< Números 36 >

1 Y vinieron a Moisés los jefes de las familias de los hijos de Galaad, hijo de Maquir, hijo de Manasés, de las familias de los hijos de José, los jefes y los jefes de familia de los hijos de José. Israel estando presente,
Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
2 Y dijo: El Señor dio órdenes a mi señor para que distribuyera la tierra como su herencia a los hijos de Israel: y el Señor le ordenó a mi señor que entregara la herencia de Zelofehad, nuestro hermano, a sus hijas.
Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
3 Ahora, si se casan con alguno de los hijos de otras tribus de los hijos de Israel, sus propiedades serán retiradas de la herencia de nuestros padres y se convertirán en parte de la herencia de la tribu en la que se unan casándose; y su herencia será quitada de la herencia de nuestra tribu.
Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
4 Y en el momento del jubileo de los hijos de Israel, sus propiedades se unirán a la herencia de la tribu de la que forman parte y serán retiradas de la herencia de la tribu de nuestros padres.
Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
5 Por la dirección del Señor, Moisés dio órdenes a los hijos de Israel, diciendo: Lo que la tribu de los hijos de José ha dicho es correcto.
Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
6 Este es el orden del Señor acerca de las hijas de Zelofehad; El Señor dice: Que tomen como sus esposos a quien mas les agrade, pero solo entre la familia de la tribu de su padre.
Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
7 Y, por lo tanto, ninguna propiedad será entregada de tribu a tribu entre los hijos de Israel; pero cada uno de los hijos de Israel guardará la herencia de la tribu de su padre.
kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
8 Y toda hija que posea bienes en cualquier tribu de los hijos de Israel debe casarse con una de las familias de la tribu de su padre, para que todo hombre de los hijos de Israel pueda conservar la herencia de sus padres.
Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
9 Y ninguna propiedad será entregada de una tribu a otra, sino que cada tribu de los hijos de Israel mantendrá su herencia.
Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
10 Entonces las hijas de Zelofehad hicieron lo que el Señor le ordenó a Moisés:
Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
11 Porque Maala, Tirsa, y Hogla, y Milca, las hijas de Zelofehad, tomaron como esposos a los hijos de los hermanos de su padre.
Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
12 Estuvieron casados ​​con las familias de los hijos de Manasés, el hijo de José, y sus bienes se mantuvieron en la tribu de la familia de su padre.
Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
13 Estas son las leyes y las órdenes que el Señor dio a los hijos de Israel por medio de Moisés, en las tierras bajas de Moab por el Jordán frente a Jericó.
Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.

< Números 36 >