< Isaías 2 >
1 La palabra que Isaías, hijo de Amoz, vio acerca de Judá y Jerusalén.
Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
2 Y acontecerá en los últimos días, que la montaña del Señor se colocará en la cima de las montañas, y se levantará sobre las colinas; y todas las naciones vendrán a él.
Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
3 Y los pueblos dirán: Vengan, subamos al monte del Señor, a la casa del Dios de Jacob, y él nos dará a conocer sus caminos, y seremos guiados por su palabra; porque de Sión saldrá la enseñanza, y la palabra del Señor de Jerusalén.
Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
4 Y él será el juez entre las naciones, y hará decisiones por muchos pueblos; y sus espadas se convertirán en hojas de arado, y sus lanzas en cuchillos de vid: ya no se volverán las naciones sus espadas una contra la otra, y el conocimiento de la guerra se habrá ido para siempre.
Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
5 Oh familia de Jacob, ven y vamos a la luz del Señor.
Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
6 Porque tú, Señor, has abandonado a tu pueblo, la familia de Jacob, porque están llenos de los caminos malvados del este, y hacen uso de artes secretas como los filisteos, y son amigos de los hijos de países extranjeros.
Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
7 Y su tierra está llena de plata y oro, y sus almacenes no tienen fin; su tierra está llena de caballos, y sus carros no tienen fin.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
8 Su tierra está llena de imágenes. Dan culto a la obra de sus manos, incluso a lo que sus dedos han hecho.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
9 Y la cabeza del hombre pobre está inclinada, y el gran hombre cae sobre su rostro; por esta causa no habrá perdón por su pecado.
Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
10 Entra en una cueva en la roca, cubriéndose de polvo, con temor del Señor, ante la gloria de su poder.
Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
11 Las miradas del hombre serán avergonzadas, y el orgullo de los hombres será humillado, y solo el Señor será levantado en ese día.
Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
12 Porque vendrá el día del Señor de los ejércitos sobre todo hombre soberbio y altivo y sobre todos los que se han ensalzado serán humillados;
Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
13 Y en todos los árboles altos del Líbano, y en todos los árboles fuertes de Basán;
tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
14 Y en todos los montes altos, y en todos los cerros que se alzan;
tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
15 Y en toda torre alta, y en todo muro fuerte;
tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
16 Y en todos los barcos de Tarsis, y en todas las pinturas preciadas.
tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
17 Y las miradas de los hombres serán avergonzadas, y el orgullo de los hombres será humillado; y solo el Señor será levantado en ese día.
Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
18 Y las imágenes nunca más serán vistas.
ndipo mafano onse adzatheratu.
19 Y los hombres irán a las grietas de las rocas y a los agujeros de la tierra, por temor al Señor, y ante la gloria de su poder, cuando salga de su lugar, sacudiendo la tierra con su fuerza.
Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
20 En ese día los hombres pondrán sus imágenes de plata y oro, que hicieron para la adoración, en la custodia de las bestias de los lugares oscuros;
Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
21 Para cubrirse en las grietas de las rocas y en los hoyos de las colinas, por temor al Señor, y ante la gloria de su poder, cuando él sale de su lugar, sacudiendo la tierra con su fuerza.
Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
22 No tenga más que ver con el hombre, cuya vida es solo un aliento, porque no tiene valor.
Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?