< Lamentaciones 3 >
1 Soy el hombre que ha visto aflicción bajo la vara de su ira.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 Por él he sido llevado a la oscuridad donde no hay luz.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 Verdaderamente contra mí, su mano se ha vuelto una y otra vez todo el día.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 Mi carne y mi piel han sido envejecidas por él y quebrantó mis huesos.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 Él ha levantado una pared contra mí, encerrándome con una amarga pena.
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 Él me ha mantenido en lugares oscuros, como aquellos que han estado muertos hace mucho tiempo.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 Me ha cercado un muro, de modo que no puedo salir; Él ha hecho grande el peso de mi cadena.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 Incluso cuando envío un grito de auxilio, él mantiene mi oración en secreto.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 . Ha levantado un muro de piedras cortadas sobre mis caminos, torció mis caminos.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 Él es como un oso esperándome, como un león en lugares secretos.
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 Por él, mis caminos se desviaron y me hicieron pedazos; me han asolado.
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 Con su arco inclinado, me ha hecho la marca de sus flechas.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 Él ha soltado sus flechas en las partes más internas de mi cuerpo.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 Me he convertido en la burla de todos los pueblos; Soy él objeto de su burla todo el día.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 Él ha hecho de mi vida nada más que dolor, amarga es la bebida que me ha dado.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 Por él, mis dientes se rompieron con piedras trituradas, y me cubrió de ceniza.
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 Mi alma es enviada lejos de la paz, no tengo más recuerdos del bien.
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 Y dije: Mi fuerza ha perecido, y mi esperanza en él Señor.
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 Ten en cuenta mi aflicción, mi vagar, el ajenjo y la amargura.
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 Mi alma aún guarda el recuerdo de ellos; y se humilla dentro de mí.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 Esto lo tengo en mente, y por eso tengo esperanza.
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 Es a través del amor del Señor que no hemos llegado a la destrucción, porque sus misericordias no tienen límites.
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 Son nuevas cada mañana; grande es su fidelidad.
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 Me dije: El Señor es mi herencia; y por eso tendré esperanza en él.
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 El Señor es bueno para los que lo esperan, para el alma que lo está buscando.
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 Es bueno seguir esperando y esperando tranquilamente la salvación del Señor.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 Es bueno que un hombre se someta al yugo cuando es joven.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 Déjalo que se siente solo, sin decir nada, porque él Señor se lo ha puesto.
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 Que ponga su boca en el polvo, si por casualidad puede haber esperanza.
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Vuelva su rostro hacia el que le da golpes; que se llene de vergüenza.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 Porque el Señor no da para siempre al hombre.
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 Porque aunque él envíe dolor, aun así tendrá lástima en toda la medida de su amor.
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 Porque no le agrada afligir y causar dolor a los hijos de los hombres.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 Aplastar bajo sus pies a todos los prisioneros de la tierra,
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 Privar del derecho de un hombre ante el Altísimo.
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 Defraudar a un hombre en su demanda, el Señor no le place.
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 ¿Quién puede decir una cosa y darle efecto si no ha sido ordenado por el Señor?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 ¿No sale mal y bien de la boca del Altísimo?
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 ¿Qué protesta puede hacer un hombre vivo, incluso un hombre sobre el castigo de su pecado?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 Hagamos una reflexión pongamos a prueba nuestros caminos, volviéndonos nuevamente al Señor;
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Levantando nuestros corazones con nuestras manos a Dios en los cielos.
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 Hemos hecho lo malo y hemos ido contra tu ley; No hemos tenido tu perdón.
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 Cubriéndonos con ira, nos perseguiste, has matado, no perdonado;
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 Cubriéndose con una nube, para que la oración no pase.
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 Nos has hecho como basura y desecho entre los pueblos.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 Las bocas de todos nuestros enemigos se abren contra nosotros.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 El temor y trampas han venido sobre nosotros, desolación y destrucción.
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Ríos de agua corren de mis ojos, por la destrucción de la hija de mi pueblo.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 Mis ojos están llorando sin parar, no tienen descanso,
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 Hasta que el Señor nos mire, hasta que vea mi problema desde cielo.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Mis ojos contristaron mi alma, por lo ocurrido a las hijas de mi pueblo.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 Los que están contra mí sin causa me persiguen como si fuera un pájaro;
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 Han puesto fin a mi vida en la prisión, pusieron piedra sobre mi.
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 Aguas cubrieron mi cabeza; Dije, estoy muerto.
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 Estaba orando a tu nombre, oh Señor, desde la prisión más baja.
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 Mi voz vino a ti; Que no se te cierre el oído a mi clamor, a mi llanto.
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Llegaste el día en que te hice mi oración: dijiste: No temas.
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 Oh Señor, has tomado la causa de mi alma, has salvado mi vida.
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 Oh Señor, has visto mi mal; sé juez en mi causa.
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 Has visto todas las malas recompensas que me han enviado, y todos sus planes contra mí.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 Sus amargas palabras han llegado a tus oídos, oh Señor, y todos sus planes contra mí;
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 Los labios de los que subieron contra mí, y sus pensamientos contra mí todo el día.
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Toman nota de ellos cuando están sentados y cuando se levanten; Yo soy su objeto de burla.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 Les darás su recompensa, Señor, respondiendo a la obra de sus manos.
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 Dejarás que sus corazones se endurezcan con tu maldición sobre ellos.
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 Irás tras ellos con ira y les pondrás fin desde debajo de los cielos del Señor.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.