< Jueces 12 >

1 Entonces los hombres de Efraín se reunieron, tomaron las armas y se dirigieron a Zafon; y dijeron a Jefté: ¿Por qué fuiste a hacer la guerra contra los hijos de Amón sin enviarnos a que fuéramos contigo? Ahora pondremos tu casa en llamas sobre ti.
Gulu la nkhondo la fuko la Efereimu linayitanidwa ndipo anawolokera ku Zafoni nakafunsa Yefita kuti, “Nʼchifukwa chiyani unawoloka kukachita nkhondo ndi Aamoni osatiyitana kuti tipite nawe? Ife tikutenthera mʼnyumba mwakomu.”
2 Y Jefté les dijo: Yo y mi gente estábamos en peligro, y los hijos de Amón fueron muy crueles con nosotros, y cuando envié por ti, no me diste ninguna ayuda contra ellos.
Yefita anayankha kuti, “Ine ndi anthu anga tinakangana kwambiri ndi Aamoni. Ndinakuyitanani koma inu simunandipulumutse mʼmanja mwawo.
3 Entonces, cuando vi que no tenía ayuda de ti, arriesgue mi propia vida y fui contra los hijos de Amón, y el Señor los puso en mis manos. ¿por qué has venido ¿Este día para hacerme la guerra?
Nditaona kuti simundithandiza, ndinayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndinawoloka kukachita nkhondo ndi a Aamoni. Yehova anandithandiza ndipo ndinawagonjetsa. Nanga nʼchifukwa chiyani mwabwera kwa ine lero kuti muchite nane nkhondo?”
4 Entonces Jefté reunió a todos los hombres de Galaad e hizo la guerra a Efraín; y los hombres de Galaad vencieron a Efraín.
Choncho Yefita anasonkhanitsa anthu a ku Giliyadi ndi kuchita nkhondo ndi Aefereimu. Ndipo Agiliyadi anagonjetsa Aefereimu chifukwa Aefereimuwo amati, “Inu a Giliyadi ndinu othawa kuchokera ku Efereimu ndi pakati pa Amanase.”
5 Y los de Galaad tomaron los lugares de cruce del Jordán contra los efraimitas; y cuando alguno de los hombres de Efraín que había salido huyendo les pedía paso; Los hombres de Galaad le preguntaban: ¿Eres tú un efraimita? Y si él respondía: No;
Choncho Agiliyadi analanda Aefereimu madooko a mtsinje wa Yorodani. Munthu aliyense wothawa ku Efereimu amati akanena kuti, “Ndiloleni ndiwoloke,” Agaliyadi ankafunsa kuti, “Kodi ndiwe mu Efurati?” Ngati iye ayankha kuti, “Ayi”
6 Entonces le dijeron: Ahora, di Shibolet; y él dijo Sibolet, y no pudo decirlo de la manera correcta; luego lo tomaron y lo mataron en los cruces del Jordán; y en ese momento fueron ejecutados cuarenta y dos mil efraimitas.
Ndiye amamuwuza kuti, “Nena kuti ‘Shiboleti.’” Tsono munthuyo akanena kuti Siboleti popeza samatha kutchula bwino mawuwa, ankamugwira ndi kumupha pomwepo pa madooko a mtsinje wa Yorodani. Nthawi imeneyo anaphedwa Aefereimu 42,000.
7 Y Jefté fue juez de Israel por seis años. Y Jefté, el galaadita, murió, y lo enterraron en su pueblo, Mizpa de Galaad.
Yefita anatsogolera Israeli zaka zisanu ndi chimodzi. Kenaka Yefita wa ku Giliyadi anamwalira, ndipo anayikidwa mu mzinda wake ku Giliyadi.
8 Y después de él, Ibzán de Belén fue juez de Israel.
Atamwalira Yefita, Ibizani wa ku Betelehemu anatsogolera Israeli.
9 Tuvo treinta hijos y treinta hijas a quienes envió a otros lugares, y obtuvo treinta esposas de otros lugares para sus hijos. Y fue juez de Israel por siete años.
Iye anali ndi ana aamuna makumi atatu ndi ana aakazi makumi atatu. Anakwatitsa ana ake akaziwo kwa anthu a fuko lina, ndipo ana ake aamuna aja anawabweretsera atsikana makumi atatu kuti awakwatire amenenso anali a fuko lina. Ibizani anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 Y murió Ibzán, y lo enterraron en Belén.
Kenaka Ibizani anamwalira, ndipo anayikidwa mu Betelehemu.
11 Y después de él, Elón, el zebulonita, fue juez de Israel; y fue juez de Israel durante diez años.
Iye atamwalira, Eloni wa fuko la Zebuloni anakhala mtsogoleri wa Aisraeli, ndipo anatsogolera Aisraeli kwa zaka khumi.
12 Y murió Elón el zebulonita, y lo enterraron en Ajalón, en la tierra de Zabulón.
Kenaka Eloni anamwalira ndipo anayikidwa ku Ayaloni mʼdziko la Zebuloni.
13 Y después de él, Abdón, hijo de Hilel, de piratón, fue juez de Israel.
Iye atamwalira, Abidoni mwana wa Hilelo wochokera ku Piratoni, anatsogolera Israeli.
14 Tuvo cuarenta hijos y treinta nietos cada uno de los cuales montaba un asno; y fue juez de Israel durante ocho años.
Iye anali ndi ana aamuna makumi anayi ndi zidzukulu makumi atatu, amene ankakwera pa abulu 70. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi zitatu.
15 Y murió Abdón, el hijo de Hillel, y lo enterraron en Piratón, en la tierra de Efraín, en la región montañosa de los amalecitas.
Ndipo Abidoni mwana wa Hilelo Mpiratoni uja anamwalira, nayikidwa ku Piratoni, mʼdziko la Efereimu, dziko lamapiri la Aamaleki.

< Jueces 12 >