< Proverbios 28 >

1 El malvado huye cuando ningún hombre lo persigue, pero los rectos no tienen miedo, como el león.
Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
2 Debido al pecado de la tierra, sus problemas aumentan; pero por un hombre de sabiduría y conocimiento serán apagados como un fuego.
Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
3 Un hombre rico que es cruel con los pobres es como una lluvia violenta que causa destrucción de alimentos.
Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
4 Los que no respetan la ley alaban al malhechor; pero tales que guardan la ley están en contra de él.
Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
5 Los hombres malvados no tienen conocimiento de lo que es correcto; pero los que van tras el Señor tienen conocimiento de todas las cosas.
Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
6 Mejor es el pobre cuyos caminos son rectos, que el hombre rico cuyos caminos no son rectos.
Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
7 El que guarda la ley es hijo sabio, pero el que se hace compañía de los glotones avergüenza a su padre.
Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
8 El que hace que su riqueza sea más grande al tomar interés, solo lo junta para el que tiene compasión de los pobres.
Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
9 En cuanto al hombre que aparta su oído para no oír la ley, incluso su oración es desagradable.
Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
10 Cualquiera que haga que los rectos vayan errantes por el mal camino, él mismo descenderá al hoyo que él ha hecho; pero los rectos tendrán buenas cosas para su herencia.
Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
11 El hombre de riqueza parece ser sabio en su opinión, pero el pobre que tiene sentido tiene una baja opinión de él.
Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
12 Cuando los rectos hacen bien, hay gran gloria; pero cuando los malhechores son levantados, los hombres se esconden.
Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
13 El que guarda sus pecados en secreto no hará bien; pero el que está abierto acerca de ellos y los abandona, obtendrá misericordia.
Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
14 Feliz es el hombre en quien está el temor del Señor en todo momento; pero aquel cuyo corazón es duro entrará en problemas.
Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
15 Como un león de voz fuerte y un oso errante, es un malvado gobernante sobre un pueblo pobre.
Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
16 El príncipe que no tiene sentido es un gobernante cruel; pero el que no desea obtener ganancias por sí mismo tendrá una vida larga.
Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
17 Alguien que ha sido la causa de la muerte de un hombre irá en vuelo al sepulcro: que ningún hombre le dé ayuda.
Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
18 Aquel cuyos caminos son rectos estará a salvo, pero repentina será la caída de aquel cuyos caminos están torcidos.
Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
19 Al arar su tierra, un hombre tendrá pan en toda su medida; pero el que persigue a los holgazanes será lo suficientemente pobre.
Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
20 Un hombre de buena fe tendrá una gran bendición, pero uno que intenta obtener riqueza rápidamente no quedará libre del castigo.
Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
21 No es bueno tener respeto por la posición de un hombre: porque un hombre hará lo malo por un poco de pan.
Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
22 El que siempre desea riqueza, corre tras el dinero, y no ve la necesidad vendrá sobre él.
Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
23 El que dice palabras de protesta a un hombre tendrá más aprobación que uno que diga palabras alabadoras con su lengua.
Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
24 El que toma de su padre o de su madre lo que es suyo por derecho, y dice: No es pecado; es lo mismo que un tomador de vida.
Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
25 El que siempre desea ganancias, es causa de pelea; pero el que pone su fe en el Señor prosperará.
Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
26 El que tiene fe en sí mismo es necio; pero todos los que caminan sabiamente estarán a salvo.
Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
27 El que da al pobre nunca tendrá necesidad, pero grandes maldiciones caerán sobre el que no les presta atención.
Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
28 Cuando los malhechores son levantados, los hombres se esconden; pero cuando la destrucción los alcanza, aumentan los justos.
Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

< Proverbios 28 >