< 2 Crónicas 7 >

1 Ahora, cuando las oraciones de Salomón terminaron, el fuego bajó del cielo, quemando todas las ofrendas; y el templo se llenó de la gloria de él Señor.
Solomoni atamaliza kupemphera, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kutentha nsembe zopsereza ndi nsembe zina, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulunguyo.
2 Y los sacerdotes no pudieron entrar en el templo del Señor, porque la casa del Señor estaba llena de la gloria del Señor.
Ansembe sanathe kulowa mʼNyumba ya Mulungu chifukwa munadzaza ulemerero wa Yehova.
3 Y todos los hijos de Israel estaban mirando cuando el fuego bajó, y la gloria del Señor estaba en la casa; y se arrodillaron, con sus caras hacia la tierra, adorando y alabando al Señor, y diciendo: Él es bueno; porque su misericordia es para siempre.
Aisraeli onse ataona moto ukuchokera kumwamba ndi ulemerero wa Yehova pamwamba pa Nyumba ya Mulungu, anagwada poyalidwa miyalapo ndipo anagunditsa nkhope zawo pansi, ndi kulambira ndi kutamanda Yehova, ponena kuti, “Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala chikhalire”
4 Entonces el rey y todo el pueblo hicieron ofrendas delante del Señor.
Tsono mfumu ndi anthu onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova.
5 El rey Salomón hizo una ofrenda de veintidós mil bueyes y ciento veinte mil ovejas. Así que el rey y todo el pueblo celebraron la fiesta de la dedicación del templo de Dios.
Ndipo mfumu Solomoni anapereka nsembe ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Kotero mfumu ndi anthu onse anachita mwambo wopereka Nyumba kwa Mulungu.
6 Y los sacerdotes estaban en sus lugares, y los levitas con sus instrumentos musicales para el canto del Señor, que David el rey había hecho para la alabanza del Señor, cuya misericordia es para siempre, cuando David cantaba con ellos y los sacerdotes sonaron cuernos delante de ellos; y todo Israel estaba de pie.
Ansembe anayimirira mʼmalo mwawo, monganso anachitira Alevi ndi zida zoyimbira za Yehova, zimene Davide anapanga zotamandira Yehova ndipo zimagwiritsidwa ntchito pamene amatamanda, ponena kuti, “Chikondi chake chikhale chikhalire.” Moyangʼanizana ndi Alevi, ansembe amaliza malipenga, ndipo Aisraeli onse anali atayimirira.
7 Entonces Salomón santificó la mitad del atrio frente al templo del Señor, ofreciendo allí las ofrendas quemadas y la grasa de las ofrendas de paz; porque no había lugar en el altar de bronce que Salomón había hecho para todas las ofrendas quemadas y las ofrendas de cereales y la grasa.
Solomoni anapatula malo a pakati pa bwalo kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndipo pamenepo anapereka nsembe zopsereza ndi mafuta, zopereka za chiyanjano, chifukwa guwa lansembe lamkuwa limene anapanga panalibe malo woti nʼkuperekerapo nsembe zopsereza, nsembe za ufa ndi mafuta.
8 Así que Salomón celebró la fiesta en ese tiempo durante siete días, y todo Israel con él, una reunión muy grande, porque la gente se había reunido desde Hamat y hasta el río de Egipto.
Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero kwa masiku asanu ndi awiri pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku chigwa cha ku Igupto.
9 Y al octavo día tuvieron una reunión santa; Las ofrendas para santificar el altar duraron siete días, y la fiesta solemne duró siete días.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panali msonkhano, pakuti anachita mwambo wopereka guwa lansembe kwa masiku asanu ndi awiri ndi masiku enanso asanu ndi awiri achikondwerero.
10 Y a los veintitrés días del mes séptimo, envió a la gente a sus tiendas, llenos de gozo y alegría en sus corazones, por todo el bien que el Señor había hecho a David a Salomón y a Israel su pueblo.
