< Salmos 76 >
1 Al Músico principal: sobre Neginoth: Salmo de Asaph: Canción. DIOS es conocido en Judá: en Israel es grande su nombre.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 Y en Salem está su tabernáculo, y su habitación en Sión.
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 Allí quebró las saetas del arco, el escudo, y la espada, y [tren] de guerra. (Selah)
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
4 Ilustre eres tú; fuerte, más que los montes de caza.
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 Los fuertes de corazón fueron despojados, durmieron su sueño; y nada hallaron en sus manos todos los varones fuertes.
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
6 A tu reprensión, oh Dios de Jacob, el carro y el caballo fueron entorpecidos.
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
7 Tú, terrible eres tú: ¿y quién parará delante de ti, en comenzando tu ira?
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
8 Desde los cielos hiciste oir juicio; la tierra tuvo temor y quedó suspensa,
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
9 Cuando te levantaste, oh Dios, al juicio, para salvar á todos los mansos de la tierra. (Selah)
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
10 Ciertamente la ira del hombre te acarreará alabanza: tú reprimirás el resto de las iras.
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 Prometed, y pagad á Jehová vuestro Dios: todos los que están alrededor de él, traigan presentes al Terrible.
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 Cortará él el espíritu de los príncipes: terrible es á los reyes de la tierra.
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.