< Salmos 109 >

1 Al Músico principal: Salmo de David. OH Dios de mi alabanza, no calles;
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 Porque boca de impío y boca de engañador se han abierto sobre mí: han hablado de mí con lengua mentirosa,
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 Y con palabras de odio me rodearon; y pelearon contra mí sin causa.
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 En pago de mi amor me han sido adversarios: mas yo oraba.
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 Y pusieron contra mí mal por bien, y odio por amor.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 Pon sobre él al impío: y Satán esté á su diestra.
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 Cuando fuere juzgado, salga impío; y su oración sea para pecado.
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 Sean sus días pocos: tome otro su oficio.
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 Sean sus hijos huérfanos, y su mujer viuda.
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Y anden sus hijos vagabundos, y mendiguen; y procuren [su pan lejos] de sus desolados hogares.
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Enrede el acreedor todo lo que tiene, y extraños saqueen su trabajo.
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 No tenga quien le haga misericordia; ni haya quien tenga compasión de sus huérfanos.
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Su posteridad sea talada; en segunda generación sea raído su nombre.
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Venga en memoria cerca de Jehová la maldad de sus padres, y el pecado de su madre no sea borrado.
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Estén siempre delante de Jehová, y él corte de la tierra su memoria.
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 Por cuanto no se acordó de hacer misericordia, y persiguió al hombre afligido y menesteroso y quebrantado de corazón, para matar[lo].
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 Y amó la maldición, y vínole; y no quiso la bendición, y ella se alejó de él.
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 Y vistióse de maldición como de su vestido, y entró como agua en sus entrañas, y como aceite en sus huesos.
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 Séale como vestido con que se cubra, y en lugar de cinto con que se ciña siempre.
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Este sea el pago de parte de Jehová de los que me calumnian, y de los que hablan mal contra mi alma.
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 Y tú, Jehová Señor, haz conmigo por amor de tu nombre: líbrame, porque tu misericordia es buena.
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 Porque yo estoy afligido y necesitado; y mi corazón está herido dentro de mí.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Voime como la sombra cuando declina; soy sacudido como langosta.
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 Mis rodillas están debilitadas á causa del ayuno, y mi carne desfallecida por falta de gordura.
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Yo he sido para ellos objeto de oprobio; mirábanme, y meneaban su cabeza.
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Ayúdame, Jehová Dios mío: sálvame conforme á tu misericordia.
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 Y entiendan que esta es tu mano; [que] tú, Jehová, has hecho esto.
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Maldigan ellos, y bendice tú: levántense, mas sean avergonzados, y regocíjese tu siervo.
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Sean vestidos de ignominia los que me calumnian; y sean cubiertos de su confusión como con manto.
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 Yo alabaré á Jehová en gran manera con mi boca, y le loaré en medio de muchos.
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 Porque él se pondrá á la diestra del pobre, para librar su alma de los que le juzgan.
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

< Salmos 109 >