Pa tsiku la 23 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Solomoni anawuza anthu aja kuti apite kwawo. Anthu anali achimwemwe ndi okondwa mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira Davide ndi Solomoni ndiponso anthu ake Aisraeli.
11 Entonces Salomón llegó al final de la construcción del templo del Señor y del palacio del rey; y todo lo que estaba en su mente para hacer en él templo del Señor y para sí mismo había sido bien hecho.
Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene zinali mu mtima mwake pa Nyumba ya Yehova ndi nyumba yake yaufumu,
12 Entonces el Señor vino a Salomón en una visión nocturna y le dijo: He escuchado tu oración, y he tomado este lugar para mí como una casa donde se deben hacer ofrendas.
Yehova anamuonekera usiku ndipo anati: “Ine ndamva pemphero lako ndipo ndadzisankhira malo ano kukhala Nyumba yanga yoperekeramo nsembe.
13 Si, en mi palabra, el cielo está cerrado, para que no llueva, o si envío langostas sobre la tierra para su destrucción, o si envío enfermedad a mi pueblo;
“Ine ndikatseka kumwamba kuti mvula isagwe, kapena kulamulira dzombe kuti liwononge dziko, kapena kutumiza mliri pakati pa anthu,
14 Si mi pueblo, de quien recibe mi nombre, se humilla y se acerca a mí en oración, buscándome y apartándose de sus malos caminos; entonces escucharé desde el cielo, ignorando su pecado, y sanaré su tierra.
ngati anthu anga, amene amatchedwa ndi dzina langa adzichepetsa ndi kupemphera ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zawo zoyipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwamba ndipo ndidzakhululuka tchimo lawo ndi kuchiritsa dziko lawo.
15 Ahora mis ojos estarán abiertos y mis oídos atentos a las oraciones hechas en este lugar.
Ndipo maso anga adzatsekuka ndi makutu anga adzakhala tcheru kumva mapemphero a pamalo pano.
16 Porque he tomado esta casa para mí y la he santificado, para que mi nombre esté allí para siempre; y mis ojos y mi corazón estarán allí en todo momento.
Ine ndasankha ndipo ndapatula Nyumba yangayi kotero kuti ndidzakhala mʼmenemo kwamuyaya. Maso ndi mtima wanga zidzakhala pano nthawi zonse.
17 Y en cuanto a ti, si sigues tu camino delante de mí como lo hizo David tu padre, haciendo lo que te he ordenado y guardando mis leyes y mis decisiones:
“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula, ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
18 Entonces fortaleceré el trono de tu reino, según el pacto que le di a David, tu padre, diciendo: Nunca estarás sin un hombre que sea gobernante en Israel.
Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu, monga ndinachitira pangano ndi abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu wolamulira Israeli.’
19 Pero si te apartas de mí, y no guardas mis órdenes y mis leyes que he puesto delante de ti, sino vas y sirves a otros dioses, dándoles adoración:
“Koma ngati iwe udzapatuka ndi kutaya malangizo ndi malamulo amene ndakupatsa ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
20 Entonces haré que esta gente sea desarraigada de la tierra que les he dado; y esta casa, que he santificado para mi nombre, la apartaré de mis ojos, y la convertiré en un ejemplo y una palabra de vergüenza entre todos los pueblos.
pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko langa limene ndinawapatsa, ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndadzipatulira. Ndipo udzakhala ngati mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
21 Y este templo se convertirá en un montón de muros rotos, y todos los que pasen serán vencidos con asombro, y dirán: ¿Por qué el Señor lo ha hecho así a esta tierra y a este templo?
Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
22 Y su respuesta será: Porque fueron rechazados del Señor, el Dios de sus padres, que los sacaron de la tierra de Egipto, y tomaron para sí otros dioses y los adoraron y se convirtieron en sus sirvientes. por eso ha enviado todo este mal sobre ellos.
Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova, Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”

< 2 Crónicas 7 >