< 1 Reyes 1 >

1 Ahora el rey David era viejo y avanzado en años; y aunque lo cubrían con cobijas, su cuerpo estaba frío.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 Entonces sus siervos le dijeron: Busquen una virgen joven para mi señor el rey, para cuidarlo y le sirva; duerma con él y le de calor.
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 Así que, después de buscar en toda la tierra de Israel a una joven hermosa, vieron a Abisag, la sunamita, y la llevaron al rey.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 Ahora ella era muy hermosa; y ella cuidaba al rey, le servía en todo momento; pero el rey no tuvo relaciones con ella.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 Entonces Adonías, hijo de Haguit, se rebeló, dijo: yo seré rey; y alistó sus carruajes de guerra y sus jinetes, con cincuenta corredores por delante.
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6 Ahora, durante toda su vida, su padre nunca fue contra él ni le dijo: ¿Por qué lo has hecho? y era un hombre muy guapo, y más joven que Absalom.
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 Y habló con Joab, hijo de Sarvia, y con el sacerdote Abiatar; y se pusieron de su lado y le dieron su apoyo.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 Pero el sacerdote Sadoc, y Benaía, hijo de Joiada, el profeta Natán y Simei y Rei, y los hombres de guerra de David no se pusieron del lado de Adonías.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 Entonces Adonías mató ovejas y bueyes y bestias gordas por la piedra de Zohelet, de Rogel; y envió a todos sus hermanos, los hijos del rey, y todos los hombres de Judá, los siervos del rey, para que vinieran a él:
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 Pero no envió a buscar al profeta Natán, a Benaía, a los otros hombres de guerra, a su hermano Salomón.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 Entonces Natán dijo a Betsabé, la madre de Salomón: ¿Acaso no ha llegado a tus oídos que Adonías, el hijo de Haguit, se haya hecho rey sin el conocimiento de David nuestro señor?
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 Ahora, permíteme hacer una sugerencia, para que puedas mantener tu vida a salvo y la vida de tu hijo Salomón.
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 Ven ahora, ve al rey David y dile: ¿No me hiciste un juramento a mi siervo, oh señor mío, diciendo: De verdad, tu hijo Salomón será rey después de mí, él subirá al trono de mi reino? ¿Por qué entonces actúa Adonías como rey?
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 Y mientras todavía hablas con el rey, iré detrás de ti y diré que tu historia es verdadera.
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 Entonces Betsabé entró en la habitación del rey; ahora el rey era muy viejo, y Abisag la sunamita le estaba sirviendo.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 Y Betsabé descendió sobre su rostro en el suelo delante del rey, dándole honor. Y él dijo: ¿Cuál es tu deseo?
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 Y ella le dijo: Señor, tú hiciste un juramento al Señor tu Dios, y diste tu palabra a tu sierva, diciendo: De verdad, tu hijo Salomón será rey después de mí, subirá al trono de mi Reino.
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 Y ahora, mira, Adonías se ha hecho a sí mismo rey sin el conocimiento de mi señor;
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 Y ha dado muerte a los bueyes y las bestias gordas y ovejas en gran número, y ha enviado a todos los hijos del rey, al sacerdote Abiatar y a Joab, el capitán del ejército; mas no ha invitado a tu siervo Salomón.
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 Y ahora, mi señor el rey, los ojos de todo Israel están sobre ti, esperando que digas quién va a ocupar el lugar de mi señor el rey después de él.
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 Pues sucederá, en cuanto mi señor el rey duerma con sus padres, yo y mi hijo Salomón seremos condenados a muerte.
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 Y mientras ella seguía hablando con el rey, entró el profeta Natán.
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 Y dijeron al rey: Aquí está el profeta Natán. Y cuando entró ante el rey, se postró sobre el suelo.
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 Y Natán dijo: Rey señor mío, ¿has dicho: Adonías será rey después de mí, sentado en el trono de mi reino?
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 Porque hoy ha bajado y ha matado bueyes, bestias gordas y ovejas en gran número, y ha enviado a todos los hijos del rey para que vengan a él, con los capitanes del ejército y el sacerdote Abiatar; y están festejando delante de él y gritando: ¡Larga vida al rey Adonías!
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 Pero yo, tu siervo, y el sacerdote Sadoc, y Benaía, hijo de Joiada, y tu siervo Salomón, él no nos ha invitado.
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 ¿Ha hecho esto mi señor el rey, sin avisar a sus siervo quien debía ser colocado en el trono de mi señor el rey después de él?
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 Entonces el rey David, en respuesta, dijo: Envía a Betsabé a venir a mí. Y ella entró y tomó su lugar delante del rey.
