< Jeremías 40 >
1 La palabra que vino a Jeremías de parte del Señor, después de que Nabuzaradán, el capitán de la guardia real, lo dejó ir a Ramá, cuando lo liberó; porque lo habían encadenado, entre todos los prisioneros de Jerusalén y Judá que fueron llevados a Babilonia.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya pamene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anamasula Yeremiyayo ku Rama. Anamupeza Yeremiya ali womangidwa ndi unyolo pamodzi ndi amʼndende ena onse a ku Yerusalemu ndi a ku Yuda amene ankapita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
2 Entonces el capitán de la guardia real tomó a Jeremías y le dijo: Él Señor tu Dios dio palabra del mal que vendría en este lugar.
Mtsogoleriyu anamupeza Yeremiya, anamuwuza kuti, “Yehova Mulungu wako analengeza kale zakuti malo ano adzawonongedwa.
3 Y el Señor lo cumplió, y ha hecho lo que dijo; porque ustedes pecaron contra el Señor al no escuchar su voz; Y es por eso que esta cosa ha venido sobre ti.
Ndipo tsopano Yehova wachitadi zimenezi monga mmene ananenera. Izi zonse zachitika chifukwa anthu inu munachimwira Yehova ndipo simunamumvere.
4 Ahora, mira, este día te estoy liberando de las cadenas que tienes en tus manos. Si te parece bien que vengas conmigo a Babilonia, entonces ven y te vigilaré; pero si no te parece bien venir conmigo a Babilonia, entonces no vengas; mira, toda la tierra está delante de ti; si te parece bien, sigue viviendo en donde más te convenga.
Koma tsopano taona, lero ndikukumasula unyolo umene unali mʼmanja mwako. Ngati ukufuna kupita nane ku Babuloni, tiye ndipo adzakusamala bwino. Koma ngati sukufuna kupita, ndiye usapite. Dziko ndi limeneli monga ukulioneramo. Uli ndi ufulu kupita kulikonse kumene ukufuna.”
5 Luego regresa a Gedalías, hijo de Ahicam, hijo de Safán, a quien el rey de Babilonia ha nombrado gobernador sobre las ciudades de Judá, y haz tu lugar de convivencia con él entre el pueblo; O ve a donde te parezca bien ir. Así que el capitán de la guardia real le dio comida y algo de dinero y lo dejó ir.
Yeremiya asanayankhe, Nebuzaradani anamuwuzanso kuti, “Ngati supita ndiye pita, ubwerere kwa Gedaliya, mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kuti akhale bwanamkubwa wa Yuda. Ukakhale naye pakati pa anthu, kapena upite kulikonse ukufuna.” Ndipo mtsogoleri uja anamupatsa Yeremiya chakudya ndi mphatso zina ndi kumulola kuti apite.
6 Jeremías fue a Gedalías, hijo de Ahicam, en Mizpa, y vivía con él entre la gente que todavía estaba en la tierra.
Motero Yeremiya anapita kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ku Mizipa ndipo anakakhala naye kumeneko pakati pa anthu amene anatsala mʼdzikomo.
7 Cuando llegó a oídos de todos los capitanes de las fuerzas que estaban en el campo y de sus hombres, que el rey de Babilonia había hecho a Gedalías, hijo de Ahicam, gobernante de la tierra, y había puesto bajo su cuidado, los hombres, las mujeres y los niños, todos los más pobres de la tierra, los que no habían sido llevados a Babilonia;
Panali atsogoleri ena a nkhondo ndi anthu awo amene sanadzipereke nawo. Iwowa anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu kukhala bwanamkubwa wa dzikolo ndipo kuti yamuyika kukhala wolamulira amuna, akazi ndi ana amene anali osauka kwambiri mʼdzikomo, amene sanawagwire ukapolo kupita nawo ku Babuloni.
8 Entonces vinieron a Gedalías en Mizpa, a Ismael, hijo de Netanías, y Johanán, hijo de Carea, Seraías, hijo de Tanhumet, los hijos de Efai, de la Netofa, y a Jezania, hijo de Maacat, ellos y sus hombres.
