< Proverbios 9 >

1 LA sabiduría edificó su casa, labró sus siete columnas;
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 Mató sus víctimas, templó su vino, y puso su mesa.
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 Envió sus criadas; sobre lo más alto de la ciudad clamó:
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 Cualquiera simple, venga acá. A los faltos de cordura dijo:
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 Venid, comed mi pan, y bebed del vino que yo he templado.
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 Dejad las simplezas, y vivid; y andad por el camino de la inteligencia.
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
7 El que corrige al escarnecedor, afrenta se acarrea: el que reprende al impío, se [atrae] mancha.
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
8 No reprendas al escarnecedor, porque no te aborrezca; corrige al sabio, y te amará.
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
9 Da al sabio, y será más sabio: enseña al justo, y acrecerá su saber.
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
10 El temor de Jehová es el principio de la sabiduría; y la ciencia de los santos es inteligencia.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
11 Porque por mí se aumentarán tus días, y años de vida se te añadirán.
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
12 Si fueres sabio, para ti lo serás: mas si fueres escarnecedor, pagarás tú solo.
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
13 La mujer loca es alborotadora; [es] simple é ignorante.
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
14 Siéntase en una silla á la puerta de su casa, en lo alto de la ciudad,
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
15 Para llamar á los que pasan por el camino, que van por sus caminos derechos.
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
16 Cualquiera simple, [dice], venga acá. A los faltos de cordura dijo:
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
17 Las aguas hurtadas son dulces, y el pan [comido] en oculto es suave.
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
18 Y no saben que allí están los muertos; que sus convidados están en los profundos de la sepultura. (Sheol h7585)
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol h7585)

< Proverbios 9 >