< 2 Crónicas 31 >

1 Ahora que todo esto había terminado, todos los hombres de Israel que estaban presentes salieron a las ciudades de Judá, causando que los pilares de piedra se rompieran y los pilares de madera representaciones de Asera, derribando los lugares altos y los altares en todo Judá y Benjamín, así como en Efraín y Manasés, hasta que todos se fueron. Entonces todos los hijos de Israel volvieron a sus ciudades, cada uno a su propiedad.
Zonse zitatha, Aisraeli onse amene anali kumeneko anapita ku mizinda ya ku Yuda, nakaphwanya miyala yachipembedzo ndi kudula mitengo ya mafano a Asera. Iwo anakawononga malo achipembedzo ndi maguwa ansembe amene anali mʼdziko lonse la Yuda, Benjamini, Efereimu ndi Manase. Atawononga zonsezi, Aisraeli anabwerera ku mizinda yawo ndi ku malo awo.
2 Entonces Ezequías puso en orden los turnos de los sacerdotes y levitas, cada uno en su división, en relación con su servicio, por las ofrendas quemadas y las ofrendas de paz, y por la ordenación de la adoración y por alabar a Dios; y sirvieran en las puertas de la casa del Señor.
Hezekiya anakhazikitsa magulu a ansembe ndi Alevi, gulu lililonse monga mwa ntchito zawo ngati ansembe kapena Alevi, kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, kutumikira, kuyamikira ndi kuyimba matamando pa zipata za ku malo okhala Yehova.
3 Y le dio al rey parte de su propiedad privada por las ofrendas quemadas, es decir, por las ofrendas de la mañana y de la tarde, y las ofrendas para el sábado y las lunas nuevas y las fiestas regulares, como se registra en la ley del Señor.
Kuchokera pa chuma chake, mfumu inapereka nsembe zopsereza za mmawa ndi madzulo ndiponso nsembe zopsereza za pa Chikondwerero cha Masabata, Chikondwerero cha Mwezi Watsopano ndipo inakhazikitsa zikondwerero monga zinalembedwera mʼmalamulo a Yehova.
4 Además, dio órdenes a la gente de Jerusalén para que les dieran a los sacerdotes y levitas la parte que les pertenecía por derecho, para que pudieran ser fuertes en el cumplimiento de la ley del Señor.
Iyo inalamula anthu amene amakhala mu Yerusalemu kupereka gawo lawo kwa ansembe ndi Alevi kuti iwowo adzipereke ku malamulo a Yehova.
5 Y cuando se hizo pública la orden, los hijos de Israel dieron de inmediato, en grandes cantidades, los primeros frutos de su grano y vino y aceite y miel, y del producto de sus campos; y tomaron en una décima parte de todo, una gran cantidad.
Lamuloli atangolilengeza, Aisraeli anapereka mowolowamanja zipatso zoyamba kucha za tirigu, vinyo watsopano, mafuta ndi uchi ndi zonse zomwe nthaka yawo inabereka. Anabweretsa zochuluka kwambiri, chakhumi cha chilichonse.
6 Y los hijos de Israel y Judá, que vivían en las ciudades de Judá, vinieron con la décima parte de sus bueyes y ovejas, y una décima parte de todas las cosas consagradas que debían ser dadas al Señor su Dios, y los pusieron por montones.
Aisraeli ndi Ayuda amene amakhala mʼmizinda ya Yuda anabweretsanso chakhumi cha ngʼombe zawo ndi nkhosa ndi chakhumi cha zinthu zoyera zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wawo, ndipo anaziyika mʼmilumilu.
7 La primera reserva de cosas se dejó en el tercer mes, y en el séptimo mes terminaron.
Anayamba kuchita izi mwezi wachitatu ndipo anatsiriza mwezi wachisanu ndi chiwiri.
8 Y cuando Ezequías y los gobernantes vinieron y vieron toda la reserva de bienes, alabaron al Señor y a su pueblo Israel.
Hezekiya ndi akuluakulu ake atabwera ndi kuona miluyo, anatamanda Yehova ndi kudalitsa anthu ake, Aisraeli.
9 Entonces Ezequías hizo preguntas a los sacerdotes y levitas sobre el almacén de bienes.
Hezekiya anafunsa ansembe ndi Alevi za miluyi;
10 Y Azarías, el principal sacerdote de la familia de Sadoc, dijo en respuesta: Desde el momento en que las personas llegaron por primera vez con sus ofrendas a la casa del Señor, hemos comido lo suficiente, y más que suficiente, porque la bendición del Señor está sobre su pueblo; Y toda esta cantidad a sobrado.
ndipo Azariya, mkulu wa ansembe, ochokera ku banja la Zadoki anayankha kuti, “Kuyambira pamene anthu anayamba kubweretsa zopereka zawo ku Nyumba ya Yehova ife takhala ndi zokwanira kudya ndi zina zambiri zosunga, chifukwa Yehova wadalitsa anthu ake, ndipo mulu umenewu ndiye zotsala.”
