< Ezequiel 39 >

1 Y tú, hijo de hombre, profetiza contra Gog, y di: Estas son las palabras del Señor: Mira, yo estoy contra ti, oh Gog, regente de Ros, Mesec y Tubal.
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 Y te haré volver, y dejaré de ti solo la sexta parte seré tu guía y te haré subir desde lo más profundo del norte; Te haré venir a los montes de Israel.
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 Y con un golpe enviaré tu arco de tu mano izquierda y tus flechas cayendo de tu mano derecha.
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 En las montañas de Israel caerás, tú y todas tus fuerzas y los pueblos que están contigo; te daré a las aves crueles de todo tipo y a las bestias del campo para que seas su alimento.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 Descenderás al campo abierto: porque lo he dicho, dice el Señor Dios.
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 Y enviaré fuego a Magog y a los que viven en las costas confiadamente: y sabrán que yo soy Dios.
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 Y haré notorio mi santo nombre entre mi pueblo Israel; Ya no dejaré que mi santo nombre sea profanado; y las naciones sabrán que yo soy Dios, el Santo en Israel.
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 Mira, viene y se hará, dice el Señor Dios; Este es el día del cual he dado palabra.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 Y los que viven en las ciudades de Israel saldrán y encenderán los instrumentos de guerra, quemando los paveses y las corazas, los arcos y las flechas y los palos y las lanzas, y durante siete años harán fuego con ellos.
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 Y no sacarán madera del campo ni la cortarán en el bosque; porque harán su fuego de los instrumentos de guerra, y tomarán por la fuerza los bienes de los que tomaron sus bienes, y se marcharán con los bienes de los que tomaron sus bienes, dice el Señor.
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 Y sucederá en aquellos días, que le daré a Gog una sepultura allí en Israel, en el valle al este del mar; ese lugar impedirá el paso a los viajeros, y allí enterrarán a Gog y a toda su ejército, y se nombrará el lugar, El valle de Hamón-Gog.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 Y los hijos de Israel los estará enterrando, por siete meses, para limpiar la tierra.
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 Y toda la gente estarán ocupados enterrándolos; y será para ellos memorable ese día en que permita que mi gloria sea vista, dice el Señor Dios.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 Y pondrán a un grupo de hombres para que no hagan otro trabajo que ir a recorrer la tierra y enterrar al resto de los que aún están en la faz de la tierra, para limpiarla; después de siete meses, se hará un reconocimiento.
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 Y mientras recorren la tierra, si alguien ve el hueso de un hombre, debe colocar una señal junto al lugar hasta que los que están haciendo el trabajo lo hayan enterrado en el valle de Hamón Gog.
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 Y allí pondrán todo el ejército de Gog, será llamada Hamona y limpiarán la ciudad.
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 Y tú, hijo de hombre, esto es lo que el Señor ha dicho: di a las aves de todo tipo y a todas las bestias del campo, reúnanse y vengan; únanse por todas partes a la ofrenda que estoy haciendo morir por ustedes, una gran ofrenda en las montañas de Israel, para que puedan tener carne para su comida y sangre para su bebida.
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 La carne de los hombres de guerra será su alimento, y beberán la sangre de los príncipes de la tierra, de ovejas y corderos, de cabras, de bueyes, todos ellos bestias gordas de Basán.
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 Continuarán festejando con la grasa hasta que estén satisfechos, y beberán la sangre hasta que se embriaguen, de mi ofrenda que he sacrificado para ustedes.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 En mi mesa tendrán comida en toda su medida, caballos y carruajes de guerra, grandes hombres y todos los hombres de guerra, dice el Señor Dios.
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 Y pondré mi gloria entre las naciones, y todas las naciones verán mis castigos que he puesto en práctica, y mi mano que he puesto sobre ellos.
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 Entonces los hijos de Israel sabrán que yo soy Dios, su Dios Supremo, desde ese día y para el futuro.
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 Y quedará claro para las naciones que los hijos de Israel fueron llevados prisioneros por su maldad; porque hicieron mal contra mí, y mi rostro se escondió de ellos; así que los entregué en manos de sus atacantes, y todos llegaron a su fin por la espada.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 En la medida de sus caminos inmundos y sus pecados, así lo hice con ellos; y mantuve mi rostro escondido de ellos.
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 Por esto ha dicho el Señor: Ahora dejaré que se cambie el destino de Jacob, y tendré misericordia de todos los hijos de Israel, y me encargaré del honor de mi santo nombre.
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 Y serán conscientes de su vergüenza y de todos los males que han hecho contra mí, cuando vivan en su tierra sin ningún sentido de peligro y sin nadie que sea motivo de temor para ellos;
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 Cuando los he recuperado de entre los pueblos y los he reunido de las tierras de sus enemigos, y me he santificado en ellos ante los ojos de un gran número de naciones.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 Y sabrán que yo soy Dios, su Dios supremo, porque los envié como prisioneros entre las naciones, y los he llevado juntos de regreso a su tierra; y no he dejado que uno de ellos esté allí por más tiempo.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 Y mi rostro ya no esconderé de ellos; porque he derramado mi espíritu sobre los hijos de Israel, dice el Señor Dios.
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ezequiel 39 >