< Proverbios 7 >

1 Hijo mío, cumple mis palabras y deja que mis reglas estén guardadas en tu mente.
Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
2 Guarda mis reglas y tendrás vida; deja que mi enseñanza sea para ti como la luz de tus ojos;
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Déjalos moslos fijar en tus dedos, y grabados en tu corazón.
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Di a la sabiduría: Tú eres mi hermana; que el conocimiento se llame tu amigo especial:
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 para que te guarden de la mujer adúltera, de la mujer extraña de palabras seductoras.
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 Mirando desde mi casa, y mirando por la ventana,
Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
7 vi entre los jóvenes inexpertos, a uno más necio que todos.
Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
8 Caminando en la calle cerca del recodo de su camino, yendo hacia la casa de ella,
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9 Al anochecer, en el tarde del día, en la oscuridad negra de la noche.
Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 Y la mujer salió a él, con el vestido de una mujer prostituta, con un corazón astuto;
Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 Ella es una mujer ligera y sin escrúpulos; sus pies no se quedan en su casa.
(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 Ahora está en la calle, ahora en los espacios abiertos, esperando en las esquinas.
Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 Entonces ella lo tomó de su mano, y lo besó, y sin vergüenza ella le dijo:
Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 Tengo un banquete de ofrendas de paz, porque hoy mis juramentos han sido efectuados.
“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 Así que salí con la esperanza de conocerte, buscándote con cuidado, y ahora te tengo a ti.
Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 Mi cama está cubierta con cojines de costura, con telas de colores del hilo de algodón de Egipto;
Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 He hecho mi cama dulce con perfumes y especias.
Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 Venga, disfrutemos de nuestro placer en el amor hasta la mañana, teniendo gozo en las delicias del amor.
Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 Porque el dueño de la casa se aleja en un largo viaje:
Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
20 Ha tomado una bolsa de dinero con él; él regresará a la luna llena.
Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 Con sus bellas palabras ella lo venció, lo convenció con sus labios seductores.
Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 El hombre necio va tras ella, como un buey que va a morir, como un ciervo tirado por una cuerda;
Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 Como un pájaro cayendo en una red; sin pensar que su vida está en peligro, hasta que una flecha entra en su costado.
mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 Ahora, mis hijos, escúchenme; presten atención a los dichos de mi boca;
Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
25 No vuelvas tu corazón a sus caminos, no vayas siguiendo sus pasos.
Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
26 Porque los heridos y humillados por ella son numerosos; y todos los que han muerto a través de ella son un gran ejército.
Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Su casa es el camino al inframundo, bajando a las salas de la muerte. (Sheol h7585)
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)

< Proverbios 7 >