< 2 Crónicas 5 >

1 Así que toda la obra que Salomón hizo para la casa del Señor fue completa. Y Salomón tomó las cosas que David su padre había dado y consagrado, la plata y el oro y todas las vasijas, y las puso en los tesoros de la casa de Dios.
Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.
2 Entonces Salomón envió a todos los hombres responsables de Israel, a todos los jefes de las tribus y a los jefes de familia de los hijos de Israel, para que vinieran a Jerusalén y trasladaran el cofre del pacto del Señor fuera de la ciudad de David, que es Sión.
Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide.
3 Y todos los hombres de Israel se reunieron con el rey en la fiesta en el séptimo mes.
Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
4 Vinieron todos los hombres responsables de Israel, y los levitas tomaron el cofre del pacto.
Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano,
5 Tomaron el cofre del pacto y la tienda de reunión y todos los vasos sagrados que estaban en la tienda; todos estos, los sacerdotes, los levitas, tomaron.
ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula,
6 Y el rey Salomón y todos los hombres de Israel que se habían reunido allí con él, estaban ante él cofre del pacto, haciendo ofrendas de ovejas y bueyes más de lo que podrían ser contados.
ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.
7 Y los sacerdotes tomaron el cofre del pacto del Señor y la pusieron en su lugar, en la habitación interior de la casa, en el Lugar Santísimo, bajo las alas de los querubines.
Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi.
8 Porque sus alas estaban extendidas sobre el lugar donde estaba el cofre del pacto, cubriendo el cofre y sus varas.
Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira.
9 Las varillas eran tan largas que sus extremos se veían desde el lugar santo delante del Lugar Santísimo, pero no fueron vistos desde afuera; y allí están hasta hoy.
Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino.
10 No había nada en el arca, excepto las dos piedras planas que Moisés colocó allí en Horeb, donde el Señor hizo un pacto con los hijos de Israel cuando salieron de Egipto.
Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
11 Cuando los sacerdotes salieron del lugar santo, porque todos los sacerdotes que estaban presentes se purificaron, sin guardar sus divisiones;
Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera.
12 Y los levitas que hacían la música, todos ellos, Asaf, Hemán, Jedutún y sus hijos y hermanos, vestidos de lino, estaban en sus lugares con sus instrumentos de bronce y cuerdas en el lado este de la altar, y con ellos ciento veinte sacerdotes tocando cuernos;
Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi.
13 Y cuando los músicos tocaban cuernos, y los que hacían la melodía en una canción, con una sola voz cantaban la alabanza y la gloria del Señor; con voces fuertes y con instrumentos de viento, y con instrumentos de música de bronce y cuerdas, alabando al Señor y diciendo: Él es bueno; Su misericordia es inmutable para siempre: entonces la casa se llenó de la nube de la gloria del Señor.
Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti, “Yehova ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.” Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo,
14 Y los sacerdotes no pudieron guardar sus lugares para hacer su trabajo a causa de la nube; porque la casa de Dios estaba llena de la gloria del Señor.
choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.

< 2 Crónicas 5 >