< Éxodo 35 >

1 Y Moisés envió a todos los hijos de Israel a que se unieran, y les dijo: Esto es lo que el Señor ha dicho y estas son sus órdenes.
Mose anasonkhanitsa gulu lonse la Aisraeli ndipo anawawuza kuti, “Zinthu zimene Yehova wakulamulirani kuti muzichite ndi izi:
2 Seis días se trabajará, pero el séptimo día es un día santo para ustedes, un día de reposo para el Señor; cualquiera que haga algún trabajo en ese día será condenado a muerte.
Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku la chisanu ndi chiwiri likhale la Sabata, tsiku lanu lopuma, lopatulika kwa Yehova. Aliyense amene adzagwira ntchito iliyonse pa tsikuli ayenera kuphedwa.
3 No se encenderá fuego en ninguna de sus casas en el día de reposo.
Pa tsiku la Sabata musakoleze moto paliponse pamene mukhala.”
4 Y dijo Moisés a toda la congregación de los hijos de Israel: Este es el mandato que el Señor ha dado:
Mose ananena kwa gulu lonse la Aisraeli kuti, “Zimene Yehova wakulamulirani ndi izi:
5 Toma de entre ustedes una ofrenda al Señor; cualquiera que tenga la voluntad en su corazón, que dé su ofrenda al Señor; oro y plata y bronce;
Kuchokera pa zomwe muli nazo, mutenge chopereka cha Yehova. Aliyense amene ali ndi mtima wofuna kupereka abweretse kwa Yehova zopereka izi: Golide, siliva ndi mkuwa;
6 Y tela azul, púrpura y rojo, y el mejor lino fino y cabello de cabras,
nsalu zobiriwira, zapepo, zofiira, nsalu zofewa; ubweya wambuzi;
7 Y pieles de carnero de color rojo, y cuero, y madera de acacia,
zikopa za nkhosa zazimuna za utoto wofiira ndi zikopa za akatumbu; matabwa amtengo wa mkesha,
8 Y aceite para las luces, y especias para el aceite sagrado de la unción y para él incienso aromático para quemar.
mafuta anyale a olivi, zonunkhiritsa mafuta odzozera ndi zopangira lubani wonunkhira;
9 Y piedras de ónice y las joyas para cortar para el efod y para él pectoral del sacerdote.
miyala yokongola ya mtundu wa onikisi ndi ina yabwino yoyika pa Efodi ndi pa chovala cha pachifuwa.
10 Y cada hombre de corazón sabio entre ustedes venga y haga lo que el Señor le haya ordenado;
“Anthu onse aluso pakati panu abwere ndi kupanga zonse zimene Yehova walamula:
11 La casa y su tienda y su cubierta, sus ganchos y sus tablas, sus varillas y sus columnas y sus basas;
Chihema ndi tenti yake ndiponso chophimba chake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
12 El arca con sus varillas y él propiciatorio el velo colgando delante de ella;
Bokosi la Chipangano pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake cha bokosilo ndi nsalu zophimba bokosilo;
13 La mesa y sus varas, todos sus vasos, y el pan de la propiciación;
tebulo pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira pamodzi ndi zipangizo zake zonse ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
14 Y el candelabro para las luces, con sus vasijas y sus lámparas y el aceite para la luz;
choyikapo nyale yowunikira pamodzi ndi zipangizo zake, nyale ndi mafuta anyalezo;
15 Y el altar para la quema de especias, con sus varas, y el aceite sagrado de la unción y él incienso aromático, y la cortina para la puerta, a la puerta de la tienda;
guwa lofukizira lubani pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira, mafuta odzozera ndi lubani onunkhira; nsalu yotchinga pa khomo lolowera mʼchihema;
16 El altar de las ofrendas quemadas, con su enrejado de bronce, sus varas y todos sus utensilios, la palangana para lavar y su base;
guwa lansembe yopsereza pamodzi ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse, beseni losambira lamkuwa ndi miyendo yake;
17 Las cortinas para él atrio, sus columnas y sus bases, y el telón para la entrada;
nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake, ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo;
18 Los estacas para la tienda, y las estacas para el atrio y sus cuerdas;
zikhomo za tenti ya chihema ndiponso za bwalo, ndi zingwe zake;
19 Las túnicas para ministrar en el lugar santo, las túnicas sagradas para el sacerdote Aarón, y las túnicas para sus hijos cuando actúan como sacerdotes.
zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.”
20 Y todos los hijos de Israel se apartaron de Moisés.
Kenaka gulu lonse la Aisraeli linachoka pamaso pa Mose,
21 Y a todos los que sintieron movidos de corazón, a todos los que se guiaron por el impulso de su espíritu, vinieron con su ofrenda para el Señor, para lo que fuera necesario para la Tienda de reunión y su obra y para las vestiduras sagradas.
ndipo aliyense amene anakhudzidwa mu mtima mwake nafuna kupereka, anabwera kudzapereka chopereka kwa Yehova cha ntchito yokonza tenti ya msonkhano, cha ntchito zonse za mʼtentimo ndi cha zovala zopatulika.
