< Ester 10 >
1 Y el rey Asuero impuso un impuesto sobre la tierra y sobre las islas del mar.
Mfumu Ahasiwero anakhometsa msonkho mʼdziko lake lonse mpaka ku zilumba zonse.
2 Y todos sus actos de poder y su gran fuerza y la historia completa del lugar elevado que el rey dio a Mardoqueo, ¿no están registrados en el libro de la historia de los reyes de Media y Persia?
Ndipo ntchito zonse zochitika ndi mphamvu zake komanso ndi zonse zofotokoza za ukulu wa Mordekai, kukwezedwa kwake ndi mfumu, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Mediya ndi Peresiya?
3 Para Mardoqueo, el judío, era superado solo por el rey Asuero, y grande entre los judíos y respetado por el cuerpo de sus compatriotas; trabajando por el bien de su pueblo, y diciendo palabras de paz a toda su simiente.
Pakuti Mordekai Myuda uja anali wachiwiri wa mfumu Ahasiwero. Kwa Ayuda onse Mordekai anali munthu wamkulu ndipo ankamukonda chifukwa ankachitira zabwino mtundu wake ndi kufunira mtendere abale ake.