< Job 35 >

1 Respondió Eliu, y dijo:
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 ¿Te parece correcto decir, mi justicia es más que la de Dios,
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 ? Porque dijiste: ¿Qué me beneficia a mí y qué provecho tengo por no haber pecado?
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 Te responderé a ti y a tus amigos:
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Vuelvan sus ojos a los cielos, y entiendan que los cielos son más altos que ustedes.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 Si has hecho mal, ¿eso no le afecta a Dios? y si tus pecados son grandes en número, ¿qué es para él?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 Si eres recto, ¿qué le das a él? ¿O qué toma él de tu mano?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 Tu maldad puede tener un efecto en un hombre como tú, o tu justicia aprovechara un hijo de hombre.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 Por la abundancia de la violencia, los hombres claman en dolor; piden ayuda a causa del brazo de los poderosos.
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 Pero nadie ha dicho: ¿Dónde está Dios mi Hacedor, que da canciones en la noche?
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 Quién nos da más conocimiento que las bestias de la tierra, y nos hace más sabios que las aves del cielo.
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Allí están clamando por el orgullo de los malhechores, pero él no les responde.
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Pero Dios no escuchará lo que es falso, ni la mirará el Omnipotente.
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Cuánto menos cuando dices que no lo ves; Esperalo, la causa está delante de él.
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 Y ahora que no ha visitado en su ira; ni se conoce con rigor.
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 Y la boca de Job está abierta de par en par para dar lo que es sin beneficio, aumentando las palabras sin conocimiento.
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

< Job 35 >