< 2 Crónicas 36 >

1 Entonces el pueblo de la tierra tomó a Joacaz, hijo de Josías, y lo hizo rey en Jerusalén en lugar de su padre.
Tsono anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namuyika kukhala mfumu mu Yerusalemu mʼmalo mwa abambo ake.
2 Joacaz tenía veintitrés años cuando llegó a ser rey; estuvo gobernando en Jerusalén durante tres meses.
Yowahazi anali wa zaka 23 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu.
3 Entonces el rey de Egipto le arrebató el reino a Jerusalén y puso en la tierra un impuesto de cien talentos de plata y un talento de oro.
Mfumu ya Igupto inamuchotsa pa udindo wa ufumu mu Yerusalemu ndipo inakhometsa msonkho dziko la Yuda wa makilogalamu 3,400 asiliva ndi agolide.
4 Y el rey de Egipto hizo rey a Eliaquim su hermano sobre Judá y Jerusalén, cambiando su nombre por Joacim. Y Necao se llevó a su hermano Joacaz a Egipto.
Mfumu ya Igupto inakhazika Eliyakimu, mʼbale wake wa Yehowahazi kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu ndipo anasintha dzina la Eliyakimu kukhala Yehoyakimu. Koma Neko anatenga Yowahazi mʼbale wake wa Eliyakimu ndi kupita naye ku Igupto.
5 Joacim tenía veinticinco años cuando llegó a ser rey; él gobernó en Jerusalén por once años, e hizo lo malo ante los ojos del Señor su Dios.
Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake.
6 Nabucodonosor, rey de Babilonia, subió contra él y lo llevó encadenado a Babilonia.
Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anachita naye nkhondo ndipo anamumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kumutenga kupita naye ku Babuloni.
7 Nabucodonosor tomó algunos de los vasos de la casa del Señor y los puso en la casa de su dios en Babilonia.
Nebukadinezara anatenganso zipangizo za ku Nyumba ya Yehova kupita nazo ku Babuloni ndipo anaziyika mʼnyumba ya Mulungu wake kumeneko.
8 Ahora, el resto de los actos de Joacim y las cosas repugnantes que hizo, y todo lo que se puede decir contra él, están registrados en el libro de los reyes de Israel y Judá; y Joaquín su hijo se convirtió en rey en su lugar.
Zochitika zina za pa ulamuliro wa Yehoyakimu, zinthu zonyansa zimene anachita ndi zonse zinapezeka kuti zinali zomutsutsa zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 Joaquín tenía dieciocho años cuando llegó a ser rey; estuvo gobernando en Jerusalén durante tres meses y diez días, e hizo lo malo ante los ojos del Señor.
Yehoyakini anali ndi zaka 21 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu ndi masiku khumi. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
10 En la primavera del año, el rey Nabucodonosor mandó que lo llevarán a Babilonia, con los utensilios más valiosos del templo del Señor, e hizo a Sedequías, hermano de su padre, rey de Judá y Jerusalén.
Nthawi ya mphukira, mfumu Nebukadinezara inayitanitsa Yehoyakini ndipo inapita naye ku Babuloni, pamodzi ndi ziwiya zamtengowapatali za mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova, ndipo anayika Zedekiya malume wake kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.
11 Sedequías tenía veintiún años cuando se convirtió en rey; Gobernó en Jerusalén durante once años.
Zedekiya anali ndi zaka 21 pamene ankakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11.
12 Él hizo lo malo ante los ojos del Señor, y no se humilló ante el profeta Jeremías que le dio la palabra del Señor.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake ndipo sanadzichepetse yekha pamaso pa mneneri Yeremiya amene ankayankhula mawu a Yehova.
13 Y tomó las armas contra el rey Nabucodonosor, aunque le había hecho jurar por Dios; pero fue terco y endureció su corazón, apartándose del Señor, el Dios de Israel.
Iye anawukiranso mfumu Nebukadinezara amene anamulumbiritsa mʼdzina la Mulungu. Iyeyo anali wosamva ndipo anawumitsa mtima wake. Sanatembenukire kwa Yehova Mulungu wa Israeli.
14 Y más que esto, todos los grandes hombres de Judá y los sacerdotes y el pueblo hicieron grandes sus pecados, volviéndose a todos los caminos repugnantes de las naciones; y dejaron inmunda la casa del Señor que él había santificado como su santuario en Jerusalén.
