< 2 Samuel 11 >
1 Ahora en la primavera, cuando los reyes salen a la guerra, David envió a Joab y sus siervos y todo Israel con él; y destruyeron la tierra de los hijos de Amón, y tomaron su posición ante Rabá, sitiaron. Pero David se quedó en Jerusalén.
Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Davide anatumiza Yowabu ndi ankhondo a mfumu pamodzi ndi gulu lonse lankhondo la Aisraeli. Iwo anawononga Aamoni ndi kuzungulira mzinda wa Raba. Koma Davide anatsala ku Yerusalemu.
2 Una tarde, David se levantó de su cama y, mientras caminaba por el techo de la casa del rey, vio a una mujer bañándose; Y la mujer era muy hermosa.
Tsiku lina cha kumadzulo Davide anadzuka pa bedi lake ndipo ankayenda pamwamba pa nyumba yake. Ali pa dengapo anaona mkazi akusamba. Mkaziyo anali wokongola kwambiri.
3 Y David envió a averiguar quién era la mujer. Y uno dijo: ¿No es ésta Betsabé, la hija de Eliam, la esposa de Urías, el hitita?
Ndipo Davide anatuma munthu wina kuti akafufuze za iye. Munthuyo anati, “Kodi uyu si Batiseba, mwana wa Eliamu, mkazi wa Uriya Mhiti?”
4 Entonces David la envió y la tomó; y ella vino a él, y él la llevó a su cama. Después de que se purificó de su inmundicia; luego regresó a su casa.
Ndipo Davide anatumiza amithenga kwa iye kukamuyitana. Batiseba anabwera kwa Davide ndipo anagona naye. (Nʼkuti mkaziyu atayeretsedwa ku masiku ake osamba). Kenaka anabwerera ku nyumba yake.
5 Y la mujer quedó embarazada. y ella le dijo a David que estaba embarazada.
Mkaziyo anakhala woyembekezera ndipo anatumiza mawu kwa Davide kunena kuti, “Ine ndine woyembekezera.”
6 Entonces envió David a Joab, diciendo: Envíame a Urías el hitita. Y Joab envió a Urías a David.
Ndipo Davide anatumiza mawu awa kwa Yowabu: “Nditumizire Uriya Mhiti.” Ndipo Yowabu anamutumiza kwa Davide.
7 Y cuando Urías se acercó a él, David le hizo preguntas sobre cómo era Joab y el pueblo, y cómo iba la guerra.
Uriya atafika kwa Davide, Davide anamufunsa za momwe analili Yowabu, za asilikali ndi momwe nkhondo inkayendera.
8 Entonces David dijo a Urías: Baja a tu casa, y lava tus pies. Y Urías se fue de la casa del rey, y una ofrenda del rey fue enviada tras él.
Kenaka Davide anati kwa Uriya, “Pita ku nyumba yako ukapumule.” Choncho Uriya anachoka ku nyumba yaufumu, ndipo mfumuyo inatumiza mphatso kwa Uriya.
9 Pero Urías tomó su descanso en la puerta de la casa del rey, con todos los siervos de su señor, y no bajó a su casa.
Koma Uriya anagona pa chipata cha nyumba yaufumu pamodzi ndi antchito onse a mbuye wake ndipo sanapite ku nyumba yake.
10 Y cuando se le dijo a David que Urías no había bajado a su casa, David le dijo a Urías, ¿No has venido de un viaje? ¿Por qué no fuiste a tu casa?
Davide atawuzidwa kuti, “Uriya sanapite ku nyumba yake.” Iye anafunsa kuti, “Kodi iwe sunachokera kutali? Nʼchifukwa chiyani sunapite ku nyumba yako?”
11 Y Urías dijo a David: Israel y Judá con el arca viven en tiendas, y mi señor Joab y los otros siervos de mi señor duermen en campo abierto; ¿Debo ir a mi casa y comer y beber, y acostarme con mi esposa? Por el Señor vivo, y por la vida de tu alma, no haré tal cosa.
Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”
12 Entonces David dijo a Urías: Estate aquí hoy, y después de eso te dejaré ir. Entonces Urías estuvo en Jerusalén ese día y el siguiente.
Ndipo Davide anati kwa iye, “Ukhale konkuno tsiku lina limodzi, ndipo mawa ndikulola kuti upite.” Kotero Uriya anakhala mu Yerusalemu tsiku limenelo ndi tsiku linalo.
13 Y enviándole David, David comió y bebió, y David logró emborracharlo. Y al caer la noche, se fue a descansar en su cama con los criados de su señor, pero él No bajó a su casa.
Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.
14 A la mañana siguiente, David le dio a Urías una carta para llevar a Joab.
Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya.
15 Y en la carta dijo: Ten cuidado de poner a Urías en el frente de la línea, donde la lucha es más violenta, y déjenlo solo, para que pueda ser vencido y condenado a muerte.
