< 1 Samuel 12 >

1 Entonces Samuel dijo a todo Israel: He aquí que he escuchado todo lo que me has dicho, y has hecho un rey sobre ti.
Pambuyo pake Samueli anawuza Aisraeli onse kuti, “Ine ndamvera zonse zimene munandiwuza ndipo ndakupatsani mfumu kuti izikulamulirani.
2 Y ahora, verás, el rey está delante de ti. En cuanto a mi ya estoy viejo y canoso, y mis hijos están contigo. He estado viviendo ante ustedes desde mis primeros días hasta ahora.
Tsopano muli ndi mfumu imene izikutsogolerani, koma ine ndakalamba, kumutu kwanga kuli imvi zokhazokha ndipo ana anga ali pamodzi ndi inu. Ndakhala ndili mtsogoleri wanu kuyambira ndili mnyamata mpaka lero.
3 Aquí estoy. Den testimonio contra mí delante del Señor; delante del hombre sobre quien puso el aceite santo ¿de quién es el buey o asno que he tomado? ¿A quién he sido falso? ¿Quién ha sido oprimido por mí? ¿De qué mano he tomado un precio por el cegamiento de mis ojos? Te lo devolveré todo.
Ine ndili pano. Ngati ndinalakwa chilichonse nditsutseni pamaso pa Yehova ndi wodzozedwa wake. Kodi ndinalanda ngʼombe ya yani? Kodi ndinalanda bulu wa yani? Kodi ndani amene ndinamudyera masuku pa mutu? Kodi ndinazunza yani? Kodi ndinalandira kwa yani chiphuphu choti nʼkundidetsa mʼmaso? Ngati ndinachita chilichonse cha izi, ine ndidzakubwezerani.”
4 Y ellos dijeron: Tú nunca nos has sido falso o cruel con nosotros; No le has quitado nada a ningún hombre.
Iwo anayankha kuti, “Inu simunatidyere masuku pamutu kapena kutizunza. Simunalande kanthu kalikonse ka munthu.”
5 Él les dijo: El Señor es testigo contra ustedes, y el hombre a quien he ungido es testigo hoy que no han visto nada malo en mí. Y dijeron: Así es, él es testigo.
Samueli anawawuza kuti, “Yehova ndiye mboni pakati pa inu ndi ine, ndiponso wodzozedwa wake ndi mboni kuti lero simunapeze chilichonse mʼdzanja langa.” Iwo anati, “Inde, Yehova ndiye mboni.”
6 Entonces Samuel dijo al pueblo: Él Señor es el testigo, que dio autoridad a Moisés y a Aarón, y que sacó a sus padres de la tierra de Egipto.
Samueli anawawuzanso kuti, “Yehova ndiye amene anasankha Mose ndi Aaroni kuti atulutse makolo anu mʼdziko la Igupto.
7 Mantengan sus lugares ahora, mientras abordo la discusión con ustedes ante el Señor y les cuento la historia de la justicia del Señor, que él ha dejado en claro mediante sus actos para ustedes y para sus padres.
Nʼchifukwa chake tsopano imani pomwepa kuti ndikufotokozereni pamaso pa Yehova, za ntchito za chipulumutso zimene Yehova anachitira inu ndi makolo anu.
8 Cuando Jacob y sus hijos llegaron a Egipto y fueron oprimidos por los egipcios, las oraciones de sus padres se acercaron al Señor, y el Señor envió a Moisés y a Aarón, quienes sacaron a sus padres de Egipto, y los puso en este lugar.
“Yakobo atapita ku dziko la Igupto, Aiguptowo akuwazunza, iwo analirira kwa Yehova kuti awathandize, ndipo Yehova anatumiza Mose ndi Aaroni, amene anatulutsa makolo anu mʼdziko la Igupto ndi kudzawakhazika pa malo ano.
9 Pero se olvidaron del Señor su Dios, y él los entregó en manos de Sísara, capitán del ejército de rey de Hazor, y en manos de los filisteos, y en manos del rey de Moab, que hizo la guerra contra ellos.
“Koma iwo anayiwala Yehova Mulungu wawo, choncho Yehova anawapereka mʼdzanja la Sisera mkulu wa ankhondo wa mzinda wa Hazori, ndiponso mʼmanja mwa Afilisti ndi mfumu ya Mowabu. Mafumu onsewa anathira nkhondo makolo anu.
10 Entonces clamando al Señor, dijeron: Hemos hecho lo malo, porque hemos abandonado al Señor, adorando a los baales y astartés: pero ahora, protégenos de los que están contra nosotros y te serviremos solo a ti.
Tsono iwo analira kwa Yehova nati, ‘Ife tachimwa, chifukwa tamusiya Yehova ndi kumatumikira mafano a Baala ndi Asiteroti. Koma tsopano tilanditseni mʼmanja mwa adani athu ndipo tidzakutumikirani.’
11 Entonces el Señor envió a Jerobaal, a Barac, a Jefté, a Samuel, y te sacó del poder de los que luchaban contra ti por todos lados, y vivieron seguros.