Kuwonjezera apo, atsogoleri onse a ansembe ndi anthu ena anapitirapitira kukhala osakhulupirika, kutsatira machitidwe onse onyansa a mitundu ina ndi kudetsa Nyumba ya Yehova Mulungu wawo, imene anayipatula mu Yerusalemu.
15 Y el Señor, el Dios de sus antepasados, les envió un mensaje de parte de sus siervos, advirtiendoles con frecuencia, porque tenía compasión de su pueblo y de su lugar de residencia;
Yehova, Mulungu wa makolo awo, ankatumiza mawu kwa iwo kudzera kwa amithenga ake kawirikawiri, chifukwa ankawamvera chisoni anthu ake ndi malo ake okhalapo.
16 Pero avergonzaron a los siervos de Dios, despreciando sus palabras y riéndose de sus profetas, hasta que la ira de Dios se movió contra su pueblo, hasta que no hubo remedio.
Koma iwo ananyoza amithenga a Mulungu, anapeputsa mawu awo ndipo ankaseka aneneri ake mpaka anawutsa mkwiyo wa Yehova pa anthu ake ndipo panalibenso mankhwala owachiritsa.
17 Entonces envió contra ellos al rey de los caldeos, que mató a espada a sus jóvenes con la espada en el santuario, y no tuvo piedad de ninguno, joven o virgen, anciano, ni inválidos. Dios los dio a todos en sus manos.
Yehova anabweretsa mfumu ya anthu a ku Babuloni, imene inapha anyamata awo ndi lupanga ku malo opatulika, ndipo sanasiye kaya mnyamata kapena mtsikana, wamkulu kapena wokalamba. Mulungu anapereka onsewo kwa Nebukadinezara.
18 Y todos los vasos de la casa de Dios, grandes y pequeños, y la riqueza almacenada de la casa del Señor y la riqueza del rey y sus jefes, se la llevaron a Babilonia.
Iye ananyamula kupita nazo ku Babuloni zipangizo zonse za mʼNyumba ya Yehova Mulungu wawo, zazikulu ndi zazingʼono zomwe, ndi chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso chuma cha mfumu ndi akuluakulu ake.
19 Y la casa de Dios fue quemada y el muro de Jerusalén derribado; Todas sus grandes casas fueron quemadas con fuego y todas sus hermosas vasijas entregadas a la destrucción.
Iwo anayatsa moto Nyumba ya Mulungu, ndipo anagwetsa makoma a Yerusalemu. Anatentha moto nyumba zonse zaufumu ndipo anawononga chilichonse chimene chinali chofunika.
20 Y a todos los que no habían muerto a espada, se los llevaron a Babilonia; y se convirtieron en siervos para él y para sus hijos hasta que el reino de Persia llegó al poder.
Iye anagwira ukapolo anthu otsala amene anapulumuka ku lupanga ndi kupita nawo ku Babuloni, ndipo anakhala antchito ake ndi ana ake mpaka pamene ufumu wa Peresiya unakhazikitsidwa.
21 Para que las palabras del Señor, que él dijo por boca de Jeremías, se hagan realidad, hasta que la tierra haya tenido placer en sus sábados; porque mientras se desperdició, la tierra guardó el sábado, hasta que se cumplieron setenta años.
Dziko linakondwera ndi masabata ake. Pa nthawi yonse ya chipasuko chake nthaka inapuma, mpaka zaka 70 zinakwana pokwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya.
22 En el primer año de Ciro, rey de Persia, para que las palabras que el Señor había dicho por boca de Jeremías se hicieran realidad, el espíritu de Ciro, rey de Persia, fue movido por el Señor, y él hizo una declaración pública y la repartió por todo su reino y la puso por escrito, diciendo:
Mʼchaka choyamba cha Koresi mfumu ya Peresiya, pofuna kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anakhudza mtima wa mfumu ya Peresiya kuti alengeze mu ufumu wake wonse ndipo anazilemba:
23 Ciro, rey de Persia, dijo: El Señor, el Dios del cielo, me ha dado todos los reinos de la tierra; y él me ha hecho responsable de construir una casa para él en Jerusalén, que está en Judá. Quienquiera que haya entre ustedes de todo su pueblo, que el Señor, su Dios, esté con él, váyase allá.
Chimene mfumu Koresi ya Peresiya ikunena ndi ichi: “Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa ine mafumu onse a dziko lapansi ndipo wandisankha kuti ndimumangire Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ku Yuda. Aliyense wa anthu ake pakati panu, Yehova Mulungu wake akhale naye, ndipo apite.”

< 2 Crónicas 36 >