< Éxodo 24 >

1 Y Señor dijo a Moisés: Sube ante SEÑOR, tú y Aarón, y Nadab, y Abiú, y setenta de los jefes de Israel; y dame culto desde la distancia.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Bwera ku phiri kuno kwa Yehova, iwe pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu a Israeli makumi asanu ndi awiri. Enanu mundipembedze muli chapatali.
2 Y sólo Moisés se acercará al Señor; pero los otros no deben acercarse, y la gente no puede subir con ellos.
Koma Mose yekha ayandikire Yehova, ndipo enawo asayandikire. Komanso anthu ena onse asakwere nawe ku phiri kuno.”
3 Entonces Moisés vino y presentó al pueblo todas las palabras del Señor y sus leyes; y todo el pueblo, respondiendo a una voz, dijo: Todo lo que el Señor ha dicho haremos.
Tsono Mose anapita kukawuza anthu mawu onse a Yehova ndi malamulo onse, ndipo anthu onse anayankha mogwirizana kuti, “Tidzachita zonse zimene Yehova wanena.”
4 Entonces Moisés puso por escrito todas las palabras del Señor, y levantándose de mañana hizo un altar al pie del monte, con doce columnas para las doce tribus de Israel.
Ndipo Mose analemba zonse zimene Yehova ananena. Mmawa mwake Mose anadzuka nayamba kumanga guwa lansembe mʼmunsi mwa phirilo ndipo anayimika miyala khumi ndi iwiri ngati zipilala kuyimira mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
5 Y envió a algunos de los jóvenes de los hijos de Israel a hacer ofrendas quemadas y ofrendas de paz de bueyes al Señor.
Kenaka Mose anatuma Aisraeli achinyamata kuti aphe ndi kukapereka kwa Yehova nsembe zopsereza zachiyanjano.
6 Y Moisés tomó la mitad de la sangre y la puso en vasijas; drenando la mitad de la sangre sobre el altar.
Mose anatenga theka la magazi ndi kuyika mʼmbale, ndipo theka linalo analiwaza pa guwa lansembe.
7 Y tomó el libro del pacto, y lo leyó a oídos del pueblo; y dijeron: Todo lo que él Señor ha dicho, haremos, y guardaremos sus leyes.
Anatenganso Buku la Chipangano ndi kuwerengera anthu. Anthuwo anayankha kuti, “Zonse zimene Yehova wanena tamva, ndipo tidzazichita.”
8 Entonces Moisés tomó la sangre y dejó que cayera sobre el pueblo, y dijo: Esta sangre es la señal del pacto que el Señor ha hecho contigo en estas palabras.
Kenaka Mose anatenga magazi, nawaza anthuwo ndipo anati, “Awa ndi magazi a pangano limene Yehova wapanga ndi inu molingana ndi mawu ake onsewa.”
9 Entonces Moisés y Aarón, Nadab y Abiú, y setenta de los jefes de Israel subieron:
Kenaka Mose pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Israeli aja anakwera ku phiri,
10 Y vieron al Dios de Israel; y bajo sus pies había, como parecía, un piso de zafiro, claro como el cielo.
ndipo anaona Mulungu wa Israeli. Pansi pa mapazi ake panali njira yoyendamo yopangidwa ndi mwala wa safiro woyalidwa bwino wa maonekedwe owala ngati thambo.
11 Y no puso su mano sobre los jefes de los hijos de Israel; vieron a Dios, y comieron y bebieron.
Ngakhale anaona Yehova koma sanafe, mʼmalo mwake anadya ndi kumwa.
12 Y él Señor dijo a Moisés: Sube a mí al monte, y espera allá; y yo te daré las piedras sobre las cuales puse por escrito la ley y las órdenes, para que enseñes al pueblo.
Yehova anati kwa Mose, “Bwera kwa ine ku phiri kuno, ndipo udikire konkuno. Ndidzakupatsa miyala imene ndalembapo malemba kuti ndiwaphunzitse.”
13 Entonces Moisés y su siervo Josué se levantaron; y Moisés subió al monte de Dios.
Ndipo anayamba ulendo wopita ku phiri la Mulungu pamodzi ndi womuthandiza wake Yoswa.
14 Y dijo a los jefes: Guardaos aquí hasta que volvamos a ustedes: Aarón y Hur están con ustedes; si alguien tiene alguna causa, que se vaya con ellos.
Apa nʼkuti Mose atawawuza akuluakulu aja kuti, “Mudikire pano mpaka titabweranso. Aaroni ndi Huri ali nanu, aliyense amene ali ndi milandu apite kwa iwo.”
15 Y Moisés subió al monte, y fué cubierto por la nube.
Mose atakwera ku phiri kuja mtambo unaphimba phirilo.
16 Y la gloria de él Señor reposaba en el monte Sinaí, y la nube estaba sobre ella por seis días; y en el séptimo día dijo el nombre de Moisés desde la nube.
Ulemerero wa Yehova unakhala pa phiri la Sinai, ndipo mtambo unaphimba phirilo kwa masiku asanu ndi limodzi. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Yehova anayitana Mose kuchokera mu mtambowo.
17 Y la gloria del Señor era como una llama en la cima de la montaña ante los ojos de los hijos de Israel.
Ulemerero wa Yehova uja unkaoneka ngati malawi a moto pamwamba pa phirilo.
18 Y Moisés subió al monte, a la nube, y estuvo allí cuarenta días y cuarenta noches.
Ndipo Mose analowa mʼmitambo nakwera phiri. Iye anakhala ku phiriko 40 usana ndi usiku.

< Éxodo 24 >