< Daniel 11 >

1 Yo también, en el primer año de Darío de Mede estaba de su lado para asegurar su posición y hacerlo fuerte.
Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
2 Y ahora te declararé lo que es verdad. Todavía hay tres reyes por venir en Persia, y el cuarto tendrá una riqueza mucho mayor que todos ellos; y cuando se haya fortalecido a través de su riqueza, pondrá sus fuerzas en movimiento contra todos los reinos de Grecia.
“Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
3 Y un rey fuerte llegará al poder, gobernando con gran autoridad y haciendo lo que le plazca.
Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
4 Y cuando se haya fortalecido, su reino será quebrantado y separado a los cuatro vientos del cielo; pero no a su descendencia, porque será desarraigada; ni según él señorío que él ejerció y su reino será para los demás y no para estos.
Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
5 Y el rey del sur será fuerte, pero uno de sus capitanes será más fuerte que él y será gobernante; y su dominio será una gran dominio.
“Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
6 Y al final de los años se unirán; y la hija del rey del sur vendrá al rey del norte para llegar a un acuerdo, pero no mantendrá la fuerza de su brazo; y su descendencia no mantendrá su lugar; pero ella será desarraigada, con aquellos que fueron la causa de su venida, y quién la engendró, y el que la fortaleció en esos tiempos.
Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
7 Pero de una rama de sus raíces se levantará para tomar su lugar, quién vendrá contra el ejército, forzando su camino hacia el lugar fuerte del rey del norte, y luchará contra ellos y prevalecerá:
“Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
8 Y llevará a sus dioses y sus imágenes de metal y sus bellas vasijas de plata y oro a Egipto; y por algunos años se mantendrá alejado del rey del norte.
Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
9 Y vendrá al reino del rey del sur, pero volverá a su tierra.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
10 Y sus hijos harán la guerra, y reunieron un ejército de grandes fuerzas, y lo atacará, inundando y pasará adelante; y volverá a llevar la guerra incluso a su fortaleza.
Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
11 Y el rey del sur se moverá con ira, y saldrá y hará guerra contra él, en este mismo rey del norte; y él reunirá un gran ejército, pero el ejército será entregado a su mano.
“Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
12 Y el ejército será quitado, y su corazón se llenará de orgullo; él será la causa de la caída de miles, pero no prevalecerá.
Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
13 Y nuevamente el rey del norte reunirá un ejército mayor que el primero; y lo atacará al final de los años, con un gran ejército y mucha riqueza.
Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
14 En aquellos tiempos, un número tomará las armas contra el rey del sur; y los hijos de los violentos entre tu pueblo se levantarán para hacer realidad la visión; pero será su caída.
“Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
15 Entonces vendrá el rey del norte, construirá una rampa y tomará una ciudad de las más fortificadas; y las fuerzas del rey del sur harán un intento por mantener su posición, incluso lo mejor de su ejército, pero no tendrán fuerzas para resistir.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
16 Y el que viene contra él hará lo que le plazca, y nadie podrá mantener su lugar delante de él; tomará su posición en la Tierra hermosa, y en su poder será consumida.
Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
17 Y puso su rostro delante para venir con la fuerza de todo su reino, hará cosas rectas con él; y él le dará a la hija de una mujer para destruirle; pero no lo respaldará ni estará de su lado.
Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
18 Después de esto, su rostro se volverá hacia las islas, y tomará varias de ellas: pero un gobernante, pondrá fin a su oprobio; y más que esto, hará que su vergüenza vuelva sobre él.
Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
19 Entonces su rostro se volverá hacia los lugares fuertes de su tierra; pero su camino se detendrá, causando su caída, y no volverá a ser visto.
Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
20 Entonces su lugar será ocupado por alguien que enviará a un hombre con la gloria de un rey para juntar riquezas; pero después de un corto tiempo la destrucción lo alcanzará, pero no en ira o en la lucha.
“Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
21 Y su lugar será ocupado por una persona despreciable, a quien no se le había dado el honor del reino; pero vendrá en tiempo de paz y obtendrá el reino con palabras lisonjeras.
“Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
22 Y sus fuerzas serán quitadas completamente de delante de él y quebrantadas; e incluso el gobernante del pacto tendrá el mismo destino.
Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
23 Y desde el momento en que lleguen a un acuerdo con él, actuará con engaño; porque tomará las armas de repente con una poca gente y vencerá,
Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
24 Contra los lugares fértiles, y hará que la basura sea parte del país; y él hará lo que sus padres no hicieron, o los padres de sus padres; distribuirá entre ellos bienes tomados en la guerra y por la fuerza; despojos, botines y riquezas; planeará sus ataques contra los lugares fuertes por un tiempo.
Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
25 Y animado por su poder y su valor contra el rey del sur con un gran ejército; y el rey del sur irá a la guerra con un ejército muy grande y fuerte; pero se verá obligado a ceder, debido a que fue traicionado;
“Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
26 Y los mismos que comían de su mesa lo destruirán, y su ejército vendrá a la destrucción completa, y muchos caerán muertos.
Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
27 Y en cuanto a estos dos reyes, sus corazones estarán fijos en hacer el mal él uno al otro y dirán mentiras él uno al otro en una mesa; pero no llegará a nada; porque el final será en el momento fijado.
Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
28 Y él volverá a su tierra con gran riqueza; y su corazón estará en contra del santo pacto; y él hará su placer y volverá a su tierra.
Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
29 A la hora fijada regresará y entrará al sur; pero en el tiempo posterior ya no será como él primero.
“Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
30 Porque los barcos de Quitim vendrán contra él, y él se desanimará, volverá lleno de ira contra el pacto santo; y actuará contra él; y él regresará y se entenderá con aquellos que han renunciado al pacto santo.
Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
31 Y los ejércitos enviados por él tomarán su posición y profanaran el lugar santo, incluso la fortaleza, y quitarán la ofrenda quemada regular y pondrán en su lugar una cosa inmunda que causa desolación.
“Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
32 Y aquellos que hacen el mal en contra del pacto, los hará apostar con sus palabras lisonjeras; pero las personas que tengan conocimiento de su Dios serán fuertes y actuarán.
Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
33 Y los que sean sabios entre la gente serán los maestros de muchos; pero caerán por la espada y por el fuego, siendo prisioneros y sufriendo despojo por mucho tiempo.
“Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
34 Ahora, en el momento de su caída, recibirán un poco de ayuda, pero se les unirán muchos con lisonjas.
Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
35 Y algunos de los sabios caerán para ser refinados, purificados y emblanquecidos hasta el tiempo del fin; porque todavía está por venir el tiempo fijo.
Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
36 Y el rey hará lo que le plazca; se pondrá en alto, se alzará sobre cada dios y dirá cosas contra el Dios de los dioses; y hablará maravillas y prosperará hasta que se complete la ira; porque lo que se ha decretado se cumplira.
“Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
37 No tendrá respeto por los dioses de sus padres ni por el dios favoritos por las mujeres; no tendrá respeto por ningún dios; porque se ensalzará a sí mismo por sobre todos.
Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
38 Pero en lugar de esto, honrará al dios de las fortalezas, y a un dios del que sus padres no tenían conocimiento, honrará con oro, plata, joyas y cosas de gran valor.
Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
39 Y hará uso de la gente de un dios extraño para hacer fortalezas; Y aquellos de quienes que le reconozcan, dará un gran honor; y los convertirá en gobernantes sobre muchos, y hará que la tierra se divida por un precio.
Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
40 Y al tiempo del fin, el rey del sur lo atacará; y el rey del norte vendrá contra él como un viento de tormenta, con carruajes de guerra, jinetes y numerosos barcos; y atravesará muchas tierras, vencerá y pasará.
“Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
41 Y vendrá a la Tierra hermosa, y decenas de miles serán vencidos; pero se evitará que caigan en sus manos: Edom y Moab y el jefe de los hijos de Ammon.
Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
42 Y su mano se extenderá sobre los países; y Egipto no estará a salvo de él.
Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
43 Pero él tendrá poder sobre las reservas de oro y plata, y sobre todas las cosas valiosas del sur; y los libios y los etíopes estarán a sus pies.
Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
44 Pero las noticias del este y del norte lo perturbarán; y él saldrá con gran ira, para enviar destrucción y acabar con muchos.
Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
45 Pondrá las carpas de su gran tabernáculo entre el mar y la hermosa montaña sagrada; pero llegará a su fin, y no habrá quien le ayude.
Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”

< Daniel 11 >