< Deuteronomio 7 >

1 Cuando el Señor tu Dios los lleve a la tierra donde van, que será tu herencia, y expulsara a las naciones de delante de ti, los hititas y los gergeseos y los amorreos y los cananeos y los ferezeos los heveos y los jebuseos, siete naciones más grandes y más fuertes que tú;
Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
2 Y cuando el Señor te haya entregado en tus manos y los hayas vencido, destrúyelos por completo. No hagas pacto con ellos, y no tengan piedad de ellos.
Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
3 No tomen esposas o esposos de entre ellos; no darás tus hijas, a sus hijos, ni las tomen para tus hijos.
Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
4 Porque a través de ellos sus hijos se volverán de mí a la adoración de otros dioses, y el Señor se moverá a la ira contra ti y te enviará la destrucción rápidamente.
Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
5 Pero esto es lo que deben hacerles: sus altares deben ser derribados y sus pilares destrozados, y sus árboles sagrados y sus imágenes quemadas con fuego.
Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
6 Porque son un pueblo santo para el Señor tu Dios: marcado por el Señor tu Dios para ser su pueblo especial de todas las naciones en la faz de la tierra.
Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
7 El Señor no les dio su amor ni los tomó para sí mismo porque eran más numeroso que cualquier otra persona; porque ustedes eran el más pequeño de las naciones;
Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
8 Pero debido a su amor por ustedes, y para mantener su juramento a sus padres, el Señor los sacó con la fuerza de su mano, liberándolos de la esclavitud de la mano de Faraón, rey de egipto.
Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
9 Entonces conoce de que el Señor tu Dios es Dios; él Dios fiel, que guarda su pacto y misericordia, a través de mil generaciones para aquellos que lo aman y guardan sus leyes;
Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
10 Recompensando a sus enemigos en su rostro con destrucción; no tendrá piedad de quienes le odian, sino que les dará un castigo.
Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
11 Así que guarda las órdenes y las leyes y las decisiones que les doy hoy y hazlas.
Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
12 Y será que si prestas atención a estas decisiones y las guardas y las cumples, entonces el Señor mantendrá su pacto con ustedes y su misericordia, como dijo en su juramento a tus padres.
Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
13 Y él les dará su amor, bendiciéndolos y multiplicándolos, enviará su bendición sobre su descendencia y el fruto de su tierra, su grano y su vino y su aceite, el aumento de su ganado. y las crías de su rebaño, en la tierra que por su juramento a su padres se comprometió a darles.
Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
14 Tendrán mayores bendiciones que cualquier otro pueblo; ningún hombre o mujer entre ustedes o entre su ganado quedará sin descendencia.
Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
15 Y el Señor les quitará todas las enfermedades, y no les pondrá ninguna de las enfermedades malignas de Egipto que han visto, sino que las pondrá sobre sus enemigos.
Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
16 Y Deben enviar destrucción sobre todos los pueblos que el Señor su Dios entregue en sus manos; no tengan piedad de ellos, y no le den adoración a sus dioses; porque eso será causa de pecado para ustedes.
Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
17 Si dicen en sus corazones, estas naciones son más numerosas que nosotros: ¿cómo vamos a quitarles su tierra?
Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
18 No temas a ellos, pero ten en cuenta lo que el Señor tu Dios hizo a Faraón y a todo Egipto;
Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
19 Los grandes castigos que sus ojos vieron, y las señales y maravillas, y la mano fuerte y el brazo extendido, mediante el cual el Señor su Dios los sacó: así hará el Señor su Dios a todos los pueblos. Así mismo hará con quienes son la causa de sus temores.
Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
20 Y el Señor enviará un avispón entre ellos, hasta que todos los demás que se han mantenido a salvo de ustedes en lugares secretos hayan sido cortados.
Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
21 No tengas miedo de ellos, porque el Señor su Dios está en medio de ustedes, un gran Dios para ser temido.
Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
22 El Señor su Dios expulsará las naciones delante de ustedes poco a poco; no deben ser eliminados rápidamente, por temor a que las bestias del campo aumenten demasiado contra ustedes.
Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
23 Pero el Señor su Dios los entregará en sus manos, dominándolos hasta que su destrucción sea completa.
Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
24 Él entregará sus reyes a sus manos, y ustedes pondrán sus nombres fuera de la existencia bajo el cielo; no hay ninguno de ellos que no ceda ante ustedes, hasta que su destrucción sea completa.
Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
25 Las imágenes de sus dioses deben ser quemadas con fuego. No tengan ningún deseo por el oro y la plata en ellos, y no lo tomen para ustedes mismos, ya que será un peligro para ustedes: es algo desagradable para el Señor tu Dios.
Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
26 Y no pueden llevar una cosa abominable a tu casa, porque como tal serán destruidos junto con ellos, pero manténganse alejados de ella con temor y odio, porque es una cosa maldita.
Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.

< Deuteronomio 7 >