< Job 17 >
1 Mi espíritu está quebrado, mis días han terminado, el sepulcro está listo para mí.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 En verdad, los que se burlan, están a mi alrededor, y mis ojos continúan viendo su amarga risa.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 Pon ahora tu fiador; porque no hay otro que ponga su mano en la mía.
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 Guardaste sus corazones de la sabiduría; por esta razón no les darás honor.
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 En cuanto al que es falso a su amigo por una recompensa, la luz se cortará de los ojos de sus hijos.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 Me ha hecho vergüenza a los pueblos; y que me escupan en la cara.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 Mis ojos se han oscurecido debido a mi dolor, y todo mi cuerpo es como una sombra.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 Los rectos se sorprenden de esto, y el que no ha hecho nada malo se levantará contra él hipócrita.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 Todavía los rectos mantendrán su camino, y el que tiene las manos limpias obtiene nuevas fuerzas.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 Pero regresen, ahora, todos ustedes, vengan; y no hallaré en ustedes a un hombre sabio.
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 Mis días han pasado, mis propósitos se han roto, incluso los deseos de mi corazón.
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 Están cambiando la noche en día; Dicen: La luz está cerca de la oscuridad.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 Si estoy esperando el sepulcro como mi casa, si he hecho mi cama en la oscuridad; (Sheol )
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol )
14 Si digo al sepulcro: Tú eres mi padre; y al gusano, mi madre y mi hermana;
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 ¿Dónde está mi esperanza? ¿Y quién verá mi deseo?
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 ¿Bajarán conmigo al inframundo? ¿Descansaremos juntos en polvo? (Sheol )
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol )