< Salmos 105 >

1 ALABAD á Jehová, invocad su nombre: haced notorias sus obras en los pueblos.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Cantadle, cantadle salmos: hablad de todas sus maravillas.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Gloriaos en su santo nombre: alégrese el corazón de los que buscan á Jehová.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Buscad á Jehová, y su fortaleza: buscad siempre su rostro.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Acordaos de sus maravillas que hizo, de sus prodigios y de los juicios de su boca,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 Oh vosotros, simiente de Abraham su siervo, hijos de Jacob, sus escogidos.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 El es Jehová nuestro Dios; en toda la tierra son sus juicios.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Acordóse para siempre de su alianza; de la palabra que mandó para mil generaciones,
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 La cual concertó con Abraham; y de su juramento á Isaac.
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 Y establecióla á Jacob por decreto, á Israel por pacto sempiterno,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 Diciendo: A ti daré la tierra de Canaán [por] cordel de vuestra heredad.
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 [Esto] siendo ellos pocos hombres en número, y extranjeros en ella.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 Y anduvieron de gente en gente, de un reino á otro pueblo.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 No consintió que hombre los agraviase; y por causa de ellos castigó los reyes.
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 No toquéis, [dijo], á mis ungidos, ni hagáis mal á mis profetas.
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Y llamó al hambre sobre la tierra, y quebrantó todo mantenimiento de pan.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Envió un varón delante de ellos, á José, [que] fué vendido por siervo.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 Afligieron sus pies con grillos; en hierro fué puesta su persona.
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 Hasta la hora que llegó su palabra, el dicho de Jehová le probó.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Envió el rey, y soltóle; el señor de los pueblos, y desatóle.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Púsolo por señor de su casa, y por enseñoreador en toda su posesión;
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 Para que reprimiera á sus grandes como él quisiese, y á sus ancianos enseñara sabiduría.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Después entró Israel en Egipto, y Jacob fué extranjero en la tierra de Châm.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Y multiplicó su pueblo en gran manera, é hízolo fuerte más que sus enemigos.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Volvió el corazón de ellos para que aborreciesen á su pueblo, para que contra sus siervos pensasen mal.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Envió á su siervo Moisés, [y] á Aarón al cual escogió.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Pusieron en ellos las palabras de sus señales, y sus prodigios en la tierra de Châm.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Echó tinieblas, é hizo oscuridad; y no fueron rebeldes á su palabra.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Volvió sus aguas en sangre, y mató sus pescados.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Produjo su tierra ranas, [aun] en las cámaras de sus reyes.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Dijo, y vinieron enjambres de moscas, y piojos en todo su término.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Volvió en su tierra sus lluvias en granizo, [y] en fuego de llamaradas.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 E hirió sus viñas y sus higueras, y quebró los árboles de su término.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Dijo, y vinieron langostas, y pulgón sin número;
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 Y comieron toda la hierba de su país, y devoraron el fruto de su tierra.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 Hirió además á todos los primogénitos en su tierra, el principio de toda su fuerza.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Y sacólos con plata y oro; y no hubo en sus tribus enfermo.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Egipto se alegró de que salieran; porque su terror había caído sobre ellos.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Extendió una nube por cubierta, y fuego para alumbrar la noche.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 Pidieron, é hizo venir codornices; y saciólos de pan del cielo.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Abrió la peña, y fluyeron aguas; corrieron por los secadales [como] un río.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 Porque se acordó de su santa palabra, [dada] á Abraham su siervo.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 Y sacó á su pueblo con gozo; con júbilo á sus escogidos.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 Y dióles las tierras de las gentes; y las labores de las naciones heredaron:
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 Para que guardasen sus estatutos, y observasen sus leyes. Aleluya.
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Salmos 105 >