< Proverbios 2 >
1 Hijo mío, lleva mis palabras a tu corazón, guardando mis leyes en tu mente;
Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 Para que tu oído preste atención a la sabiduría, y tu corazón se convierta en conocimiento.
ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 Verdaderamente, si clamas por el buen sentido, y tu pedido es por conocimiento;
ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 Si la estás buscando como plata, y buscándola como riqueza almacenada;
ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 Entonces el temor de Jehová será claro para ti, y el conocimiento de Dios será tuyo.
ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6 Porque el Señor da sabiduría; de su boca salen el conocimiento y la razón:
Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7 Él tiene la salvación almacenada para los rectos, él es un pectoral para aquellos en quienes no hay maldad;
Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8 Vigila los caminos que son correctos, y cuida a los que le temen.
pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9 Entonces conocerás la justicia y la rectitud, y la conducta recta, incluso de todo buen camino.
Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 Porque la sabiduría entrará en tu corazón, y el conocimiento agradará a tu alma;
Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 Los propósitos sabios te cuidarán, y el conocimiento te mantendrá;
Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12 Te da la salvación del hombre malo, de aquellos cuyas palabras son falsas;
Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
13 Que dejan el camino de la justicia, para andar por caminos oscuros;
amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
14 Quienes se complacen en la maldad, y se complacen en los malos designios del pecador;
amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 Cuyos caminos no son rectos, y cuyos pasos se vuelven malvados:
Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16 Para sacarte del poder de la mujer extraña, que dice palabras seductoras;
Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 ¿Quién es falsa con el marido de sus primeros años, y no tiene en cuenta el acuerdo con Dios?
amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 Porque su casa está en camino a la muerte; sus pasos descienden a las sombras:
Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 Los que van a ella no vuelven; sus pies no se mantienen en los caminos de la vida:
Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
20 para que puedas seguir el camino de los hombres buenos, y seguir los pasos de los rectos.
Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 Porque los rectos vivirán en la tierra, y los buenos la tendrán por heredad.
Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 Pero los pecadores serán cortados de la tierra, y aquellos cuyos actos son falsos serán desarraigados.
Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.