 El Señor me hizo el comienzo de su camino, la primera de sus obras en el pasado.
“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
23 Desde los días eternos, me fue dado mi lugar, desde el nacimiento de los tiempos, antes que la tierra fuese.
Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
24 Cuando no había fondo, me dieron a luz, cuando no había fuentes que fluyeran con agua.
Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
25 Antes que pusiera los montes en su lugar, antes de que nacieran las colinas,
Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
26 cuando no había hecho la tierra, ni los campos, ni el polvo del mundo.
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
27 Cuando preparó los cielos, yo estaba allí: cuando puso un arco sobre la faz del abismo:
Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
28 Cuando hizo fuertes los cielos arriba: cuando las fuentes del abismo se fijaron:
pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
29 Cuando puso un límite al mar, para que las aguas no vayan en contra de su palabra: cuando puso en posición las bases de la tierra:
pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
30 Entonces yo estaba a su lado, como un maestro de obras; y yo era su deleite día tras día, tocando delante de él en todo el tiempo;
Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
31 Jugando en su tierra; y mi deleite fue con los hijos de los hombres.
Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
32 Escúchenme, hijos míos, porque son felices los que guardan mis caminos.
“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Tomen ustedes mi enseñanza y háganse sabio; no la dejen ir.
Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
34 Bienaventurado el hombre que me presta atención, mirando a mis puertas día tras día, manteniendo su lugar junto a las columnas de mi casa.
Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
35 Porque él que me recibe, obtiene vida, y la gracia del Señor vendrá a él.
Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 Pero él que se aparta de mí, hace mal a su alma: todos mis enemigos están enamorados de la muerte.
Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”

< Proverbios 8 >