< Salmos 112 >
1 Aleluya. BIENAVENTURADO el hombre que teme á Jehová, [y] en sus mandamientos se deleita en gran manera.
Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 Su simiente será poderosa en la tierra: la generación de los rectos será bendita.
Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3 Hacienda y riquezas hay en su casa; y su justicia permanece para siempre.
Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Resplandeció en las tinieblas luz á los rectos: [es] clemente, y misericordioso, y justo.
Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5 El hombre de bien tiene misericordia y presta; gobierna sus cosas con juicio.
Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6 Por lo cual no resbalará para siempre: en memoria eterna será el justo.
Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7 De mala fama no tendrá temor: su corazón está apercibido, confiado en Jehová.
Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8 Asentado está su corazón, no temerá, hasta que vea en sus enemigos [su deseo].
Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9 Esparce, da á los pobres: su justicia permanece para siempre; su cuerno será ensalzado en gloria.
Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10 Verálo el impío, y se despechará; crujirá los dientes, y se repudrirá: perecerá el deseo de los impíos.
Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.