< Isaías 18 >

1 ¡Ay! Tierra del sonido de las alas, que está al otro lado de los ríos de Etiopía,
Tsoka kwa anthu a ku Kusi. Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
2 Que envía a sus representantes por el mar, incluso en barcos de papiro en las aguas. Regresa rápidamente, oh representantes, a una nación alta y suave, a un pueblo que causa temor a lo largo de toda su historia; una nación fuerte y opresora, cuya tierra está atravesada por ríos.
Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo, mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi, ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro, kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala, ndi woopedwa ndi anthu. Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena. Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”
3 Todos ustedes pueblos del mundo, y ustedes que viven en la tierra, cuando una bandera se alza en las montañas, presten atención; y cuando suene la bocina, escuchen.
Inu nonse anthu a pa dziko lonse, inu amene mumakhala pa dziko lapansi, pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri yangʼanani, ndipo pamene lipenga lilira mumvere.
4 Porque esto es lo que el Señor me ha dicho: Estaré callado, observando desde mi lugar; como el calor claro cuando brilla el sol, como una niebla de rocío en el calor del verano.
Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti, “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana, monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha, monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
5 Porque antes del momento de entrar en las uvas, después de la apertura del capullo, cuando la flor se haya convertido en una uva lista para triturar, quitará las pequeñas ramas con cuchillos, cortando, podando y tirara las ramas.
Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka ndiponso mphesa zitayamba kupsa, Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira, ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
6 Serán para las aves de las montañas, y para las bestias de la tierra: las aves de rapiña pasarán allí el verano, y las bestias salvajes de la tierra pasarán el invierno allí.
Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama ndiponso zirombo zakuthengo; mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe, ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.
7 En ese tiempo se hará una ofrenda al Señor de ejércitos de un pueblo alto y suave, causando temor a través de toda su historia; una nación fuerte y opresora, cuya tierra está atravesada por ríos, una ofrenda llevada al lugar del nombre del Señor de los ejércitos, al Monte Sión.
Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse, zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala, kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe, mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo, anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje. Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.

< Isaías 18 >