11 Entonces Ezequías dijo que los almacenes debían estar listos en la casa del Señor; y esto fue hecho.
Hezekiya analamula kuti akonze zipinda zosungiramo za mʼNyumba ya Yehova, ndipo izi zinachitika.
12 Y en ellos pusieron todas las ofrendas, las décimas y las porciones consagradas, sin guardar nada, y sobre ellos estaba Conanias el levita, y a Simei, su hermano, le siguió.
Ndipo iwo mokhulupirika anabweretsa zopereka, chakhumi ndi mphatso zopatulika. Konaniya Mlevi ndiye amayangʼanira zinthu zimenezi ndipo mʼbale wake Simei ndiye anali wachiwiri wake.
13 Y Jehiel, Azazias, Nahat, Asael y Jerimot y Jozabad y Eliel e Ismaquias, Mahat y Benaía eran supervisores, bajo la dirección de Conanias y Simei su hermano, por orden de Ezequías el rey y Azarías, el gobernante de la casa de Dios.
Yehieli, Azaziya, Nahati, Asaheli, Yerimoti, Yozabadi, Elieli, Isimakiya, Mahati ndi Benaya anali oyangʼanira motsogozedwa ndi Konaniya ndi Simei, mʼbale wake. Iwowa anasankhidwa ndi mfumu Hezekiya ndi Azariya mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu.
14 Y Core, el hijo de Imna el levita, el guardián de la puerta del este, tenía el control de las ofrendas dadas gratuitamente a Dios, y la distribución de las ofrendas del Señor y las porciones consagradas.
Kore mwana wa Imuna Mlevi, mlonda wa Chipata Chakummawa, amayangʼanira zopereka zaufulu kwa Mulungu, ankagawa zopereka za kwa Yehova ndiponso mphatso zopatulika.
15 Y debajo de él estaban Edén y Miniamin y Jesua y Semaías, Amarías y Secanias, en los pueblos de los sacerdotes, quienes se hicieron responsables de dar el reparto de las porciones, por turnos, a pequeños y grandes:
Edeni, Miniyamini, Yesuwa, Semaya, Amariya, Sekaniya amamuthandiza mokhulupirika mʼmizinda yonse a ansembe kugawira kwa ansembe anzawo monga mwa magulu awo, aakulu ndi aangʼono omwe.
16 Así como a todos los varones, de tres años y más, enumerados por sus familias, que entraron en la casa del Señor para hacer lo que se necesitaba día a día, para su trabajo especial con sus turnos.
Kuwonjezera apa, amagawira ana aamuna a zaka zitatu kapena kupitirira amene mayina awo anali mʼmbiri ya mibado yawo, amene adzalowe mʼNyumba ya Yehova kugwira ntchito za tsiku ndi tsiku za magulu awo, molingana ndi udindo ndi magulu awo.
17 Las familias de los sacerdotes fueron nombradas por los nombres de sus padres, pero los levitas, de veinte años en adelante, fueron listados en relación a su servicio en sus turnos;
Ndipo anazigawa kwa ansembe amene analembetsa mayina awo mwa mbiri ya mabanja awo, chimodzimodzinso Alevi amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira molingana ndi udindo wawo ndi magulu awo.
18 Y en las listas estaban todos sus pequeños y sus esposas y sus hijos e hijas, todo la familia, porque se consagraban fielmente a la santidad.
Iwo anaphatikizanso ana onse aangʼono, akazi ndiponso ana aamuna ndi ana aakazi a gulu lonse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado yawo iyi, pakuti anakhulupirika pa kudzipatula okha.
19 Y en cuanto a los hijos de Aarón, los sacerdotes, que viven en el campo en las afueras de sus pueblos, en cada pueblo diferente había hombres, inscritos por su nombre, para dar su parte de los bienes a todos los hombres, entre los sacerdotes, y a todos los que estaban incluidos entre los levitas.
Kunena za ansembe, zidzukulu za Aaroni, amene amakhala mʼminda yozungulira mizinda yawo kapena mzinda wina uliwonse, anthu anasankhidwa mowatchula mayina kuti azipereka magawo kwa munthu wamwamuna aliyense pakati pawo ndiponso kwa onse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado ya Alevi.
20 Esto hizo Ezequías a través de todo Judá; hizo lo que era bueno, correcto y verdadero delante del Señor su Dios.
Izi ndi zimene Hezekiya anachita mu Yuda monse, kuchita zabwino, zolungama ndi zokhulupirika pamaso pa Yehova Mulungu wake.
21 Y por todo lo que hizo, en relación con el servicio del templo de Dios y su ley y sus órdenes, recibió instrucciones de Dios y lo hizo con un propósito serio; Y por eso fue prosperado.
Pa chilichonse chimene anachita pa ntchito ya Nyumba ya Mulungu ndi pa kumvera malangizo ndi malamulo, iye anafunafuna Mulungu wake ndipo anagwira ntchito ndi mtima wake wonse. Ndipo zinthu zimamuyendera bwino.

< 2 Crónicas 31 >