< Job 3 >

1 Entonces, abriendo su boca y maldiciendo el día de su nacimiento,
Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 Job dijo:
Ndipo Yobu anati:
3 Perezca el día de mi nacimiento y la noche en que se dijo: Un niño es concebido.
“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
4 Que ese día, hubiera sido oscuro; y Dios no hubiera tomado nota de esto desde lo alto, y no hubiera resplandecido la luz del día;
Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
5 Deja que la oscuridad y la noche negra sea su redentor; deja que se cubra con una nube; Deja que las sombras oscuras del día te envíen miedo.
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
6 En cuanto a esa noche que la oscuridad espesa la tome; Que no tenga gozo entre los días del año; Que no venga en el número de los meses.
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
7 En cuanto a esa noche, que hubiera sido estéril; Que ninguna voz de alegría hubiera sonado en ella;
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
8 Que la maldigan los que ponen una maldición en el día; que están listos para despertar a Leviatán.
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
9 Sean oscuras sus estrellas de la mañana; Que esté buscando luz, pero que no la tenga; Que no vea los rayos del alba.
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 Porque no cerró las puertas del vientre de mi madre, ni oculto los problemas de mis ojos.
Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
11 ¿Por qué la muerte no me tomó cuando salí del cuerpo de mi madre, por qué no, cuando salí del vientre, entregue mi espíritu?
“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 ¿Por qué hubo rodillas que me recibieron o por qué los pechos para que me den leche?
Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 Porque entonces podría haber ido a mi descanso en silencio, y en el sueño, haber estado en paz,
Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 Con los reyes y los sabios de la tierra, que edificaron grandes casas para sí mismos;
pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 O con los gobernantes que tenían oro, y cuyas casas estaban llenas de plata;
pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 O como un aborto de niño que nunca podría haber existido; Como niños pequeños que no han visto la luz.
Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 Allí dejan de perturbar los malvados, y aquellos cuyas fuerzas han llegado a su fin tienen descanso.
Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 Allí los prisioneros están en paz juntos. La voz del capataz no vuelve a sus oídos.
A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 El pequeño y el grande están allí, y el siervo está libre de su amo.
Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
20 ¿Por qué le da luz al que está en problemas, y la vida al alma amarga;
“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 Para aquellos cuyo deseo es la muerte, pero no viene; que la buscan más que la riqueza secreta;
kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 ¿Que se alegran con gran gozo y se regocijan cuando llegan a su último lugar de descanso;
amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
23 Pporque se le da luz a un hombre que no sabe por donde va, y que está acorralado por Dios?
Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 En lugar de mi comida tengo pena, y de mí salen gritos de dolor como agua.
Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 Porque lo que estaba temiendo ha venido sobre mi y de lo cual tengo miedo me aconteció.
Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 No tengo paz, ni silencio, ni descanso; nada más que el dolor viene sobre mí.
Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”

< Job 3 >