Iwowa anapita ku Mizipa kwa Gedaliya. Amene anapitawo ndi awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani ndi Yonatani ana a Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti, ana a Efai a ku Netofa, ndi Yezaniya mwana wa Maaka, iwowo pamodzi ndi anthu awo.
9 Y Gedalías, hijo de Ahicam, hijo de Safán, les hizo un juramento a ellos y a sus hombres, diciendo: No tengan temor de someterse a los caldeos; sigan viviendo en la tierra y sean siervos del rey de Babilonia, y todo estará bien.
Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, anawalonjeza iwo pamodzi ndi anthuwo mwalumbiro. Ndipo anati, “Musaope kuwatumikira Ababuloni. Khalani mʼdziko muno, tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
10 En cuanto a mí, viviré en Mizpa como tu representante ante los caldeos que vienen a nosotros; pero ustedes recojan en sus vasijas vino, frutas de verano y aceite, y habiten en los pueblos que han tomado.
Ine ndidzakhala ku Mizipa kuti ndizikuyimirirani kwa Ababuloni amene azidzabwera kwa ife, koma inu muzikolola vinyo wanu, zipatso zanu, mafuta anu ndi kuzisunga mʼmitsuko yanu, nʼkumakhala mʼmizinda imene mwalandayo.”
11 De la misma manera, cuando todos los judíos que estaban en Moab y entre los hijos de Amón y en Edom y en todos los países, tuvieron noticias de que el rey de Babilonia había dejado que Judá se quedara con algunos de sus habitantes y que él había puesto sobre ellos a Gedalías, hijo de Ahicam, hijo de Safán;
Nawonso Ayuda onse a ku Mowabu, ku Amoni, ku Edomu ndi a ku mayiko ena onse anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasiyako anthu ena ku Yuda ndipo kuti inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala bwanamkubwa wawo.
12 Entonces todos los judíos regresaron de todos los lugares a los que habían ido en vuelo y llegaron a la tierra de Judá, a Gedalías, en Mizpa, y recogieron en gran abundancia vino y frutas de verano.
Tsono Ayuda onsewo anabwerera ku Yuda, ku Mizipa kwa Gedaliya, kuchokera ku mayiko onse kumene anabalalikira. Ndipo anakolola zipatso zochuluka ndi vinyo wambiri.
13 Entonces Johanan, el hijo de Carea, y todos los capitanes de las fuerzas que estaban en el campo, llegaron a Gedalías en Mizpa,
Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri a ankhondo onse amene sanadzipereke aja anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya
14 Y le dijo: ¿Sabes que Baalis, el rey de los hijos de Amón, ha enviado a Ismael, el hijo de Netanías, para que te quiten la vida? Pero Gedalías, el hijo de Ahicam, no confiaba en lo que decían.
ndipo anamufunsa kuti, “Kodi sukudziwa kuti Baalisi mfumu ya Aamoni watuma Ismaeli mwana wa Netaniya kuti akuphe?” Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu sanawankhulupirire.
15 Entonces Johanán, el hijo de Carea, le dijo a Gedalías en Mizpa en secreto: Déjame ir ahora a matar a Ismael, el hijo de Netanias, sin que nadie lo sepa; ¿por qué te ha de quitar tu vida para que todos los judíos que se han reunido a ustedes a tu alrededor sean dispersados para hacerlos huir, y el resto de los hombres de Judá llegan a su fin?
Tsono Yohanani mwana wa Kareya, mwamseri anawuza Gedaliya ku Mizipa kuti, “Loleni ndipite ndikaphe Ismaeli mwana wa Netaniya, ndipo palibe amene ati adziwe. Akuphereninji ndi kuchititsa Ayuda onse, amene akuzungulirani kuti abalalike ndi kuti otsala a ku Yuda awonongeke?”
16 Pero Gedalías, el hijo de Ahicam, le dijo a Johanan, el hijo de Carea: No debes hacer esto; porque lo que dices acerca de Ismael es falso.
Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu anawuza Yohanani mwana wa Kareya kuti, “Usachite zimenezo! Zimene ukunena za Ismaeli ndi zabodza.”