< Isaías 20 >

1 En el año en que el comandante llegó a Asdod, enviado por Sargón, rey de Asiria, hizo una guerra contra ella y la tomó;
Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda,
2 En aquel momento vino la palabra del Señor a Isaías, hijo de Amoz, que decía: Ve, y quítate la túnica y los zapatos de tus pies. Y así lo hizo, andando sin ropa y sin zapatos en los pies.
nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.
3 Y el Señor dijo: Como mi siervo Isaías estuvo sin ropa y sin zapatos durante tres años como una señal y una maravilla para Egipto y Etiopía.
Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi,
4 Así se llevará el rey de Asiria a los prisioneros de Egipto y a los expulsados de Etiopía, jóvenes y viejos, sin ropa y sin zapatos, y con la espalda descubierta, para vergüenza de Egipto.
momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto.
5 Y estarán llenos de temor, y ya no tendrán fe en Etiopía, que era su esperanza, o en Egipto, que era su gloria.
Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi.
6 Y los que viven junto al mar dirán en ese día: Mira el destino de nuestra esperanza, a quien acudimos en busca de ayuda y salvación del rey de Asiria: ¿qué esperanza tenemos entonces de la salvación?
Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’”

< Isaías 20 >