< Éxodo 17 >

1 Y los hijos de Israel salieron del desierto de Sin, por etapas, según el Señor les dio órdenes, y levantaron sus tiendas en Refidim; y no había agua potable para el pueblo.
Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku chipululu cha Sini, ndi kumayenda malo ndi malo monga momwe anawalamulira Yehova. Iwo anamanga misasa yawo ku Refidimu koma kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa.
2 Entonces el pueblo se enojó con Moisés y le dijo: Danos agua para beber. Y Moisés dijo: ¿Por qué estás enojado conmigo? y ¿por qué pones a Dios a prueba?
Kotero iwo anakangana ndi Mose nati, “Tipatse madzi akumwa.” Mose anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukukangana ndi ine? Chifukwa chiyani mukumuyesa Yehova?”
3 Y la gente tenía gran necesidad de agua; y murmuraron contra Moisés, y dijeron: ¿Por qué nos has sacado de Egipto para enviarnos la muerte a nosotros, nuestros hijos y nuestro ganado a causa de la necesidad de agua?
Koma anthu anali ndi ludzu pamenepo ndipo anangʼungʼudza pamaso pa Mose namufunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto kuti ife, ana athu pamodzi ndi ziweto zathu tife ndi ludzu?”
4 Y Moisés, clamando al Señor, dijo: ¿Qué he de hacer con este pueblo? están casi listos para matarme apedreando.
Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, “Kodi ndichite chiyani ndi anthu awa? Iwo atsala pangʼono kundigenda ndi miyala.”
5 Y él Señor dijo a Moisés: Continúa delante del pueblo, y toma a algunos de los jefes de Israel contigo, y toma en tu mano la vara que estaba tendida sobre el Nilo, y vete.
Yehova anati kwa Mose, “Pita patsogolo pa anthuwo. Tenga ndodo imene unamenyera nyanja ya Nailo pamodzi ndi akuluakulu ena a Israeli ndi kunyamuka.
6 Mira, tomaré mi lugar delante de ti sobre la roca en Horeb; y cuando le das un golpe a la roca, saldrá agua de ella, y la gente beberá. Y Moisés lo hizo ante los ojos de los jefes de Israel.
Ine ndidzayima patsogolo pako pafupi ndi thanthwe la ku Horebu. Ukamenye thanthwelo, madzi adzatuluka kuti anthu amwe.” Motero Mose anachita zimenezi pamaso pa akuluakulu a Israeli.
7 Y dio a ese lugar el nombre de Masah y Meriba, porque los hijos de Israel se enojaron, y porque pusieron al Señor a prueba, diciendo: ¿Está el Señor con nosotros o no?
Ndipo iye anatcha malowo Masa ndi Meriba chifukwa Aisraeli anakangana ndi kuyesa Yehova ponena kuti, “Kodi pakati pathu pali Yehova kapena palibe?”
8 Entonces vino Amalec y peleó contra Israel en Refidim.
Amaleki anabwera ku Refidimu kudzamenyana ndi Aisraeli.
9 Y Moisés dijo a Josué: Juntanos una banda de hombres y sal a hacer guerra contra Amalec; mañana tomaré mi lugar en la cima del monte con la vara de Dios en mi mano.
Mose anati kwa Yoswa, “Sankha amuna amphamvu ndipo upite ukamenyane ndi Amaleki. Mawa ndidzayima pamwamba pa phiri nditagwira ndodo ya Mulungu.”
10 Entonces Josué hizo como Moisés le dijo, y fue a la guerra contra Amalec; y Moisés, Aarón y Hur subieron a la cima del monte.
Ndipo Yoswa anachitadi monga Mose anamulamulira. Iye anapita kukamenyana ndi Aamaleki ndipo Mose, Aaroni ndi Huri anapita pamwamba pa phiri.
11 Y mientras Moisés levantaba su mano, Israel era más fuerte; más cuando soltaba su mano, Amalec se hacía más fuerte.
Mose ankati akakweza manja ake, Aisraeli amapambana, koma akatsitsa manja akewo Amaleki amapambana.
12 Pero las manos de Moisés se cansaban; así que pusieron una piedra debajo de él y él se sentó en ella, Aarón y Hur apoyando sus manos, uno de un lado y el otro sobre el otro; así que mantuvieron sus manos sin caer hasta que el sol se puso.
Manja a Mose atatopa, Aaroni ndi Huri anatenga mwala ndi kuyika pansi ndipo Mose anakhalapo. Aaroni ndi Huri anagwirizitsa manja a Mose wina mbali ina winanso mbali ina. Choncho manja a Mose analimba mpaka kulowa kwa dzuwa.
13 Y Josué venció a Amalec y a su pueblo a espada.
Kotero Yoswa anagonjetsa asilikali ankhondo a Amaleki ndi lupanga.
14 Y el SEÑOR dijo a Moisés: Haz un registro de esto en un libro, para que se guarde en la memoria, y repítelo en los oídos de Josué: que todo recuerdo de Amalec será desarraigado por completo de la tierra.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Lemba izi mʼbuku kuti zidzakumbukirike ndipo uwonetsetse kuti Yoswa amve zimenezi, chifukwa Ine ndidzafafaniziratu Amaleki pa dziko lapansi, kotero kuti palibe amene adzawakumbukire.”
15 Entonces Moisés levantó un altar, y le dio el nombre Él Señor es mi estandarte:
Mose anamanga guwa lansembe ndipo analitcha Yehova Chipambano Changa (Yehova Nisi).
16 Porque dijo: Él Señor juró que habrá guerra contra Amalec de generación en generación.
Ndipo anati, “Kwezani mbendera ya Yehova. Yehova adzachitabe nkhondo ndi mibado yonse ya Aamaleki.”

< Éxodo 17 >