< Génesis 4 >

1 Y el varón tuvo relaciones con su mujer Eva, y quedó encinta, y dio a luz a Caín, y dijo: Me ha dado un hombre él Señor.
Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
2 Entonces ella volvió a tener un hijo y dio a luz a Abel, su hermano. Y Abel era pastor de ovejas, pero Caín era granjero.
Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
3 Y después de un tiempo, Caín le dio al Señor una ofrenda de los frutos de la tierra.
Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
4 Y Abel dio una ofrenda de los corderos de su rebaño y de su grasa. Y el Señor estaba complacido con la ofrenda de Abel;
Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
5 Pero en Caín y en su ofrenda no se complació. Y Caín estaba enojado y su rostro se puso triste.
Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
6 Y él Señor dijo a Caín: ¿Por qué estás enojado? y por qué tu cara está triste?
Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
7 Si lo haces bien, ¿no tendrás honor? y si lo haces mal, el pecado te espera en la puerta, deseando tenerte, pero no dejes que sea tu amo.
Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
8 Y dijo Caín a su hermano: Pasemos al campo; y estando ellos en el campo, Caín atacó a su hermano Abel y lo mató.
Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
9 Y él Señor dijo a Caín: ¿Dónde está tu hermano Abel? Y él dijo: No tengo idea: ¿soy el guardián de mi hermano?
Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
10 Y él dijo: ¿Qué has hecho? la voz de la sangre de tu hermano me está llamando desde la tierra.
Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
11 Y ahora eres maldito de la tierra, cuya boca está abierta para recibir la sangre de tu hermano de tu mano;
Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
12 La tierra ya no te dará su fruto como la recompensa de tu trabajo; serás un vagabundo errante sobre la tierra.
Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
13 Y dijo Caín: Mi castigo es mayor que mi fuerza.
Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
14 Me has enviado hoy de la faz de la tierra y de delante de tu rostro; Voy a ser un vagabundo errante sobre la tierra, y el que me vea me matará.
Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
15 Y él Señor dijo: De cierto, si muere Caín, siete vidas serán tomadas por él. Y el Señor puso una marca en Caín para que nadie lo matara.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
16 Y se apartó Caín de delante de la faz del Señor, y se quedó a vivir en la tierra de Nod, al oriente del Edén.
Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
17 Y Caín tuvo relaciones con su esposa, y ella engendró y dio a luz a Enoc; y él hizo una ciudad, y le dio a la ciudad el nombre de Enoc por su hijo.
Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
18 Y Enoc tuvo un hijo Irad; e Irad fue padre de Mehujael; y Mehujael padre de Metusael; y Metusael fue padre de Lamec.
Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
19 Y Lamec tuvo dos mujeres; el nombre de uno era Ada, y el nombre del otro Zila.
Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
20 Y Ada dio a luz a Jabal; era el padre de los que viven en tiendas y tienen ganado.
Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
21 Y el nombre de su hermano era Jubal: él era el padre de todos los que tocan con arpa y flauta.
Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
22 Y Zila dio a luz a Tubal-caín, que es el padre de todo fabricante de instrumentos de bronce y de hierro, y la hermana de Tubal-caín fue Naama.
Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
23 Y dijo Lamec a sus mujeres, Ada y Zila, escucha mi voz; esposas de Lamec, presten atención a mis palabras, porque yo pondría a muerte a un hombre por una herida, y a un joven por un golpe;
Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
24 Si se quieren tomar siete vidas como castigo por la muerte de Caín, setenta y siete serán tomadas por las de Lamec.
Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
25 Y Adán volvió a tener relaciones con su esposa, y ella dio a luz a un hijo al que dio el nombre de Set, porque ella dijo: Dios me ha dado otra simiente en lugar de Abel, a quien Caín mató.
Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
26 Y Set tuvo un hijo, y le dio el nombre de Enós: en este tiempo los hombres primero hicieron uso del nombre del Señor en adoración.
Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.

< Génesis 4 >