< Amós 3 >

1 Escucha esta palabra que el Señor ha dicho contra ti, hijos de Israel, contra toda la familia que saqué de la tierra de Egipto, diciendo:
Inu Aisraeli, imvani mawu awa amene Yehova wayankhula kutsutsana nanu, kutsutsana ndi banja lonse limene analitulutsa mu Igupto:
2 Solo a ti de todas las familias de la tierra me he escogido; por esta razón les enviaré castigo por todos sus pecados.
“Inu nokha ndi amene ndinakusankhani pakati pa mabanja onse a dziko lapansi; nʼchifukwa chake ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu onse.”
3 ¿Es posible que dos vayan caminando juntos, si no es por acuerdo?
Kodi anthu awiri nʼkuyendera limodzi asanapangane?
4 ¿Un león dará su fuerte rugir en el bosque cuando no haya comida? ¿La voz del cachorro sonará desde su agujero si no ha apresado algo?
Kodi mkango umabangula mʼnkhalango usanagwire nyama? Kodi msona wamkango umalira mʼphanga mwake pamene sunagwire kanthu?
5 ¿Es posible que un pájaro sea llevado a una red sin haber cazador? ¿Se levantará la red de la tierra si no ha atrapado nada?
Kodi mbalame nʼkutera pa msampha pamene palibe nyambo yake? Kodi msampha umafwamphuka usanakole kanthu?
6 Si suena la bocina en la ciudad, ¿no estará llena de miedo la gente? ¿vendrá el mal a una ciudad si el Señor no lo ha hecho?
Kodi pamene lipenga la nkhondo lalira mu mzinda, anthu sanjenjemera? Pamene tsoka lafika mu mzinda, kodi si Yehova amene wachititsa zimenezo?
7 Ciertamente el Señor no hará nada sin dejar en claro su secreto a sus siervos, los profetas.
Zoonadi Ambuye Yehova sachita kanthu asanawulule zimene akufuna kuchita kwa atumiki ake, aneneri.
8 Si suena el rugir del león; ¿Quién no tendrá miedo? El Señor Dios ha dicho la palabra; ¿Es posible que el profeta se calle?
Mkango wabangula, ndani amene sachita mantha? Ambuye Yehova wayankhula, ndani amene sanganenere?
9 Proclamen las noticias en las grandes casas de Asdod y en la tierra de Egipto, y digan: Reúnase en las montañas de Samaria, y vean qué grandes tumultos hay en medio de ella, y qué actos crueles se hacen en ella.
Lengezani zimenezi ku nyumba zaufumu za ku Asidodi ndiponso ku nyumba zaufumu za ku Igupto: “Sonkhanani ku mapiri a ku Samariya; onani chisokonezo pakati pake ndiponso kuponderezana pakati pa anthu ake.”
10 Porque no tienen conocimiento de cómo hacer lo correcto, dice el Señor, los que acumulan violencia y destrucción en sus palacios.
“Iwo sadziwa kuchita zolungama, ndipo amadzaza malo awo otetezedwa ndi zinthu zolanda ku nkhondo ndi zakuba,” akutero Yehova.
11 Por esta razón, dice el Señor, vendrá un adversario, rodeándote en la tierra por todos lados; y tu fuerza caerá y tus palacios serán destruidos.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akunena izi: “Mdani adzalizungulira dzikoli; iye adzagwetsa malinga ako, ndi kufunkha nyumba zako zaufumu.”
12 Estas son las palabras del Señor: Como el criador de ovejas saca de la boca del león dos patas o parte de una oreja; así serán arrebatados los hijos de Israel, que descansan en Samaria en la esquina de una cama o en los cojines de seda de un sofá.
Yehova akuti, “Monga mʼbusa amalanditsa mʼkamwa mwa mkango miyendo iwiri yokha kapena msonga yokha ya khutu, moteronso ndimo mmene adzapulumukire Aisraeli amene amakhala mu Samariya pa msonga za mabedi awo, ndi ku Damasiko pa akakhutagona awo.”
13 Escucha ahora y da testimonio contra la familia de Jacob, dice el Señor Dios, el Dios de los ejércitos;
“Imvani izi ndipo mupereke umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo,” akutero Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
14 Porque en el día en que yo castigue a Israel por sus pecados, enviaré castigo sobre los altares de Betel, y los cuernos del altar serán cortados y descenderán a la tierra.
“Pa tsiku limene ndidzalange Israeli chifukwa cha machimo ake, ndidzagumula maguwa ansembe a ku Beteli; nyanga za guwa zidzathyoka ndipo zidzagwa pansi.
15 Y enviaré destrucción a la casa de invierno con la casa de verano; y también casas de marfil perecerán y los palacios serán destruidos, dice el Señor.
Ndidzagwetsa nyumba ya pa nthawi yozizira pamodzi ndi nyumba ya pa nthawi yotentha; nyumba zokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu zidzawonongedwa ndipo nyumba zikuluzikulu zidzaphwasulidwa,” akutero Yehova.

< Amós 3 >