< Eclesiastés 4 >
1 Y nuevamente vi todas las cosas crueles que se hacen bajo el sol; estaba el llanto de aquellos que les habían hecho mal, y no tenían consolador; y de las manos de los malvados estaba el poder, pero no tenían consolador.
Ndinayangʼananso ndi kuona chipsinjo chimene chimachitika pansi pano: ndinaona misozi ya anthu opsinjika, ndipo iwo alibe owatonthoza; mphamvu zinali ndi anthu owapsinjawo ndipo iwonso analibe owatonthoza.
2 Mi alabanza fue para los muertos que han ido a su muerte, más que para los vivos que aún tienen vida.
Ndipo ndinanena kuti akufa, amene anafa kale, ndi osangalala kuposa amoyo, amene akanalibe ndi moyo.
3 Sí, más feliz que los muertos o los vivos parecía el que nunca ha estado, que no ha visto el mal que se hace bajo el sol.
Koma wopambana onsewa ndi amene sanabadwe, amene sanaone zoyipa zimene chimachitika pansi pano.
4 Y vi que la causa de todo el trabajo y de todo lo que está bien hecho era la envidia del hombre al prójimo. Esto de nuevo es para ningún propósito y aflicción de espíritu.
Ndipo ndinazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
5 El hombre necio, doblando sus manos, toma la carne de su propio cuerpo para comer.
Chitsiru chimangoti manja ake lobodo ndi kudzipha chokha ndi njala.
6 Una mano llena de descanso es mejor que dos manos llenas de problemas y aflicción de espíritu.
Nʼkwabwino kukhala ndi dzanja limodzi lodzaza uli pa mtendere, kuposa kukhala ndi manja awiri odzaza uli pa mavuto, ndipo uku nʼkungodzivuta chabe.
7 Luego volví y vi un ejemplo de lo que no tiene propósito bajo el sol.
Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano:
8 Es aquel que está solo, sin sucesor, y sin hijo o hermano; pero no hay fin a todo su trabajo, y él nunca tiene suficiente riqueza. ¿Para quién, entonces, estoy trabajando y manteniéndome del placer? Esto de nuevo no tiene ningún propósito, y es un trabajo amargo.
Panali munthu amene anali yekhayekha; analibe mwana kapena mʼbale. Ntchito yake yolemetsa sinkatha, ndipo maso ake sankakhutitsidwa ndi chuma chake. Iye anadzifunsa kuti, “Kodi ntchito yosautsayi ndikuyigwirira yani? Nanga nʼchifukwa chiyani ndikudzimana chisangalalo?” Izinso ndi zopandapake, zosasangalatsa!
9 Dos son mejores que uno, porque tienen una buena recompensa por su trabajo.
Kukhala awiri nʼkwabwino kuposa kukhala wekha, chifukwa ntchito ya anthu awiri ili ndi phindu:
10 Y si uno tiene una caída, el otro le dará una mano; pero infeliz es el hombre que está solo, porque no tiene ayudante.
Ngati winayo agwa, mnzakeyo adzamudzutsa. Koma tsoka kwa munthu amene agwa ndipo alibe wina woti amudzutse!
11 De nuevo, si dos están durmiendo juntos, son cálidos, pero ¿cómo puede uno ser cálido por sí mismo?
Komanso ngati anthu awiri agona malo amodzi, adzafunditsana. Koma nanga mmodzi angadzifunditse yekha?
12 Y dos atacados por uno estarían a salvo, y tres cuerdas torcidas juntas no se rompen rápidamente.
Munthu mmodzi angathe kugonjetsedwa, koma anthu awiri akhoza kudziteteza. Chingwe cha maulusi atatu sichidukirapo.
13 Un joven que es pobre y sabio es mejor que un rey que es viejo e insensato y no será guiado por la sabiduría de los demás.
Wachinyamata wosauka koma wanzeru aposa mfumu yokalamba koma yopusa imene simvanso malangizo.
14 Porque de la prisión el joven viene a ser rey, aunque al nacer solo era un hombre pobre en el reino.
Wachinyamatayo angathe kuchokera ku ndende ndi kudzakhala mfumu, kapena angathe kubadwa wosauka mʼdziko la mfumuyo.
15 Vi a todos los que vivían bajo el sol alrededor del joven que iba a ser gobernante en lugar del rey.
Ndipo ndinaona kuti iwo onse amene anakhala ndi moyo ndi kuyenda pansi pano anatsatira wachinyamatayo, amene anatenga malo a mfumu.
16 No hubo fin de todas las personas, de todos aquellos cuya cabeza era, pero los que vengan después no se deleitarán en él. Esto de nuevo no tiene ningún propósito y es aflicción de espíritu.
Mfumu ikhoza kulamulira anthu osawerengeka, komabe itamwalira, palibe amene adzayamikire zomwe mfumuyo inachita. Izinso ndi zopandapake, nʼkungozivuta chabe.