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 Entonces el rey hizo un juramento y dijo: Por el Señor vivo, que ha sido mi salvador de todos mis problemas,
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
30 Cuando te juré por el Señor, el Dios de Israel, diciendo: Ciertamente, tu hijo Salomón se hará rey después de mí, sentado en mi lugar en mi trono; Así lo haré este día.
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 Entonces Betsabé descendió sobre su rostro al suelo, haciendo reverencia al rey, y dijo: Que mi señor, el rey David, siga viviendo para siempre.
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 Y el rey David dijo: Llama al sacerdote Sadoc, al profeta Natán y a Benaía, hijo de Joiada. Y vinieron delante del rey.
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 Y el rey les dijo: Toma contigo a los siervos de tu señor, y pon a mi hijo Salomón en mi mula, y llévalo a Gihón;
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 Dejen que el sacerdote Sadoc y el profeta Natán ungirán con aceite santo sobre él para hacerle rey sobre Israel; y al sonar la bocina digan: ¡Larga vida al rey Salomón!
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 Luego, suban tras él, y él entrará y tomará su lugar en el trono de mi reino; porque él debe ser rey en mi lugar, y yo he ordenado que él sea gobernante sobre Israel y sobre Judá.
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 Y Benaía, hijo de Joiada, respondiendo al rey, dijo: Así sea: y que el Señor, el Dios de mi señor el rey, lo diga.
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 Como el Señor ha estado con mi señor el rey, así puede estar con Salomón y hacer que el trono de su autoridad sea mayor que el de mi señor el rey David.
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 Entonces el sacerdote Sadoc, y el profeta Natán, y Benaía, hijo de Joiada, y los cereteos y los peleteos, descendieron y pusieron a Salomón sobre la mula del rey David y lo llevaron a Gihón.
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 Entonces el sacerdote Sadoc tomó el cuerno de aceite del santuario y ungió con aceite santo a Salomón. Y cuando sonó el cuerno, todas las personas dijeron: ¡Larga vida al rey Salomón!
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 Y todo el pueblo subió tras él, tocando flautas, y se alegraron con gran alegría, y la tierra se estremeció con el sonido.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 Y llegó a oídos de Adonías y de todos los invitados que estaban con él cuando terminaron de comer. Y Joab, al oír el sonido del cuerno, dijo: ¿Cuál es la razón de este ruido en la ciudad?
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 Y mientras las palabras estaban en sus labios, vino Jonatán, hijo del sacerdote Abiatar; Y Adonías dijo: Entra; Porque eres un hombre de buena fe y las noticias que tienes para nosotros serán buenas.
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 Y respondiendo Jonatán, dijo a Adonías: No es así, pero nuestro señor el rey David ha hecho rey a Salomón:
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 Y él envió con él al sacerdote Sadoc, al profeta Natán, a Benaía, hijo de Joiada, a los cereteos y a los peleteos; Y lo pusieron sobre la mula del rey.
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 Entonces el sacerdote Sadoc y el profeta Natán lo ungieron con aceite santo y lo hicieron rey en Gihón; y volvieron de allí con alegría, y la ciudad estaba toda alborotada. Este es el ruido que ha llegado a tus oídos.
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 Y ahora Salomón está sentado en el trono del reino.
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 Y los siervos del rey se acercaron a nuestro señor el rey David, bendiciéndolo y diciendo: Que Dios haga el nombre de Salomón mejor que tu nombre, y el trono de su autoridad mayor que tu trono; y el rey se inclinó para adorar en su cama.
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 Entonces el rey dijo: Alabado sea el Dios de Israel, que ha dado a uno de mi descendencia como rey en mi lugar este día y ha dejado que mis ojos lo vean.
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 Y todos los invitados de Adonías se levantaron temerosos y se fueron, cada uno por su lado.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 Y Adonías estaba lleno de temor por causa de Salomón; Se levantó y fue al altar, y se puso las manos en los cuernos.
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 Y le dieron a Salomón una palabra, diciendo: Mira, Adonías teme tanto al rey Salomón, que ha puesto sus manos sobre los cuernos del altar, diciendo: Que el rey Salomón primero me dé su juramento de que no matará a espada a su siervo.
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 Y Salomón dijo: Si se ve que es un hombre de buena fe, ninguno de sus cabellos será tocado; pero si se ve algún delito en él, debe ser ejecutado.
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 Envió, pues, el rey Salomón, y lo bajaron del altar. Y vino y dio honor al rey Salomón; Y Salomón le dijo: Ve a tu casa.
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

< 1 Reyes 1 >