< Salmos 145 >

1 Salmo de alabanza: de David. ENSALZARTE he, mi Dios, mi Rey; y bendeciré tu nombre por siglo y para siempre.
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Cada día te bendeciré, y alabaré tu nombre por siglo y para siempre.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Grande es Jehová y digno de suprema alabanza: y su grandeza es inescrutable.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Generación á generación narrará tus obras, y anunciarán tus valentías.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 La hermosura de la gloria de tu magnificencia, y tus hechos maravillosos, hablaré.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 Y la terribilidad de tus valentías dirán los hombres; y yo recontaré tu grandeza.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Reproducirán la memoria de la muchedumbre de tu bondad, y cantarán tu justicia.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 Clemente y misericordioso es Jehová, lento para la ira, y grande en misericordia.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 Bueno es Jehová para con todos; y sus misericordias sobre todas sus obras.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Alábente, oh Jehová, todas tus obras; y tus santos te bendigan.
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 La gloria de tu reino digan, y hablen de tu fortaleza;
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 Para notificar á los hijos de los hombres sus valentías, y la gloria de la magnificencia de su reino.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Tu reino es reino de todos los siglos, y tu señorío en toda generación y generación.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Sostiene Jehová á todos los que caen, y levanta á todos los oprimidos.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Los ojos de todos esperan en ti, y tú les das su comida en su tiempo.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Abres tu mano, y colmas de bendición á todo viviente.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 Justo es Jehová en todos sus caminos, y misericordioso en todas sus obras.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Cercano está Jehová á todos los que le invocan, á todos los que le invocan de veras.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Cumplirá el deseo de los que le temen; oirá asimismo el clamor de ellos, y los salvará.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Jehová guarda á todos los que le aman; empero destruirá á todos los impíos.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 La alabanza de Jehová hablará mi boca; y bendiga toda carne su santo nombre por siglo y para siempre.
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.

< Salmos 145 >