< Isaías 14 >

1 Porque el Señor tendrá misericordia de Jacob, y volverá a hacer de Israel su pueblo especial, y los pondrá en su tierra; y el hombre extranjero se juntara a ellos y se unirá a la familia de Jacob.
Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
2 Y el pueblo los llevará con ellos a su lugar, y los hijos de Israel les darán una herencia en la tierra del Señor como sirvientes y sirvientas, haciéndolos prisioneros de los cuales eran prisioneros; y serán gobernantes de sus amos.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
3 Y será en el día en que el Señor te dé descanso de tu dolor, de tu angustia y del duro yugo que te habían puesto.
Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
4 Que recitarás esta amarga canción contra el rey de Babilonia, y dirás: ¡Cómo ha terminado el cruel tirano! Como cesó la ciudad de oro;
mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
5 La vara de los que hacen el mal, la vara de los gobernantes, es quebrantada por el Señor;
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
6 Aquel cuya vara estaba sobre los pueblos con una ira interminable, gobernando a las naciones con ira, con un gobierno incontrolado.
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
7 Toda la tierra está en reposo y está en silencio y estalla en cantos de alegría.
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
8 Incluso los árboles del bosque se alegran sobre ti, los árboles del Líbano, diciendo: Desde el momento de tu caída, ningún cortador de madera ha subido contra nosotros con un hacha.
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
9 El inframundo se conmueve con tu venida, los muertos están despiertos ante ti, incluso los fuertes de la tierra. Todos los reyes del mundo se han levantado de sus asientos. (Sheol h7585)
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol h7585)
10 Todos te responden y te dicen: ¿Te has vuelto débil como nosotros? ¿Has sido hecho como nosotros?
Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
11 Tu orgullo ha descendido al inframundo y el ruido de tus instrumentos de música; Los gusanos están debajo de ti, y tu cuerpo está cubierto con ellos. (Sheol h7585)
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol h7585)
12 ¡Qué grande es tu caída del cielo, oh lucero de la aurora, hijo de la mañana! ¿Cómo has caído a la tierra, tú que debilitabas a las naciones?
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 Porque dijiste en tu corazón: Subiré al cielo, haré mi asiento más alto que las estrellas de Dios; Tomaré mi lugar en la montaña del lugar de reunión de los dioses, en las partes más alejadas del norte.
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 Subiré más alto que las nubes; Seré como el Altísimo.
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 Pero descenderás al inframundo, incluso a sus partes más profundas. (Sheol h7585)
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol h7585)
16 Los que te vean te estarán observando con cuidado, pensarán profundamente y dirán: ¿Es éste el perturbador de la tierra, el agitador de los reinos?
Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
17 Que hizo del mundo un desperdicio, derribando sus ciudades; Quien no dejó escapar a sus prisioneros de la cárcel.
munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
18 Todos los reyes de la tierra descansan en gloria, cada uno en su sepulcro.
Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
19 Pero tú, como un nacimiento antes de su tiempo, estás tendido sin lugar de descanso en la tierra; vestido con los cuerpos de los muertos que han sido arrojados a la espada, que descienden a las partes más bajas del inframundo; Un cuerpo muerto, aplastado bajo el pie.
Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
20 En cuanto a tus padres, no estarás unido a ellos en su lugar de descanso, porque has sido la causa de la destrucción de tu tierra y de la muerte de tu pueblo; la semilla del malvado no tendrá lugar en la memoria del hombre.
Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 Prepara un lugar de muerte para sus hijos, por el mal hecho de sus padres; para que no puedan subir y tomar la tierra por su herencia, cubriendo la faz del mundo con ciudades.
Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
22 Porque subiré contra ellos, dice el Señor de los ejércitos, cortando el nombre y la descendencia de Babilonia, el hijo y el hijo del hijo, dice el Señor.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
23 Y te haré una herencia para el erizo y los estanques de agua; y la barreré con la escoba de la destrucción, dice el Señor de los ejércitos.
“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
24 El Señor de los Ejércitos ha hecho un juramento, diciendo: Lo que había pensado ciertamente se cumplirá, y lo que había planeado se llevará a cabo.
Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 Para que el asirio sea quebrantado en mi tierra, y aplastado bajo mis montañas: allí será quitado su yugo, y su gobierno sobre ellos llegará a su fin.
Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
26 Este es el propósito para toda la tierra, y esta es la mano extendida sobre todas las naciones.
Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 Porque es el propósito del Señor de los ejércitos, y ¿quién lo hará inútil? cuando su mano está extendida, ¿por quién puede ser devuelta?
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
28 En el año de la muerte del rey Acaz, esta palabra llegó al profeta:
Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
29 No se alegren, oh Filistea, todos ustedes, porque se quebró la vara que los oprimía; porque de la raíz de la serpiente saldrá una serpiente venenosa, y su fruto será una serpiente venenosa alada.
Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 Y los más pobres de la tierra tendrán comida, y los necesitados tendrán un lugar de descanso seguro, pero tu simiente llegará a su fin por la necesidad de comida, y el resto de ustedes serán puestos a la espada.
Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
31 ¡Envía un clamor, oh puerta! ¡Gime de tristeza, pueblo! Desanímate, tu tierra ha quedado en nada, oh Filistea; porque sale un humo del norte, y todos mantienen su lugar en la fila.
Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 ¿Qué respuesta dará, entonces, mi pueblo a los representantes de la nación? Que el Señor es el constructor de Sión, y ella será un lugar seguro para los pobres de su pueblo.
Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”

< Isaías 14 >