< Jeremías 33 >

1 Entonces la palabra del Señor vino a Jeremías la segunda vez, mientras él todavía estaba encerrado en el lugar de los vigilantes armados, diciendo:
Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
2 Estas son las palabras del Señor, que hizo la tierra, el Señor que la afirmó en su sitio; el Señor es su nombre;
“Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
3 Deja que tu clamor venga a mí, y te daré una respuesta, y te haré ver grandes cosas y cosas secretas de las que no tienes conocimiento.
‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
4 Porque esto es lo que el Señor, el Dios de Israel, ha dicho acerca de las casas de este pueblo y las casas de los reyes de Judá, que se han destruido para hacer rampas y la espada.
Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
5 Vinieron a pelear con los caldeos, pero solo servirán para llenar la ciudad con cadáveres de hombres a los que he condenado a muerte en mi ira y en mi furor, y debido a cuya maldad he mantenido el rostro cubierto de esta ciudad.
Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
6 Mira, los sanaré, les daré la salud nuevamente, los sanaré; y les dejaré ver la paz y la verdad en abundancia.
“‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
7 Y dejaré que se cambie el destino de Judá y de Israel, y los reconstruiré como al principio.
Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
8 Y los limpiaré de todos sus pecados, con los cuales han estado pecando contra mí; Tendré perdón por todos sus pecados, con los cuales ellos han estado pecando contra mí, y con los cuales han hecho el mal contra mí.
Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
9 Y este pueblo será para mí un nombre de alegría, una alabanza y una gloria ante todas las naciones de la tierra, quienes, al oír todo el bien que estoy haciendo por ellos, temblarán de miedo. Por todo el bien y la paz que estoy haciendo por ello.
Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
10 Esto es lo que el Señor ha dicho: Se volverán a oír en este lugar, del cual dices: Es un desperdicio, sin hombres y sin animales; incluso en las ciudades de Judá y en las calles de Jerusalén, en ruinas y despobladas, sin hombre y sin animal,
“Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
11 Voces felices, la voz de alegría, la voz del hombre recién casado y la voz de la novia, las voces de los que dicen: Alaben al Señor de los ejércitos, porque el Señor es bueno y su misericordia para siempre; las voces de los que van con alabanza a la casa del Señor. Porque devolveré los cautivos de la tierra para que vuelvan a ser como él principio, dice el Señor.
mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
12 Esto es lo que ha dicho el Señor de los ejércitos: Nuevamente habrá en este lugar, que es un desperdicio, sin hombre y sin animal, y en todos sus pueblos, volverá haber un lugar de descanso donde los criadores de ovejas harán sus rebaños descansar.
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
13 En los pueblos de la región montañosa, en los pueblos de las tierras bajas, en los pueblos del sur y en la tierra de Benjamín y en los alrededores de Jerusalén y en los pueblos de Judá, los rebaños volverán a pasar bajo la mano del que los cuenta, dice el Señor.
Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
14 Mira, vienen días, dice el Señor, cuando cumpliré la buena palabra que he dicho acerca del pueblo de Israel y del pueblo de Judá.
“‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
15 En aquellos días y en ese tiempo, permitiré que una Rama de justicia suba para David; y él será juez de justicia en la tierra.
“‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
16 En aquellos días, Judá tendrá la salvación y Jerusalén estará segura: y este es el nombre que le será dado: El Señor es nuestra justicia.
Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
17 Porque él Señor ha dicho: David nunca estará sin un descendiente que ocupe su lugar en el trono del reino de Israel;
Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
18 Y los sacerdotes y los levitas nunca estarán sin un descendiente que venga ante mí, ofreciendo ofrendas quemadas, incienso ofrendas de cereales y ofrendas de bestias en todo momento.
ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
19 Y vino la palabra del Señor a Jeremías, diciendo:
Yehova anawuza Yeremiya kuti:
20 El Señor ha dicho: Si es posible que se rompa mi pacto del día y la noche, que el día y la noche ya no lleguen a sus horas fijas,
Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
21 Entonces mi pacto con mi siervo David puede romperse, de modo que ya no tenga un hijo para ocupar su lugar en el asiento del reino; y mi pacto con los levitas, los sacerdotes, mis siervos.
Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
22 Como no es posible que el ejército del cielo esté contado, o la arena del mar medida, así haré la simiente de mi siervo David y los levitas mis siervos.
Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
23 Y vino la palabra del Señor a Jeremías, diciendo:
Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
24 ¿Has tomado nota de lo que estas personas han dicho, las dos familias, que el Señor escogió para sí mismo, los ha desechado? Esto lo dicen, mirando a mi gente con desprecio, en sus ojos, ya no es una nación.
“Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
25 El Señor ha dicho: Si no he hecho el día y la noche, y si los límites del cielo y la tierra no han sido fijados por mí,
‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
26 Entonces, dejaré de cuidar de la simiente de Jacob y de David mi siervo, de modo que no tomaré de su descendencia para ser gobernantes sobre la simiente de Abraham, Isaac y Jacob; porque haré volver su cautividad y tendré misericordia de ellos.
monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”

< Jeremías 33 >