< Oseas 8 >

1 Pon la trompeta en tu boca. Él viene como un águila contra la casa del Señor; porque han ido en contra de mi pacto, no han guardado mi ley.
“Ika lipenga pakamwa pako. Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova chifukwa anthu aphwanya pangano langa ndiponso agalukira lamulo langa.
2 Clamarán a mi: Nosotros, Israel, te conocemos, oh Dios de Israel.
Israeli akulirira kwa Ine kuti, ‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
3 Israel ha renunciado a lo que es bueno; Sus enemigos irán tras él.
Koma Israeli wakana zabwino; mdani adzamuthamangitsa.
4 Han puesto reyes, pero no por mí; han nombrado príncipes, pero yo no lo sabía; han hecho imágenes de plata y oro, para su propia destrucción.
Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga. Amasankha akalonga popanda chilolezo changa. Amadzipangira mafano asiliva ndi agolide koma adzawonongeka nawo.
5 No tendré nada que ver con tu becerro, oh Samaria; mi ira arde contra ellos; ¿Cuánto tiempo pasará antes de que los hijos de Israel se purifiquen?
Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe! Mkwiyo wanga wayakira anthuwo. Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
6 El artesano lo hizo, no es dios; El buey de Samaria se partirá en pedazos.
Mafanowa ndi ochokera ku Israeli! Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso; si Mulungu amene anamupanga. Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa, mwana wangʼombe wa ku Samariya.
7 Porque han sembrado el viento, y su fruto será la tormenta; su grano no tiene tallo, no dará comida, y si lo tiene, una nación extranjera lo tomará.
“Aisraeli amadzala mphepo ndipo amakolola kamvuluvulu. Tirigu alibe ngala; sadzabala chakudya. Akanabala chakudya alendo akanadya chakudyacho.
8 Israel ha venido a la destrucción; ahora están entre las naciones como una copa en la que no hay placer.
Israeli wamezedwa, tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina ngati chinthu cha chabechabe.
9 Porque subieron a Asiria como un asno salvaje; Efraín ha comprado amantes.
Pakuti iwo anapita ku Asiriya ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha. Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
10 Pero aunque dan dinero a las naciones para que lo ayuden, los juntaré y los afligiré un poco por la carga del rey y gobernantes.
Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu, Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi. Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.
11 Debido a que Efraín ha aumentado los altares por el pecado, los altares se han convertido en una causa de pecado para él.
“Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo, maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
12 Aunque pongo mi ley por escrito para él en diez mil reglas, son consideradas como algo extraño.
Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga, koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
13 Él da las ofrendas de sus amantes, y toma la carne como alimento; pero el Señor no tiene placer en ellos; ahora tendrá en cuenta su maldad y les dará el castigo de sus pecados; Regresarán a Egipto.
Amapereka nsembe za nyama kwa Ine ndipo iwo amadya nyamayo, koma Yehova sakondwera nazo. Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo: iwowo adzabwerera ku Igupto.
14 Porque Israel no tiene memoria de su Hacedor, y ha levantado los palacios de los reyes; y Judá ha hecho grande el número de sus ciudades amuralladas. Pero enviaré un incendio a sus pueblos y pondré fin a sus palacios.
Israeli wayiwala Mlengi wake ndipo wamanga nyumba zaufumu; Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga. Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo, moto umene udzatenthe malinga awo.”

< Oseas 8 >