22 Vinieron, hombres y mujeres, todos los que estaban dispuestos a dar, y dieron alfileres, narigueras, anillos de dedo y adornos para el cuello, todo de oro; todos dieron una ofrenda de oro al Señor.
Onse amene anali ndi mtima wofuna, amuna ndi amayi omwe anabwera kudzapereka zodzikometsera zagolide za mtundu uliwonse: zomangira zovala, ndolo, mphete ndi zokometsera. Onse anapereka golide wawo monga nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
23 Y todos los que tenían tela azul, púrpura y rojo, y el mejor lino y pelo de cabra, y pieles de oveja de color rojo y cuero, se los dieron.
Aliyense amene anali ndi nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo kapena yofiira kapena yofewa, yosalala, kapena ubweya wambuzi, zikopa za nkhosa zonyika mu utoto wofiira kapena zikopa anazibweretsa.
24 Todos los que tenían plata y bronce les ofrecieron al Señor; y todos los que tenían madera de acacia, como la que se necesitaba para el trabajo, se la dieron.
Onse amene anapereka chopereka cha siliva kapena mkuwa anabweretsa monga chopereka kwa Yehova. Ndipo aliyense amene anali ndi matabwa a mtengo wa mkesha kuti awagwiritse ntchito mbali ina iliyonse ya ntchitoyo, anabweretsa.
25 Y todas las mujeres que eran expertas con sus manos, hicieron telas, y dieron la obra de sus manos, tela azul, púrpura y rojo, y el mejor lino.
Mayi aliyense waluso analuka ndi manja ake ndi kubweretsa chomwe analuka cha mtundu wa mtambo, chapepo kapena chofiira kapena chofewa, chosalala.
26 Y aquellas mujeres que tenían el conocimiento, hicieron el cabello de las cabras en tela.
Ndipo amayi onse amene anali ndi mtima wofuna ndipo anali ndi luso analuka ubweya wa mbuzi.
27 Y los príncipes dieron piedras de ónice, y las joyas cortadas para el efod y el pectoral del sacerdote;
Atsogoleri anabweretsa miyala ya onikisi ndi miyala yokongola yoyika pa efodi ndi chovala chapachifuwa.
28 Y la sal y el aceite para la luz, y el aceite santo para la unción y él incienso aromático.
Anabweretsanso zonunkhiritsa ndiponso mafuta owunikira a olivi ndi odzozera ndi zofukizira zonunkhira.
29 Los hijos de Israel, cada hombre y cada mujer, por el impulso de sus corazones, dieron sus ofrendas libremente al Señor por la obra que el Señor le había ordenado a Moisés que hiciera.
Aisraeli onse aamuna ndi aakazi amene anali ndi mtima wofuna, anabweretsa kwa Yehova chopereka chaufulu ku ntchito yonse ya Yehova imene analamulira kudzera mwa Mose kuti achite.
30 Y Moisés dijo a los hijos de Israel: He aquí que el SEÑOR designó a Bezaleel, hijo de Uri, hijo de Hur, de la tribu de Judá;
Kenaka Mose anati kwa Aisraeli, “Taonani, Yehova wasankha Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa fuko la Yuda,
31 Y lo ha llenado del espíritu de Dios, en toda sabiduría, conocimiento y arte de todo tipo;
ndipo wamudzaza ndi Mzimu wa Mulungu kotero kuti ali ndi luso ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndipo akudziwa bwino ntchito zonse zamanja monga izi:
32 Como diseñador experto de cosas bellas, trabajando en oro, plata y bronce;
Kulemba ndondomeko ya ntchito zaluso ndi kupanga zinthu zagolide, zasiliva ndi zamkuwa,
33 Entrenado en el corte de piedras y el adorno de la madera y en todo tipo de trabajos manuales.
kusema ndi kuyika miyala yokongola, kukonza zinthu zamatabwa ndiponso kugwira ntchito ina iliyonse yamanja.
34 Y le dio a él, y a Aholiab, hijo de Ahisamac, de la tribu de Dan, el poder de entrenar a otros.
Ndipo Iye wapereka kwa Bezaleli pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani luso lophunzitsa ena.
35 A ellos les ha dado conocimiento de todas las artes del artesano, del diseñador y del obrero experto; del fabricante de bordado en tela azul, púrpura y rojo y el mejor lino y del fabricante de telas; son capacitados en todas las artes del diseñador y el obrero entrenado.
Mulungu wawapatsa maluso osiyanasiyana, maluso ogoba, olemba ndondomeko, opeta zokometsera pa nsalu zamtundu wamtambo, zapepo ndi zofiira ndiponso zofewa zosalala ndi zoluka. Onsewa ndi amisiri a ntchito zamanja ndi zokonza ndondomeko.

< Éxodo 35 >