Choncho Yehova anatumiza Yeru-Baala, Bedani, Yefita ndi Samueli ndipo anakulanditsani mʼmanja mwa adani anu amene anakuzungulirani, kotero munakhala mwamtendere.
12 Y cuando viste que Nahas, el rey de los amonitas, que venía contra ustedes, me pidieron un rey: No! ¡Queremos un rey para nuestro gobernante! cuando él Señor tu Dios era su rey.
“Koma mutaona kuti Nahasi mfumu ya Amoni inkabwera kudzamenyana nanu, inu munandiwuza kuti, ‘Ayi, ife tikufuna mfumu kuti itilamulire,’ ngakhale kuti Yehova Mulungu wanu ndiye anali mfumu yanu.
13 Aquí, entonces, el rey que han escogido. Él Señor ha puesto un rey que ustedes pidieron.
Tsopano nayi mfumu imene mwayisankha, imene munayipempha. Onani, Yehova wakupatsani mfumu.
14 Si en el temor del Señor son sus siervos, oyen su voz y no van en contra de las órdenes del Señor, sino que son fieles al Señor su Dios, y el rey que gobierna sobre ustedes, entonces harán bien.
Ngati muziopa Yehova ndi kumamutumikira ndi kumamumvera, osamupandukira ndiponso ngati inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Yehova Mulungu wanu, ndiye zinthu zonse zidzakuyenderani bwino.
15 Pero si no escuchas la voz del Señor, sino vas contra sus órdenes, entonces la mano del Señor estará contra ustedes, como lo fue contra sus padres.
Koma mukapanda kumvera Yehova ndi kumupandukira, ndiye adzakulangani pamodzi ndi mfumu yanu yomwe.
16 Ahora, manténgase donde están y vean esta gran cosa que el Señor hará ante sus ojos.
“Tsono imani pomwepa kuti muone chinthu chachikulu chimene Yehova ali pafupi kuchita pamaso panu!
17 ¿No es ahora el momento del corte de grano? Mi clamor subirá al Señor y él enviará truenos y lluvia; para que puedan ver y ser conscientes de su gran pecado que han cometido ante los ojos del Señor al desear un rey para ustedes mismos.
Kodi ino si nthawi yokolola tirigu? Komabe ndipemphera kwa Yehova kuti agwetse mvula ya mabingu. Zikatero mudzadziwa kuti tchimo lanu limene mwachita popempha mfumu kwa Yehova ndi lalikulu.”
18 Entonces Samuel hizo oración al Señor; y él Señor envió truenos y lluvias ese día, y todo el pueblo temía al Señor y a Samuel.
Choncho Samueli anapemphera, ndipo Yehova anatumiza mvula ya mabingu tsiku lomwelo. Apo anthu aja anaopa kwambiri Yehova ndi Samueli.
19 Y todo el pueblo le dijo a Samuel: Ruega al Señor tu Dios para que la muerte no nos alcance; porque además de todos nuestros pecados hemos hecho este mal, al desear un rey.
Tsono anamupempha Samueli nati, “Chonde mutipempherere kwa Yehova, ife atumiki kuti tingafe pakuti pa machimo athu onse tawonjezapo tchimo lopempha mfumu.”
20 Entonces Samuel dijo al pueblo: No teman: en verdad han hecho lo malo, pero no se aparten del Señor; Sean sus siervos con todo su corazón.
Samueli anayankha kuti, “Musaope, inu mwachitadi tchimo ili, koma musaleke kumutsata Yehova ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse.
21 Y no vayas por el camino de aquellos dioses falsos en los que no hay beneficio ni salvación, porque son falsos.
Ndipo musatsate mafano achabechabe amene alibe phindu ndipo sangakupulumutseni popeza ndi achabechabe.
22 Porque el Señor no entregará a su pueblo por el honor de su nombre; porque fue un placer del Señor hacer de ustedes un pueblo para sí mismo.
Yehova adzakana anthu ake kuopa kuti dzina lake lamphamvu linganyozeke, pakuti chinamukondweretsa Yehova kuti akusandutseni inu kukhala anthu ake.
23 Y en cuanto a mí, nunca iré en contra de las órdenes del Señor al renunciar a mis oraciones por ustedes: pero continuaré enseñándoles el camino bueno y correcto.
Ndiponso kunena za ine, zisachitike kuti ndichimwire Yehova pakulephera kukupemphererani. Ndipo ine ndidzakuphunzitsani njira yabwino ndi yolungama kuti muziyendamo.
24 Solo vayan en el temor del Señor y ríndanle culto de todo su corazón, teniendo en cuenta las grandes cosas que ha hecho por ustedes.
Koma onetsetsani kuti mukuopa Yehova ndi kumutumikira mokhulupirika ndi mtima wanu wonse. Nthawi zonse muziganizira zinthu zazikulu wakhala akukuchitirani.
25 Pero si siguen haciendo el mal, la destrucción los alcanzará a ustedes y a su rey.
Komabe mukapitirira kuchita zoyipa, ndiye kuti inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzachotsedwa.”

< 1 Samuel 12 >