< Números 6 >

1 Y él Señor dijo a Moisés:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Di a los hijos de Israel: Si un hombre o una mujer hace un juramento para mantenerse separado, voto de nazareo; y entregarse al Señor;
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri,
3 Debe mantenerse alejado del vino y las bebidas fuertes, y no debe tomar vino mezclado o bebida fuerte o cualquier bebida hecha de uvas, u otras uvas, verdes o secas.
sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma.
4 Siempre que esté separado, no puede tomar nada hecho de la vid, desde sus semillas hasta su piel.
Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’
5 Todo el tiempo que esté bajo su juramento no permita que ninguna navaja sea sobre su cabeza; hasta que los días mientras él está separado terminen, él es santo y su cabello no puede ser cortado.
“‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’
6 Mientras esté separado, no podrá acercarse a ningún cadáver.
Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo.
7 No puede ser inmundo por su padre o su madre, su hermana o su hermano, si les llega la muerte; porque está bajo un juramento de mantenerse separado para Dios.
Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake.
8 Todo el tiempo que él está separado, él es santo para el Señor.
Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.
9 Si la muerte llega repentinamente a un hombre a su lado, su cabeza es contaminada, deje que se le corte el pelo el día en que se limpie, el séptimo día.
“Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri.
10 Y al octavo día, que se dirija al sacerdote, a la puerta de la tienda de la reunión, con dos palomas o dos tórtolas;
Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano.
11 Y el sacerdote dará uno por la ofrenda por el pecado y el otro por la ofrenda quemada para quitar el pecado que vino sobre él a causa de los muertos, y santificara la cabeza ese mismo día.
Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.
12 Y le dará al Señor sus días de estar separados, ofreciendo un cordero del primer año como ofrenda por la culpa del pecado: pero los días anteriores serán anulados, porque se volvió impuro por cuanto fue contaminado su nazareato.
Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.
13 Y esta es la ley para el que está separado, cuando se terminan los días necesarios: debe venir a la puerta de la tienda de la reunión,
“Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
14 Ofrecerá su ofrenda al Señor; un cordero del primer año, sin defecto, para una ofrenda quemada, y un cordero hembra del primer año, sin defecto, para la ofrenda por el pecado, y un macho oveja, sin defecto, para las ofrendas de paz,
Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano,
15 Y una canasta de pan sin levadura, panes de la mejor harina mezclada con aceite, y panes delgados sin levadura cubiertos de aceite, con su ofrenda de comida y ofrendas de bebidas.
ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.
16 Y el sacerdote los llevará ante el Señor, y hará su ofrenda por el pecado y su holocausto;
“Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza.
17 Dando las ovejas de las ofrendas de paz, con la canasta de pan sin levadura; y al mismo tiempo, el sacerdote hará su ofrenda de comida y su ofrenda de bebida.
Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.
18 Dejen que su cabello largo, la señal de su juramento, se corte en la puerta de la Tienda de la reunión, y que lo ponga en el fuego donde arden las ofrendas de paz.
“Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
19 Y el sacerdote sacará de la canasta la pata cocida de la oveja y una torta sin levadura y una torta fina, y las pondrá en las manos del nazareo después de que se haya cortado su cabello.
“Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija.
20 Meciéndose como una ofrenda mecida ante el Señor; esto es santo para el sacerdote, junto con el pecho y la pierna levantada; Después de eso, el hombre puede tomar vino.
Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.
21 Esta es la ley para el que hace un juramento de mantenerse separado, y por su ofrenda al Señor por ese motivo, además de lo que puede obtener; esta es la ley de su juramento, que tendrá que cumplir.
“Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”
22 Y él Señor dijo a Moisés:
Yehova anawuza Mose kuti,
23 Diles a Aarón y a sus hijos: Estas son las palabras de bendición que ustedes deben usar para bendecir a los hijos de Israel; diles a ellos,
“Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,
24 Que el Señor te envíe su bendición y te guarde:
“‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
25 Que la luz del rostro del Señor brille sobre ti y tenga de ti misericordia;
Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
26 Que él favor del Señor descanse sobre ti y que te dé paz.
Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’”
27 Y ​​pondrán mi nombre sobre los hijos de Israel, y yo les daré mi bendición.
Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.

< Números 6 >