Mʼkalatayo analembamo kuti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha kuti akanthidwe ndi kufa.”
16 Entonces, mientras Joab observaba la ciudad, puso a Urías en el lugar donde estaba claro para él que eran los mejores guerreros.
Kotero Yowabu atawuzinga mzindawo, anamuyika Uriya pamalo pamene amadziwa kuti pali asilikali amphamvu.
17 Salieron los hombres de la ciudad y se pelearon con Joab; y varios de los hombres de David murieron en la lucha, y con ellos Urías el hitita.
Ankhondo a mu mzindawo atabwera kudzamenyana ndi Yowabu, anthu ena a gulu la ankhondo la Davide anaphedwa ndipo Uriya Mhiti uja anaphedwanso.
18 Entonces Joab envió a David noticias de todo lo que había ocurrido en la guerra:
Yowabu anatumiza wamthenga kwa Davide kukafotokoza mwatsatanetsatane za nkhondoyo.
19 Y dio órdenes al hombre que recibió la noticia, diciendo: Después de que le hayas dado al rey todas las noticias sobre la guerra,
Iye anamulangiza wa mthengayo kuti, “Pamene ukatsiriza kufotokozera mfumu za ku nkhondozi,
20 Si el rey está enojado y dice: ¿Por qué te acercaste tanto al pueblo para pelear? ¿No era cierto que sus arqueros estarían en la pared?
mfumu ikapsa mtima, ndipo akakakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani munapita pafupi ndi mzindawo kukamenya nkhondo? Inu simunadziwe kuti atha kukuponyerani mivi kuchokera pa khoma?
21 ¿Quién mató a Abimelec, hijo de Jerobaal? ¿Acaso una mujer no le arrojó una gran piedra desde la pared y lo mató en Thebez? ¿Por qué te acercaste tanto a la pared? Entonces dile: Tu siervo Urías el hitita está entre los muertos.
Kodi anapha Abimeleki mwana wa Yerubeseti ndani? Kodi mkazi sanamuponyere mphero kuchokera pa khoma? Kotero kuti anakafera ku Tebezi. Nʼchifukwa chiyani munafika pafupi ndi khoma?’ Ngati iye akafunsa zimenezi, iwe ukanene kwa iye kuti, ‘Mtumiki wanunso Uriya Mhiti wafa.’”
22 Entonces el hombre fue y vino a David, y le dio todas las noticias que Joab le había enviado para dar; luego David se enojó con Joab y dijo: ¿Por qué te acercaste tanto a la ciudad para la pelea? ¿No era cierto que sus arqueros estarían en la pared? ¿Quién mató a Abimelec, el hijo de Jerobaal? ¿Acaso una mujer no le arrojó una gran piedra desde la pared y lo mató en Thebez? ¿Por qué te acercaste tanto a la pared?
Mthengayo ananyamuka, ndipo atafika anamuwuza Davide zonse zimene Yowabu anamutuma kuti akanene.
23 Y el hombre dijo a David: En verdad, los hombres nos vencieron y salieron contra nosotros al campo abierto, pero los enviamos de regreso a las mismas puertas del pueblo.
Mthengayo anati kwa Davide, “Anthuwo anatiposa mphamvu ndipo anabwera kudzalimbana nafe poyera, koma ife tinawabwezera ku chipata cha mzindawo.
24 Y los arqueros enviaron sus flechas a tus siervos desde el muro, y algunos de los siervos del rey murieron, y entre ellos está tu siervo Urías el hitita.
Ndipo anthu oponya mivi anatiponyera kuchokera pa khoma, anthu ena a mfumu afa. Kuwonjezera apo, mtumiki wanu Uriya Mhiti wafanso.”
25 Entonces David dijo al hombre: Ve y dile a Joab: No permitas que esto te cause pena; porque un hombre puede llegar a su muerte por la espada como otro: lucha aún más fuerte contra la ciudad, y tomarla: y anímalo.
Davide anamuwuza mthengayo kuti, “Ukanene izi kwa Yowabu: ‘Zimenezi zisakukhumudwitse; lupanga limapha wina nthawi zinanso wina. Limbikitsa nkhondo pa mzindawo ndipo uwuwononge!’ Ukanene zimenezi pomulimbikitsa Yowabu.”
26 Y cuando la esposa de Urías tuvo noticias de que su esposo había muerto, ella se entregó a llorar por él.
Mkazi wa Uriya atamva kuti mwamuna wake wafa, analira maliro.
27 Y cuando pasaron los días de llanto, David la llamó y la llevó a su casa, y ella se convirtió en su esposa y le dio un hijo. Pero el Señor no estaba complacido con lo que David había hecho.
Nthawi yolira maliro itatha, Davide anamubweretsa ku nyumba yake, ndipo anakhala mkazi wake nabala mwana wamwamuna. Koma Yehova sanakondwe ndi zimene Davide anachitazo.